< Zekaria 2 >
1 A LAWA hou ae la kuu mau maka iluna, ike ae la, aia hoi, he kanaka me ke kaula-ana ma kona lima.
Kenaka ndinayangʼananso, ndipo ndinaona munthu atanyamula chingwe choyezera mʼmanja mwake.
2 I aku la au, Aihea la oe e hele ana? I mai la kela ia'u, E ana iho ai ia Ierusalema, i ike au i kona laula a me kona loa.
Ndipo ndinafunsa kuti, “Kodi ukupita kuti?” Anandiyankha kuti, “Akukayeza Yerusalemu kuti ndidziwe mulifupi mwake ndi mulitali mwake.”
3 Aia hoi, hele aku la ka anela i kamailio me au, a hele aku la hoi kekahi anela e ae e halawai me ia;
Taonani, mngelo amene amayankhula nane uja akuchoka, mngelo wina anabwera kudzakumana naye
4 A olelo aku la ia ia, E holo aku oe, e olelo aku i keia kanaka opiopio, penei, E noho puni ole i ka pa na kanaka o Ierusalema, no ka nui o na kanaka a me na holoholona iloko.
ndipo anamuwuza kuti, “Thamanga, kamuwuze mnyamatayo kuti, ‘Yerusalemu udzakhala mzinda wopanda malinga chifukwa mudzakhala anthu ambiri ndiponso ziweto zochuluka.
5 No ka mea, owau auanei he paku ahi nona a puni, wahi a Iehova, a owau hoi iloko ona he nani.
Ndipo Ine mwini ndidzakhala linga lamoto kuteteza mzindawo,’ akutero Yehova, ‘ndipo ndidzakhala ulemerero mʼkati mwake.’
6 Ea! ea! e holo hoi oukou mai ka aina kukuluakau aku, wahi a Iehova: no ka mea, ua hoopuehu aku au ia oukou me na makani eha o ka honua, wahi a Iehova.
“Tulukani! Tulukani! Thawaniko ku dziko la kumpoto,” akutero Yehova, “pakuti ndinakumwazirani ku mphepo zinayi zamlengalenga,” akutero Yehova.
7 E Ziona e, e hoopakele ia oe iho, e ka mea e noho pu ana me ke kaikamahine a Babulona.
“Tuluka, iwe Ziyoni! Thawa, iwe amene umakhala mʼdziko la mwana wamkazi wa Babuloni!”
8 No ka mea, penei ka olelo ana mai a Iehova o na kaua, Mahope o ka nani, ua hoouna mai oia ia'u i na lahuikanaka, i ka poe nana oukou i hao mai; no ka mea, o ka mea hoopa aku ia oukou, hoopa no ia i ka onohi o kona maka.
Pakuti Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Atatha kundilemekeza wanditumiza kwa anthu a mitundu ina amene anakufunkhani; pakuti aliyense wokhudza inu wakhudza mwanadiso wanga.
9 Aia hoi, e lulu aku no au i kuu lima maluna o lakou, a e haoia'ku lakou e ko lakou poe kauwa; a e ike auanei oukou ua hoouna mai o Iehova o na kaua ia'u.
Ndithu Ine ndidzawamenya anthuwo ndi dzanja langa ndipo amene anali akapolo awo ndiye adzawalande zinthu. Pamenepo mudzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse ndiye wandituma.
10 E olioli, e hauoli hoi, e ke kaikamahine o Ziona; no ka mea, aia hoi, e hele aku ana au, a e noho au iwaena pu o oukou, wahi a Iehova.
“Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, fuwula ndipo sangalala. Pakuti taona ndikubwera, ndipo ndidzakhala pakati pako,” akutero Yehova.
11 Ia la hoi, he nui na lahuikanaka e hui aku ia lakou iho me Iehova, a e lilo lakou i kanaka no'u, a e noho no wau iwaena pu o oukou; a e ike auanei oukou na Iehova o na kaua wau i hoouna mai iou la.
“Nthawi imeneyo anthu a mitundu yambiri adzabwera kwa Yehova ndipo adzasanduka anthu anga. Ndidzakhala pakati pako ndipo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse wandituma kwa iwe.
12 A e komo auanei o Iehova i ka Iuda i kuleana nona ma ka aina hoano, a e koho hou oia ia Ierusalema.
Yehova adzachititsa kuti Yuda akhale chuma chake mʼdziko lopatulika ndipo adzasankhanso Yerusalemu.
13 E hamau oukou, e na kanaka a pau imua o Iehova; no ka mea, ua hoalaia'e oia mai kona noho hoano ae.
Khalani chete pamaso pa Yehova anthu nonse, chifukwa Iye wavumbuluka kuchoka ku malo ake opatulika.”