< איוב 20 >
Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
לכן שעפי ישיבוני ובעבור חושי בי | 2 |
“Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
מוסר כלמתי אשמע ורוח מבינתי יענני | 3 |
Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
הזאת ידעת מני-עד מני שים אדם עלי-ארץ | 4 |
“Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
כי רננת רשעים מקרוב ושמחת חנף עדי-רגע | 5 |
kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
אם-יעלה לשמים שיאו וראשו לעב יגיע | 6 |
Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
כגללו לנצח יאבד ראיו יאמרו איו | 7 |
iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
כחלום יעוף ולא ימצאהו וידד כחזיון לילה | 8 |
Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
עין שזפתו ולא תוסיף ולא-עוד תשורנו מקומו | 9 |
Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
בניו ירצו דלים וידיו תשבנה אונו | 10 |
Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
עצמותיו מלאו עלומו ועמו על-עפר תשכב | 11 |
Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
אם-תמתיק בפיו רעה-- יכחידנה תחת לשנו | 12 |
“Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
יחמל עליה ולא יעזבנה וימנענה בתוך חכו | 13 |
ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
לחמו במעיו נהפך מרורת פתנים בקרבו | 14 |
koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
חיל בלע ויקאנו מבטנו ירשנו אל | 15 |
Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
ראש-פתנים יינק תהרגהו לשון אפעה | 16 |
Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
אל-ירא בפלגות-- נהרי נחלי דבש וחמאה | 17 |
Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
משיב יגע ולא יבלע כחיל תמורתו ולא יעלס | 18 |
Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
כי-רצץ עזב דלים בית גזל ולא יבנהו | 19 |
Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
כי לא-ידע שלו בבטנו בחמודו לא ימלט | 20 |
“Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
אין-שריד לאכלו על-כן לא-יחיל טובו | 21 |
Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
במלאות שפקו יצר לו כל-יד עמל תבאנו | 22 |
Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
יהי למלא בטנו--ישלח-בו חרון אפו וימטר עלימו בלחומו | 23 |
Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
יברח מנשק ברזל תחלפהו קשת נחושה | 24 |
Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
שלף ויצא מגוה וברק ממררתו יהלך עליו אמים | 25 |
Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
כל-חשך טמון לצפוניו תאכלהו אש לא-נפח ירע שריד באהלו | 26 |
mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
יגלו שמים עונו וארץ מתקוממה לו | 27 |
Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
יגל יבול ביתו נגרות ביום אפו | 28 |
Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
זה חלק-אדם רשע--מאלהים ונחלת אמרו מאל | 29 |
Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”