< Nahuma 3 >

1 A UWE ke kulanakauhale koko! Ua piha oia a pau i ka wahahee, a me ka powa; Aole e laweia'ku ke pio;
Tsoka kwa mzinda wopha anthu, mzinda wodzaza ndi mabodza, mzinda wodzaza ndi anthu olanda zinthu anzawo, mu mzinda mʼmene simusowa anthu osautsidwa nthawi zonse!
2 O ka poha o ka huipa, a o ka halulu o ke kaa ana o na kaa, A o ka holo ana o na lio, a o ka lele ana o na halekaa.
Kulira kwa zikwapu, mkokomo wa mikombero, kufuwula kwa akavalo ndiponso phokoso la magaleta!
3 Kaikai ae ka hoohololio i ka pahikaua wakawaka a me ka ihe huali; A he nui ka poe i pepehiia, a he nui na kupapau; Aohe hope o na heana, A hina lakou maluna o ko lakou mau heana.
Kuthamanga kwa anthu okwera pa akavalo, kungʼanima kwa malupanga ndi kunyezimira kwa mikondo! Anthu ambiri ophedwa, milumilu ya anthu akufa, mitembo yosawerengeka, anthu akupunthwa pa mitemboyo.
4 No ka nui o na moe kolohe ana o ka wahine maikai hookamakama, Nona na anaana. Ka mea kuai i na lahuikanaka ma kona moe kolohe ana, A me na ohana, ma kona mau anaana ana;
Zonsezi ndi chifukwa cha zilakolako za mkazi wachiwerewere, wokopa anthu uja, mkazi wochita zamatsenga, amene anakopa mitundu ya anthu ndi zachiwerewere zake, ndiponso anthu a mitundu ina ndi zaufiti zake.
5 Aia hoi, ua maka e aku au ia oe, wahi a Iehova o na kaua; A e huli ae au i kou kapa maluna o kou maka, A e hoike aku au i kou olohelohe ana i na lahuikanaka, A i kou hilahila i na aupuni.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikutsutsana nawe. Ndidzakuvula chovala chako. Anthu a mitundu ina ndidzawaonetsa umaliseche wako ndipo udzachita manyazi pamaso pa maufumu onse.
6 A e hoolei aku au maluna ou i na mea haumia, A e hoolilo au ia oe i mea e manao ole ia, A e hooku au ia oe i mea e makaikaiia.
Ndidzakuthira zonyansa, ndidzakuchititsa manyazi ndiponso kukusandutsa chinthu choseketsa.
7 A o na mea a pau e nana aku ia oe, Holo no lakou mai ou aku la, me ka i ana aku, Ua lukuia o Nineva! Owai la ka mea e auwe ia ia? A mahea la wau e imi aku ai i na mea hooluolu nou?
Onse amene adzakuona adzakuthawa ndipo adzati, ‘Ninive wasanduka bwinja, adzamulira ndani?’ Kodi ndingamupeze kuti munthu woti nʼkukutonthoza?”
8 Ua oi anei kou maikai mamua o ko No-Amona, Ka mea e noho ana ma na muliwai, Ua hoopuniia oia e na wai, O ke kai kona paku, a o kona papohaku mai ke kai mai ia?
Kodi ndiwe wopambana Tebesi, mzinda wokhala mʼmbali mwa Nailo, wozunguliridwa ndi madzi? Mtsinjewo unali chitetezo chake, madziwo anali linga lake.
9 O Aitiopa kona ikaika a me Aigupita, aohe heluia; O Puta a me Lubima kou mau mea kokua.
Mphamvu zake zinali Kusi ndi Igupto, Puti ndi Libiya anali ena mwa abwenzi ake.
10 Aka, ua laweia'ku oia, ua hele pio aku ia; A ua ulupaia kana mau keiki liilii ma ke poo o na alanui a pau: A hailona lakou no kona poe kanaka hanohano, A ua hoopaaia kona mau kanaka nui a pau i na kaulahao.
Komabe anthu a ku Tebesi anagwidwa ndipo anapita ku ukapolo. Ana ake anawaphwanyitsa pansi mʼmisewu yonse ya mu mzindamo. Anachita maere ogawana anthu ake otchuka, ndipo anthu ake onse amphamvu anamangidwa ndi maunyolo.
11 A e ona no hoi oe, a e hunaia oe; A e imi no oe i ka ikaika no ka poe enemi.
Iwenso Ninive udzaledzera; udzabisala ndipo udzafunafuna malo othawirako kuopa mdani.
12 A e like kou mau wahi paa me ka laau fiku, me ka hua pala mua, Ina e hooluliia, e haule iho lakou iloko o ka waha o ka mea e ai ana.
Malo ako onse otetezedwa ali ngati mitengo ya mkuyu yokhala ndi zipatso zoyambirira kucha; pamene agwedeza mitengoyo, nkhuyuzo zimagwera mʼkamwa mwa wofuna kuzidya.
13 Aia hoi, o kou poe kanaka iwaena ou, ua like me na wahine; A e hoohamama loa ia na pukapa o kou aina i kou poe enemi; A e hoopau ke ahi i kou mau kaola.
Tayangʼana ankhondo ako, onse ali ngati akazi! Zipata za dziko lako zatsekukira adani ako; moto wapsereza mipiringidzo yake.
14 E hukiwai ae nou, no ka popilikia, E hoopaa oe i kou mau wahi paa; E komo oe iloko o ka lepo, a e hehi iho i ka lepo kawili, A e hoopaa i kahi puhi pohaku-ula.
Tungani madzi woti mudzamwe nthawi ya kuzunguliridwa kwanu, limbitsani chitetezo chanu! Pondani dothi, ikani mʼchikombole, konzani khoma la njerwa!
15 Malaila e hoopau ai ke ahi ia oe; E oki mai ka pahikaua ia oe, E ai iho no ia ia oe, e like me ka uhini huluhulu: E hoomahuahua ia oe iho e like me ka uhini huluhulu; Hoonui ia oe iho e like me ka uhini nui.
Kumeneko moto udzakupserezani; lupanga lidzakukanthani ndipo lidzakuwonongani ngati likuwononga ziwala. Chulukanani ngati ziwala, chulukanani ngati dzombe!
16 Ua hoonui oe i kou poe kalepa mamua o na hoku o ka lani: Hoopalahalaha aku ka uhini huluhulu, a lele aku la.
Mwachulukitsa chiwerengero cha anthu a malonda anu mpaka kupambana nyenyezi za mlengalenga, koma iwo ngati dzombe akuwononga dziko ndipo kenaka akuwuluka nʼkuchoka.
17 Ua like kou poe alii me na uhini, A o kou poe lunakoa e like me na uhini nui loa, Ka mea e kau ana ma ka papohaku i ka la anu, A puka mai ka la, lele aku lakou, aole i ikeia ko lakou wahi.
Akalonga ako ali ngati dzombe, akuluakulu ako ali ngati gulu la dzombe limene lamatirira pa khoma nthawi yozizira, koma pamene dzuwa latuluka limawuluka, ndipo palibe amene amadziwa komwe lapita.
18 Ke hiamoe nei kou poe kahuhipa, e ke alii o Asuria: E noho iho kou poe alii; Ua hoopuehuia kou poe kanaka ma na mauna, Aohe mea nana lakou e hoakoakoa mai.
Iwe mfumu ya ku Asiriya, abusa ako agona tulo; anthu ako olemekezeka amwalira. Anthu ako amwazikira ku mapiri popanda ndi mmodzi yemwe wowasonkhanitsa.
19 Aohe mea hoola i kou eha ana; ua nui kou eha; O ka poe a pau e lohe i kou lono, e paipai lakou i ko lakou lima maluna ou; No ka mea, maluna owai anei i hele mau ole aku ai kou hewa?
Palibe chimene chingachize bala lako; chilonda chako sichingapole. Aliyense amene amamva za iwe amawomba mʼmanja chifukwa cha kugwa kwako, kodi alipo amene sanazilawepo nkhanza zako zosatha?

< Nahuma 3 >