< איוב 24 >

מדוע--משדי לא-נצפנו עתים וידעו לא-חזו ימיו 1
“Chifukwa chiyani Wamphamvuzonse sayikiratu nthawi yoti aweruze? Chifukwa chiyani iwo amene amadziwa Iyeyo amayembekezera pachabe masiku oterewa?
גבלות ישיגו עדר גזלו וירעו 2
Anthu amasuntha miyala ya mʼmalire, kuti akuze dziko lawo; amadyetsa ziweto zimene aba.
חמור יתומים ינהגו יחבלו שור אלמנה 3
Amalanda abulu a ana amasiye ndipo amatenganso ngʼombe ya mkazi wamasiye ngati chikole.
יטו אבינים מדרך יחד חבאו עניי-ארץ 4
Amachotsa mʼmisewu anthu osauka, ndipo amathamangitsa amphawi onse mʼdziko.
הן פראים במדבר-- יצאו בפעלם משחרי לטרף ערבה לו לחם לנערים 5
Amphawiwo amakhala ngati mbidzi mʼchipululu, amayendayenda kufuna chakudya; dziko lowuma limapereka chakudya cha ana awo.
בשדה בלילו יקצירו (יקצורו) וכרם רשע ילקשו 6
Iwo amakolola za mʼminda ya eni ake, ndipo amakunkha mphesa mʼminda ya anthu oyipa.
ערום ילינו מבלי לבוש ואין כסות בקרה 7
Amagona maliseche usiku wonse kusowa zovala; pa nthawi yozizira amasowa chofunda.
מזרם הרים ירטבו ומבלי מחסה חבקו-צור 8
Amavumbwa ndi mvula ya mʼmapiri ndipo amakangamira ku matanthwe kusowa pobisalapo.
יגזלו משד יתום ועל-עני יחבלו 9
Amatsomphola mwana wamasiye wa ku bere; ndipo amagwira mwana wakhanda wa mʼmphawi kuti akhale chikole.
ערום הלכו בלי לבוש ורעבים נשאו עמר 10
Amphawi amangoyenda maliseche kusowa zovala; amasenza mitolo ya tirigu, koma nʼkumagonabe ndi njala.
בין-שורתם יצהירו יקבים דרכו ויצמאו 11
Iwo amayenga mafuta a olivi mʼminda ya anthu oyipa; amapsinya mphesa, koma nʼkumamvabe ludzu.
מעיר מתים ינאקו-- ונפש-חללים תשוע ואלוה לא-ישים תפלה 12
Kubuwula kwa anthu amene akufa kumamveka kuchokera mu mzinda, anthu ovulala akulirira chithandizo. Koma Mulungu sakuyimba mlandu wina aliyense.
המה היו--במרדי-אור לא-הכירו דרכיו ולא ישבו בנתיבתיו 13
“Pali ena amene amakana kuwala, amene safuna kuyenda mʼkuwalako kapena kukhala mʼnjira zake.
לאור יקום רוצח--יקטל-עני ואביון ובלילה יהי כגנב 14
Dzuwa likalowa, wopha anzake amadzuka ndipo amakapha osauka ndi amphawi; nthawi ya usiku iye amasanduka mbala.
ועין נאף שמרה נשף לאמר-- לא-תשורני עין וסתר פנים ישים 15
Munthu wachigololo amadikira chisisira; iyeyo amaganiza kuti, ‘Palibe amene akundiona,’ ndipo amaphimba nkhope yake.
חתר בחשך בתים יומם חתמו-למו לא-ידעו אור 16
Mbala zimathyola nyumba usiku, koma masana zimadzitsekera; izo zimathawa kuwala.
כי יחדו בקר למו צלמות כי-יכיר בלהות צלמות 17
Pakuti kwa onsewa mdima wandiweyani ndiye kuti kwawachera. Iwo amachita ubale ndi zoopsa za mdima.
קל-הוא על-פני-מים-- תקלל חלקתם בארץ לא-יפנה דרך כרמים 18
“Komatu iwowo ndi thovu loyandama pa madzi; minda yawo ndi yotembereredwa pa dzikolo kotero kuti palibe amene amapita ku minda ya mpesa.
ציה גם-חם יגזלו מימי-שלג שאול חטאו (Sheol h7585) 19
Monga momwe kutentha ndi chilala zimasungunulira madzi owundana ndi momwemonso mmene manda amachotsera omwe achimwa. (Sheol h7585)
ישכחהו רחם מתקו רמה-- עוד לא-יזכר ותשבר כעץ עולה 20
Mayi wowabereka amawayiwala, mphutsi zimasangalala powadya; anthu oyipa sakumbukiridwanso koma amathyoka ngati mtengo.
רעה עקרה לא תלד ואלמנה לא ייטיב 21
Amachitira nkhanza mayi wosabala ndi mayi amene alibe mwana, ndipo sakomera mtima mkazi wamasiye.
ומשך אבירים בכחו יקום ולא-יאמין בחיין 22
Koma Mulungu amawononga munthu wamphamvu mwa mphamvu zake; ngakhale munthuyo atakhazikika, alibe chiyembekezo cha moyo wake.
יתן-לו לבטח וישען ועיניהו על-דרכיהם 23
Mulungu atha kuwalola kuti akhale mosatekeseka, koma amakhala akupenyetsetsa njira zawo.
רומו מעט ואיננו והמכו ככל יקפצון וכראש שבלת ימלו 24
Kwa kanthawi kochepa oyipa amakwezedwa ndipo kenaka saonekanso; amatsitsidwa ndipo amachotsedwa monga ena onse; amadulidwa ngati ngala za tirigu.
ואם-לא אפו מי יכזיבני וישם לאל מלתי 25
“Ngati zimenezi sizoona, ndani angaonetse kuti ndine wabodza ndi kusandutsa mawu anga kukhala wopanda pake?”

< איוב 24 >