< איוב 28 >
כי יש לכסף מוצא ומקום לזהב יזקו | 1 |
Pali mgodi wa siliva ndiponso malo oyengerapo golide.
ברזל מעפר יקח ואבן יצוק נחושה | 2 |
Chitsulo amachikumba pansi, ndipo mkuwa amawusungunula ku miyala yamkuwa.
קץ שם לחשך ולכל-תכלית הוא חוקר אבן אפל וצלמות | 3 |
Munthu amalowa mu mdima atatenga nyale, amafunafuna miyala mpaka ku malire a mgodiwo, kufuna mkuwa mu mdima wandiweyani.
פרץ נחל מעם-גר--הנשכחים מני-רגל דלו מאנוש נעו | 4 |
Amakumba njira zapansi mu mgodimo, kutali ndi kumene kumakhala anthu, kumalo kumene phazi la munthu silinapondeko; iye amakhala ali lende pansipo namazungulira uku ndi uku.
ארץ--ממנה יצא-לחם ותחתיה נהפך כמו-אש | 5 |
Nthaka, imene imatulutsa zakudya, kunsi kwake kumachita ngati kwasandulizika ndi moto;
מקום-ספיר אבניה ועפרת זהב לו | 6 |
miyala ya safiro imachokera mʼmatanthwe ake, ndipo mʼfumbi lake mumakhala miyala yagolide.
נתיב לא-ידעו עיט ולא שזפתו עין איה | 7 |
Palibe mbalame yodya zinzake imene imadziwa njira yobisikayi, palibe kamtema amene anayiona.
לא-הדריכוהו בני-שחץ לא-עדה עליו שחל | 8 |
Zirombo zolusa sizipondamo mʼnjiramo, ndipo mkango sudzeranso mʼmenemo.
בחלמיש שלח ידו הפך משרש הרים | 9 |
Munthu amaphwanya matanthwe olimba, ndipo amagubuduza mapiri kuyambira mʼtsinde.
בצורות יארים בקע וכל-יקר ראתה עינו | 10 |
Amabowola njira mʼmatanthwewo; ndipo amaona chuma chonse cha mʼphirimo.
מבכי נהרות חבש ותעלמה יצא אור | 11 |
Amaletsa mitsinje ya pansipo kuti isayendenso, motero amatulutsira poyera zinthu zobisika.
והחכמה מאין תמצא ואי זה מקום בינה | 12 |
“Koma nzeru zingapezeke kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
לא-ידע אנוש ערכה ולא תמצא בארץ החיים | 13 |
Munthu sadziwa kufunika kwake kwa nzeruzo; nzeruyo sipezeka pa dziko lino la anthu amoyo.
תהום אמר לא בי-היא וים אמר אין עמדי | 14 |
Phompho likuti, ‘Sizipezeka mwa ine muno.’ Nyanja ikuti, ‘Mwa ine munonso ayi.’
לא-יתן סגור תחתיה ולא ישקל כסף מחירה | 15 |
Nzeru sungazigule ndi golide wabwino kwambiri, mtengo wake sungawuyerekeze ndi siliva wambiri.
לא-תסלה בכתם אופיר בשהם יקר וספיר | 16 |
Nzeru singagulidwe ndi golide wa ku Ofiri, kapena ndi miyala ya onikisi kapena ya safiro.
לא-יערכנה זהב וזכוכית ותמורתה כלי-פז | 17 |
Nzeru sungayiyerekeze ndi golide kapena mwala wa galasi, sungayigule ndi zokometsera zagolide.
ראמות וגביש לא יזכר ומשך חכמה מפנינים | 18 |
Miyala ya korali ndi krisitali siyoyeneranso ndi kuyitchula nʼkomwe; mtengo wa nzeru ndi woposa miyala ya rubi.
לא-יערכנה פטדת-כוש בכתם טהור לא תסלה | 19 |
Nzeru sungayiyerekeze ndi miyala ya topazi ya ku Kusi; nzeru singagulidwe ndi golide wabwino kwambiri.
והחכמה מאין תבוא ואי זה מקום בינה | 20 |
“Kodi tsono nzeru zimachokera kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
ונעלמה מעיני כל-חי ומעוף השמים נסתרה | 21 |
Malo ake ndi obisika kwa zamoyo zonse, ndi obisika ngakhale kwa mbalame zamlengalenga.
אבדון ומות אמרו באזנינו שמענו שמעה | 22 |
Chiwonongeko ndi imfa zikuti, ‘Tangomva mphekesera chabe ya zimenezo!’
אלהים הבין דרכה והוא ידע את-מקומה | 23 |
Mulungu yekha ndiye amadziwa njira yake yopita kumeneko, ndipo Iye yekha amadziwa kumene nzeru imakhala,
כי-הוא לקצות-הארץ יביט תחת כל-השמים יראה | 24 |
pakuti Iye amayangʼana mpaka ku malekezero a dziko lapansi ndipo amaona zonse za kunsi kwa thambo.
לעשות לרוח משקל ומים תכן במדה | 25 |
Iye atapatsa mphepo mphamvu zake, nayeza kuzama kwa nyanja,
בעשתו למטר חק ודרך לחזיז קלות | 26 |
atakhazikitsa lamulo loti mvula izigwa ndi kukonza njira ya chingʼaningʼani cha bingu,
אז ראה ויספרה הכינה וגם-חקרה | 27 |
pamenepo ndi pamene anayangʼana nzeruzo naziyeza mtengo wake; nazikhazikitsa ndi kuzisanthula bwino lomwe.
ויאמר לאדם--הן יראת אדני היא חכמה וסור מרע בינה | 28 |
Ndipo Iye anati kwa munthu, ‘Taonani, kuopa Ambuye, ndiye nzeru zimenezo ndipo kuthawa zoyipa ndiye kumvetsa zinthu kumeneko.’”