< Iona 4 >

1 A HE mea hewa nui ia ia Iona, a huhu iho la ia.
Koma Yona anakhumudwa kwambiri ndipo anakwiya.
2 A pule aku la no ia ia Iehova, i aku la, Ke noi aku nei au ia oe, e Iehova, aole anei keia kuu olelo, i kuu noho ana ma ko'u aina? Nolaila i holo aku ai au mamua i Taresisa: no ka mea, ua ike no au he Akua ahonui oe, a me ke aloha, e hakalia ana i ka huhu, a he lokomaikai nui, a me ka haalele i ka manao hoopai.
Iye anapemphera kwa Yehova kuti, “Inu Yehova, kodi izi si zimene ndinanena ndikanali kwathu? Nʼchifukwa chaketu ine ndinafulumira kuthawa kupita ku Tarisisi. Ine ndinadziwa kuti ndinu Mulungu wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wa chikondi chopanda malire, Mulungu amene mumaleka kubweretsa tsoka.
3 Ano hoi, e Iehova, ke noi aku nei au ia oe, e lawe oe i kuu ola mai o'u aku la; no ka mea, ua oi ka maikai o kuu make mamua o ke ola.
Ndipo tsopano, Inu Yehova, ingondiphani basi, pakuti ndi bwino kuti ndife kupambana nʼkukhala ndi moyo.”
4 A olelo mai o Iehova, He pono anei nou ka huhu?
Koma Yehova anayankha kuti, “Kodi nʼkoyenera kuti iwe ukwiye?”
5 A hele aku la o Iona iwaho o ke kulanakauhale, a noho iho la ma ka hikina o ke kulanakauhale, a hana iho la ilaila i wahi lanai nona, a noho iho la malalo o kona malu, i ike aku ia i ka mea e hanaia ma ke kulanakauhale.
Yona anatuluka mu mzindamo nakakhala pansi cha kummawa kwa mzindawo. Kumeneko anadzimangira chithando nakhala mʼmenemo mu mthunzi, kudikira kuti aone zimene zichitikire mzindawo.
6 A hoomakaukau o Iehova ke Akua i laau aila, a hooulu ae la ia mea maluna o Iona, i lilo ia i wahi malumalu o kona poo, e hoopakele ia ia mai kona mea kaumaha. A olioli nui o Iona i ka laau aila.
Tsono Yehova Mulungu anameretsa msatsi ndi kuyikulitsa kuti ipereke mthunzi kwa Yona kuchotsa mavuto ake; ndipo Yona anasangalala kwambiri chifukwa cha msatsiyo.
7 A hoomakaukau ke Akua i wahi enuhe i ka wanaao i ka la apopo, a ai iho la ia i ka laau aila, a mae iho la ia.
Koma tsiku linalo mmawa, Mulungu anabweretsa mbozi imene inadya msatsiyo ndipo inafota.
8 A i ka wa i puka mai ai ka la, hoomakaukau ke Akua i makani hikina wela: a kau ka la maluna o ke poo o Iona, a maule iho la ia, a manao iho la iloko ona e make, a i iho la, ua oi ka maikai o kuu make mamua o ke ola.
Dzuwa litatuluka, Yehova anabweretsa mphepo yotentha yochokera kummawa, ndipo dzuwa linatentha pamutu pa Yona kotero analenguka nalo. Iye anangofuna atafa, ndipo anati, “Ndi bwino kuti ndife kupambana nʼkukhala ndi moyo.”
9 A olelo mai la ke Akua ia Iona, He pono anei kou huhu no ka laau aila? A i aku la ia, He pono ko'u huhu a i ka make.
Koma Mulungu anati kwa Yona, “Kodi nʼkoyenera kuti iwe ukwiye chifukwa cha msatsi?” Iye anayankha kuti, “Inde nʼkoyenera. Kukwiya kwanga nʼkofuna kufa nako.”
10 A olelo mai o Iehova, Ua minamina anei oe i ka laau aila, ka mea aole oe i luhi, aole hoi oe i hooulu: kupu mai no ia i ka po hookahi, a make iho la i ka po hookahi:
Koma Yehova anati, “Iwe ukumvera chisoni msatsiwo, ngakhale kuti sunawugwirire ntchito kapena kuwukulitsa. Inamera pa usiku umodzi ndipo inafanso pa usiku umodzi.
11 Aole anei he pono ko'u mina mina ana ia Nineva, ke kulanakauhale nui, iloko ona he lehulehu, hookahi haneri a me ka iwakalua na tausani a keu aku, ka poe ike ole iwaena o ka lima akau a me ka lima hema; a ua nui loa hoi na holoholona?
Koma mu Ninive muli anthu opitirira 120,000 amene sadziwa kusiyanitsa kuti chabwino nʼchiti ndipo choyipa nʼchiti, mulinso ziweto zochuluka. Kodi sindiyenera kumvera chisoni mzinda waukulu ngati uwu?”

< Iona 4 >