< איוב 36 >
Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:
כתר-לי זעיר ואחוך כי עוד לאלוה מלים | 2 |
“Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
אשא דעי למרחוק ולפעלי אתן-צדק | 3 |
Nzeru zanga ndimazitenga kutali; ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
כי-אמנם לא-שקר מלי תמים דעות עמך | 4 |
Ndithudi mawu anga si abodza; wanzeru zangwiro ali ndi inu.
הן-אל כביר ולא ימאס כביר כח לב | 5 |
“Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu; Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
לא-יחיה רשע ומשפט עניים יתן | 6 |
Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
לא-יגרע מצדיק עיניו ואת-מלכים לכסא וישיבם לנצח ויגבהו | 7 |
Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama; amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
ואם-אסורים בזקים ילכדון בחבלי-עני | 8 |
Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo, ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
ויגד להם פעלם ופשעיהם כי יתגברו | 9 |
Iye amawafotokozera zomwe anachita, kuti iwo anachimwa modzikuza.
ויגל אזנם למוסר ויאמר כי-ישובון מאון | 10 |
Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
אם-ישמעו ויעבדו יכלו ימיהם בטוב ושניהם בנעימים | 11 |
Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira, adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere, adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
ואם-לא ישמעו בשלח יעברו ויגועו בבלי-דעת | 12 |
Koma ngati samvera, adzaphedwa ndi lupanga ndipo adzafa osadziwa kanthu.
וחנפי-לב ישימו אף לא ישועו כי אסרם | 13 |
“Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo; akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
תמת בנער נפשם וחיתם בקדשים | 14 |
Amafa akanali achinyamata, pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
יחלץ עני בעניו ויגל בלחץ אזנם | 15 |
Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo; Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.
ואף הסיתך מפי-צר-- רחב לא-מוצק תחתיה ונחת שלחנך מלא דשן | 16 |
“Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso, kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani, kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
ודין-רשע מלאת דין ומשפט יתמכו | 17 |
Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu; chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
כי-חמה פן-יסיתך בספק ורב-כפר אל-יטך | 18 |
Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma; musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
היערך שועך לא בצר וכל מאמצי-כח | 19 |
Kodi chuma chanu kapena mphamvu zanu zonse zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
אל-תשאף הלילה-- לעלות עמים תחתם | 20 |
Musalakalake kuti usiku ubwere, pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
השמר אל-תפן אל-און כי-על-זה בחרת מעני | 21 |
Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo, chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.
הן-אל ישגיב בכחו מי כמהו מורה | 22 |
“Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu. Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
מי-פקד עליו דרכו ומי-אמר פעלת עולה | 23 |
Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite, kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
זכר כי-תשגיא פעלו-- אשר שררו אנשים | 24 |
Kumbukirani kutamanda ntchito zake zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
כל-אדם חזו-בו אנוש יביט מרחוק | 25 |
Anthu onse amaziona ntchitozo; anthuwo amaziona ali kutali.
הן-אל שגיא ולא נדע מספר שניו ולא-חקר | 26 |
Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe! Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.
כי יגרע נטפי-מים יזקו מטר לאדו | 27 |
“Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo, timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
אשר-יזלו שחקים ירעפו עלי אדם רב | 28 |
mitambo imagwetsa mvulayo ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
אף אם-יבין מפרשי-עב תשאות סכתו | 29 |
Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera, momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
הן-פרש עליו אורו ושרשי הים כסה | 30 |
Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse, zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
כי-בם ידין עמים יתן-אכל למכביר | 31 |
Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
על-כפים כסה-אור ויצו עליה במפגיע | 32 |
Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani, ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
יגיד עליו רעו מקנה אף על-עולה | 33 |
Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho; ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.