< Zepania 2 >

1 E HOAO ia oukou iho, a e hoaoia hoi, e ka lahuikanaka hilahila ole;
Sonkhanani pamodzi, sonkhanani pamodzi, inu mtundu wochititsa manyazi,
2 Mamua o ka hiki ana mai o ka olelopaa, Mamua o ka hele ana o ka la e like me ka opala; Mamua mai o ke kau ana mai o ka inaina enaena o Iehova ia oukou; Mamua mai o ke kau ana mai o ka la o ko Iehova inaina ia oukou.
isanafike nthawi yachiweruzo, nthawi yanu isanawuluke ngati mungu, usanakufikeni mkwiyo woopsa wa Yehova, tsiku la ukali wa Yehova lisanafike pa inu.
3 E imi oukou ia Iehova, e ka poe akahai a pau o ka honua, Ka poe i hahai i kona makemake: E imi i ka pono, e imi i ke akahai; I maluhia ai paha oukou i ka la o ko Iehova inaina.
Funafunani Yehova, inu nonse odzichepetsa a mʼdziko, inu amene mumachita zimene amakulamulani. Funafunani chilungamo, funafunani kudzichepetsa; mwina mudzatetezedwa pa tsiku la mkwiyo wa Yehova.
4 No ka mea, e haaleleia auanei o Gaza, E neoneo auanei hoi o Asekelona. E hookukeia auanei o Asedoda i ka wa awakea, A e hookahuliia o Ekerona.
Gaza adzasiyidwa ndipo Asikeloni adzasanduka bwinja. Nthawi yamasana Asidodi adzakhala wopanda anthu ndipo Ekroni adzazulidwa.
5 Auwe ka poe e noho ana ma kahakai! O ka poe Kereti! ke ku e nei ka olelo a Iehova ia oukou. E Kanaana, ka aina o ko Pilisetia, E hoopau auanei au ia oe i koe ole kekahi kanaka.
Tsoka inu okhala mʼmbali mwa nyanja, inu mtundu wa Akereti; mawu a Yehova akutsutsa iwe Kanaani, dziko la Afilisti. “Ndidzakuwononga ndipo palibe amene adzatsale.”
6 A e lilo auanei ka aina kahakai i wahi no na hale kahuhipa, a me na pahipa.
Dziko la mʼmbali mwa nyanja, kumene kumakhala Akereti, lidzakhala malo a abusa ndi la makola a nkhosa.
7 A e lilo ua aina la no ke koena o ka ohana a Iuda; E ai auanei lakou iloko olaila: A i ke ahiahi, e moe lakou iloko o na hale o Asekelona; No ka mea, e ike mai auanei o Iehova ko lakou Akua ia lakou, A e hoihoi mai i ko lakou poe pio.
Malowa adzakhala a anthu otsala a nyumba ya Yuda; adzapezako msipu. Nthawi ya madzulo adzagona mʼnyumba za Asikeloni. Yehova Mulungu wawo adzawasamalira; adzabwezeretsa mtendere wawo.
8 Ua lohe au i ka hoohewa ana mai a ka Moaba, A me ka olelo hoino ana a ka Amona, I ka mea a lakou i hoino ai i ko'u poe kanaka, A hookiekie ae la e ku e mai i ko lakou palena aina.
“Ndamva kunyoza kwa Mowabu ndi chipongwe cha Amoni, amene ananyoza anthu anga ndi kuopseza kuti alanda dziko lawo.
9 Nolaila, ma kuu ola ana, wahi a Iehova o na kaua, O ke Akua no ka Iseraela, E like auanei o Moaba me Sodoma, a o ka Amona e like me Gomora, He nahelehele ooi, me na lua paakai, a me ka neoneo mau loa: Na ke koena o ko'u poe kanaka lakou e hao aku, A e lilo lakou no ke koena o ko'u poe kanaka.
Choncho, pali Ine Wamoyo,” akutero Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, “Ndithu, Mowabu adzasanduka ngati Sodomu, Amoni adzasanduka ngati Gomora; malo a zomeramera ndi maenje a mchere, dziko la bwinja mpaka muyaya. Anthu anga otsala adzawafunkha; opulumuka a mtundu wanga adzalandira dziko lawo.”
10 E hiki no ia mea ia lakou, no ko lakou hoohanohano ana, No ka olelo hoino ana a lakou i haanou ai, A me ka hookiekie ku e i ka poe kanaka o Iehova o na kaua.
Ichi ndi chimene adzalandire chifukwa cha kunyada kwawo, chifukwa chonyoza ndi kuchitira chipongwe anthu a Yehova Wamphamvuzonse.
11 He mea hooweliweli auanei o Iehova ia lakou; No ka mea, e hoohoka auanei oia i na akua a pau o ka honua; A e hoomana aku ia ia ko na aina a pau o kanaka e, O kela mea keia mea ma kona wahi iho.
Yehova adzawachititsa mantha kwambiri pamene adzawononga milungu yonse ya mʼdzikomo. Ndipo mitundu ya anthu pa dziko lonse idzamulambira, uliwonse ku dziko la kwawo.
12 Oukou no hoi, e ko Aitiopa, E houia auanei hoi oukou i kuu pahikaua.
“Inunso anthu a ku Kusi, mudzaphedwa ndi lupanga.”
13 E o aku hoi oia i kona lima e ku e i ke kukulu akau, A e luku aku ia Asuria; a e hooneoneo ia Nineva, A panoa e like me ka waoakua.
Yehova adzatambasulira dzanja lake kumpoto ndi kuwononga Asiriya, kusiya Ninive atawonongekeratu ndi owuma ngati chipululu.
14 E moe iho na ohana hipa iloko ona, A me na holoholona a pau o na aina: E moe no hoi ka pelikana, a me ke kipoda maluna o na kia pohaku ona: E hookani ko lakou leo ma na puka makani ona; He neoneo ma na paepae puka, no ka mea, e weheia auanei na papa kedera ona.
Nkhosa ndi ngʼombe zidzagona pansi kumeneko, pamodzi ndi nyama zakuthengo za mtundu uliwonse. Akadzidzi a mʼchipululu ndi akanungu adzakhala pa nsanamira zake. Kulira kwawo kudzamveka mʼmazenera, mʼmakomo mwawo mudzakhala zinyalala zokhazokha, nsanamira za mkungudza zidzakhala poonekera.
15 O keia ke kulanakauhale olioli i noho nanea, Ka mea i olelo iho iloko o kona naau, Owau wale no, aohe lua! Nani kona lilo ana i mea neoneo, kahi e moe ai na holoholona hihiu! O ka mea e maalo ana ae ia wahi, e kahaha ia me ka hooluliluli aku i kona lima.
Umenewu ndiye mzinda wosasamala umene kale unali wotetezedwa. Unkanena kuti mu mtima mwake, “Ine ndine, ndipo palibenso wina wondiposa.” Taonani lero wasanduka bwinja, kokhala nyama zakutchire! Onse owudutsa akuwunyoza ndi kupukusa mitu yawo.

< Zepania 2 >