< הושע 6 >
לכו ונשובה אל יהוה כי הוא טרף וירפאנו יך ויחבשנו | 1 |
“Bwerani, tiyeni tibwerere kwa Yehova. Iye watikhadzula, koma adzatichiritsa. Iye wativulaza, koma adzamanga mabala athu.
יחינו מימים ביום השלישי יקמנו ונחיה לפניו | 2 |
Pakapita masiku awiri adzatitsitsimutsa; pa tsiku lachitatu Iye adzatiukitsa kuti tikhale ndi moyo pamaso pake.
ונדעה נרדפה לדעת את יהוה כשחר נכון מצאו ויבוא כגשם לנו כמלקוש יורה ארץ | 3 |
Tiyeni timudziwe Yehova, tiyeni tilimbike kumudziwa Iye. Adzabwera kwa ife mosakayikira konse ngati kutuluka kwa dzuwa; adzabwera kwa ife ngati mvula ya mʼchilimwe, ngati mvula ya nthawi yamphukira imene imakhathamiritsa nthaka.”
מה אעשה לך אפרים מה אעשה לך יהודה וחסדכם כענן בקר וכטל משכים הלך | 4 |
Iwe Efereimu, kodi ndichite nawe chiyani? Kodi ndichite nawe chiyani, iwe Yuda? Chikondi chanu chili ngati nkhungu yammawa, ngati mame a mmamawa amene amakamuka msanga.
על כן חצבתי בנביאים--הרגתים באמרי פי ומשפטיך אור יצא | 5 |
Choncho ndakuwazani ngati nkhuni kudzera mwa aneneri anga, ndakuphani ndi mawu a pakamwa panga; chigamulo changa chinangʼanima ngati mphenzi pa inu.
כי חסד חפצתי ולא זבח ודעת אלהים מעלות | 6 |
Pakuti Ine ndimafuna chifundo osati nsembe, ndi kudziwa Mulungu kulekana ndi nsembe zopsereza.
והמה כאדם עברו ברית שם בגדו בי | 7 |
Monga Adamu, anthuwa aphwanya pangano langa, iwo sanakhulupirike kwa Ine.
גלעד קרית פעלי און--עקבה מדם | 8 |
Giliyadi ndi mzinda wa anthu ochita zoyipa, okhala ndi zizindikiro za kuphana.
וכחכי איש גדודים חבר כהנים דרך ירצחו שכמה כי זמה עשו | 9 |
Monga momwe mbala zimadikirira anthu, magulu a ansembe amachitanso motero; iwo amapha anthu pa njira yopita ku Sekemu, kupalamula milandu yochititsa manyazi.
בבית ישראל ראיתי שעריריה (שערוריה) שם זנות לאפרים נטמא ישראל | 10 |
Ndaona chinthu choopsa kwambiri mʼnyumba ya Israeli. Kumeneko Efereimu akuchita zachiwerewere, ndipo Israeli wadzidetsa.
גם יהודה שת קציר לך בשובי שבות עמי | 11 |
“Kunenanso za iwe Yuda, udzakolola chilango. “Pamene ndiwabwezere anthu anga zinthu zabwino.”