< איוב 16 >

ויען איוב ויאמר 1
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
שמעתי כאלה רבות מנחמי עמל כלכם 2
“Ndinamvapo zambiri monga zimenezi; nonsenu ndinu anthu osatha kutonthoza mtima mnzanu.
הקץ לדברי-רוח או מה-ימריצך כי תענה 3
Kodi mawu anu ochulukawo adzatha? Kodi chikukuvutani nʼchiyani kuti muzingoyankhula mawu otsutsawa?
גם אנכי-- ככם אדברה לו יש נפשכם תחת נפשי-- אחבירה עליכם במלים ואניעה עליכם במו ראשי 4
Inenso ndikanatha kuyankhula monga inu, inuyo mukanakhala monga ndilili inemu; Ine ndikanatha kuyankhula mawu omveka bwino kutsutsana nanu ndi kukupukusirani mutu wanga.
אאמצכם במו-פי וניד שפתי יחשך 5
Ndipo mawu a pakamwa panga akanakulimbikitsani; chitonthozo chochokera pa milomo yanga chikanachepetsa ululu wanu.
אם-אדברה לא-יחשך כאבי ואחדלה מה-מני יהלך 6
“Koma ine ndikati ndiyankhule ululu wanga sukuchepa; ndipo ndikati ndikhale chete, ululu wanga sukuchokabe.
אך-עתה הלאני השמות כל-עדתי 7
Ndithudi, Inu Mulungu mwanditha mphamvu; mwawononga banja langa lonse.
ותקמטני לעד היה ויקם בי כחשי בפני יענה 8
Inu mwandimanga ndipo kundimangako kwakhala umboni; kuwonda kwanga kwandiwukira ndipo kukuchita umboni wonditsutsa.
אפו טרף וישטמני--חרק עלי בשניו צרי ילטש עיניו לי 9
Mulungu amabwera kwa ine mwankhanza ndipo amadana nane, amachita kulumira mano; mdani wanga amandituzulira maso.
פערו עלי בפיהם--בחרפה הכו לחיי יחד עלי יתמלאון 10
Anthu amatsekula pakamwa pawo kundikuwiza; amandimenya pa tsaya mwachipongwe ndipo amagwirizana polimbana nane.
יסגירני אל אל עויל ועל-ידי רשעים ירטני 11
Mulungu wandipereka kwa anthu ochita zoyipa ndipo wandiponyera mʼmanja mwa anthu oyipa mtima.
שלו הייתי ויפרפרני-- ואחז בערפי ויפצפצני ויקימני לו למטרה 12
Ine ndinali pamtendere, koma Mulungu ananditswanya; anandigwira pa khosi ndi kundiphwanya. Iye anandisandutsa choponyera chandamale chake;
יסבו עלי רביו-- יפלח כליותי ולא יחמל ישפך לארץ מררתי 13
anthu ake oponya mauta andizungulira. Mopanda kundimvera chisoni, Iye akulasa impsyo zanga ndipo akutayira pansi ndulu yanga.
יפרצני פרץ על-פני-פרץ ירץ עלי כגבור 14
Akundivulaza kawirikawiri, akuthamangira pa ine monga munthu wankhondo.
שק תפרתי עלי גלדי ועללתי בעפר קרני 15
“Ndasokerera chiguduli pa thupi langa ndipo ndayika mphamvu zanga pa fumbi.
פני חמרמרה (חמרמרו) מני-בכי ועל עפעפי צלמות 16
Maso anga afiira ndi kulira, ndipo zikope zanga zatupa;
על לא-חמס בכפי ותפלתי זכה 17
komatu manja anga sanachite zachiwawa ndipo pemphero langa ndi lolungama.
ארץ אל-תכסי דמי ואל-יהי מקום לזעקתי 18
“Iwe dziko lapansi, usakwirire magazi anga; kulira kwanga kofuna thandizo kusalekeke!
גם-עתה הנה-בשמים עדי ושהדי במרמים 19
Ngakhale tsopano mboni yanga ili kumwamba; wonditchinjiriza pa mlandu wanga ali komweko.
מליצי רעי אל-אלוה דלפה עיני 20
Wondipembedzera ndi bwenzi langa, pamene maso anga akukhuthula misozi kwa Mulungu;
ויוכח לגבר עם-אלוה ובן-אדם לרעהו 21
iye, mʼmalo mwanga, amamudandaulira Mulungu monga munthu amadandaulira bwenzi lake.
כי-שנות מספר יאתיו וארח לא-אשוב אהלך 22
“Pakuti sipapita zaka zambiri ndisanayende mʼnjira imene sindidzabwerera.”

< איוב 16 >