< איוב 22 >
Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
הלאל יסכן-גבר-- כי-יסכן עלימו משכיל | 2 |
“Kodi munthu nʼkukhala waphindu kwa Mulungu? Kodi munthu wanzeru angamupindulire Iye?
החפץ לשדי כי תצדק ואם-בצע כי-תתם דרכיך | 3 |
Kodi Wamphamvuzonse akanapeza chabwino chotani iweyo ukanakhala wolungama? Kodi iyeyo akanapeza phindu lanji makhalidwe ako akanakhala angwiro?
המיראתך יכיחך יבוא עמך במשפט | 4 |
“Kodi nʼchifukwa choti umamuopa, kuti azikudzudzula, kuti azifuna kukukokera ku mlandu?
הלא רעתך רבה ואין-קץ לעונתיך | 5 |
Kodi osati nʼchifukwa chakuti kuyipa kwako nʼkwakukulu? Kodi machimo ako si opanda malire?
כי-תחבל אחיך חנם ובגדי ערומים תפשיט | 6 |
Iwe unkawumiriza abale ako kuti akupatse chikole popanda chifukwa; umalanda anthu zovala zawo ndi kuwasiya amaliseche.
לא-מים עיף תשקה ומרעב תמנע-לחם | 7 |
Sunawapatse madzi anthu otopa, ndipo unawamana chakudya anthu anjala,
ואיש זרוע לו הארץ ונשוא פנים ישב בה | 8 |
ngakhale unali munthu wamphamvu, wokhala ndi malo akeake, munthu waulemu wake, wokhala mʼdzikomo.
אלמנות שלחת ריקם וזרעות יתמים ידכא | 9 |
Ndipo akazi amasiye unawachotsa wopanda kanthu, ndipo unapondereza ana amasiye.
על-כן סביבותיך פחים ויבהלך פחד פתאם | 10 |
Nʼchifukwa chake misampha yakuzungulira, nʼchifukwa chake tsoka ladzidzidzi lakuchititsa mantha,
או-חשך לא-תראה ושפעת-מים תכסך | 11 |
nʼchifukwa chake kuli mdima kuti sungathe kuona kanthu, nʼchifukwa chakenso madzi achigumula akumiza.
הלא-אלוה גבה שמים וראה ראש כוכבים כי-רמו | 12 |
“Kodi Mulungu sali kutalitali kumwamba? Ndipo ona nyenyezi zili mmwamba kwambirizo, ona kutalika kwake pamene zililipo!
ואמרת מה-ידע אל הבעד ערפל ישפוט | 13 |
Komabe iweyo ukunena kuti, ‘Kodi Mulungu amadziwa chiyani? Kodi Iye amaweruza mu mdima woterewu?
עבים סתר-לו ולא יראה וחוג שמים יתהלך | 14 |
Mitambo yakuda yamuphimba, kotero kuti Iye sakutiona pamene akuyendayenda pamwamba pa thambopo.’
הארח עולם תשמור-- אשר דרכו מתי-און | 15 |
Kodi iwe udzayendabe mʼnjira yakale imene anthu oyipa ankayendamo?
אשר-קמטו ולא-עת נהר יוצק יסודם | 16 |
Iwo anachotsedwa nthawi yawo isanakwane, maziko awo anakokoloka ndi madzi achigumula.
האמרים לאל סור ממנו ומה-יפעל שדי למו | 17 |
Anthuwo anati kwa Mulungu, ‘Tichokereni! Kodi Wamphamvuzonse angatichitire chiyani?’
והוא מלא בתיהם טוב ועצת רשעים רחקה מני | 18 |
Chonsecho ndi Iye amene anadzaza nyumba zawo ndi zinthu zabwino, choncho ine sindigwirizana ndi uphungu wa anthu oyipa.
יראו צדיקים וישמחו ונקי ילעג-למו | 19 |
“Anthu olungama amaona kuwonongeka kwawo ndipo amakondwera; anthu osalakwa amangoseka, akamuona woyipa akulangidwa.
אם-לא נכחד קימנו ויתרם אכלה אש | 20 |
Amanena kuti, ‘Ndithudi adani athu awonongeka ndipo moto wawononga chuma chawo!’
הסכן-נא עמו ושלם בהם תבואתך טובה | 21 |
“Gonjera Mulungu kuti ukhale naye pamtendere; ukatero udzaona zabwino.
קח-נא מפיו תורה ושים אמריו בלבבך | 22 |
Landira malangizo a pakamwa pake ndipo usunge mawu ake mu mtima mwako.
אם-תשוב עד-שדי תבנה תרחיק עולה מאהלך | 23 |
Ukabwerera kwa Wamphamvuzonse udzabwezeretsedwa; ukachotsa zoyipa zonse zimene zimachitika mʼnyumba mwako,
ושית-על-עפר בצר ובצור נחלים אופיר | 24 |
ndipo chuma chamtengowapatali nuchiona ngati fumbi, golide wa ku Ofiri numutaya ku miyala ya ku zigwa.
והיה שדי בצריך וכסף תועפות לך | 25 |
Pamenepo Wamphamvuzonseyo adzakhala golide wako, siliva wako wamtengowapatali.
כי-אז על-שדי תתענג ותשא אל-אלוה פניך | 26 |
Pamenepo udzakondwera naye Wamphamvuzonse ndipo udzakweza nkhope yako kwa Mulungu.
תעתיר אליו וישמעך ונדריך תשלם | 27 |
Udzamupempha ndipo adzakumvera, ndipo udzapereka zimene unalonjeza.
ותגזר-אמר ויקם לך ועל-דרכיך נגה אור | 28 |
Chimene watsimikiza kuti uchite, chidzachitikadi, kuwala kudzakuwunikira pa njira yako.
כי-השפילו ותאמר גוה ושח עינים יושע | 29 |
Pamene anthu agwetsedwa pansi, iwe nʼkunena kuti, ‘Akwezeni!’ Pamenepo Iye adzapulumutsa anthu oponderezedwa.
ימלט אי-נקי ונמלט בבר כפיך | 30 |
Iye adzapulumutsa ngakhale munthu amene ndi wolakwa, ameneyo adzapulumutsidwa kudzera mʼkulungama kwako.”