< Ioba 24 >

1 NO ka mea, aole i hoonaloia na manawa mai ka Mea mana aku, No ke aha la aole ka poe ike ia ia e noonoo i kona mau la?
“Chifukwa chiyani Wamphamvuzonse sayikiratu nthawi yoti aweruze? Chifukwa chiyani iwo amene amadziwa Iyeyo amayembekezera pachabe masiku oterewa?
2 Hoonee aku lakou i na palena aina, A lawe wale aku lakou i ka poe hipa, a hanai aku ia lakou.
Anthu amasuntha miyala ya mʼmalire, kuti akuze dziko lawo; amadyetsa ziweto zimene aba.
3 Alakai aku lakou i ka hokikane o ka poe makua ole; A lawe lakou i ka bipi a ka wahinekanemake i uku panai.
Amalanda abulu a ana amasiye ndipo amatenganso ngʼombe ya mkazi wamasiye ngati chikole.
4 Ua kipaku lakou i ka poe nele mai ke ala aku; Pee pu aku la na ilihune o ka honua.
Amachotsa mʼmisewu anthu osauka, ndipo amathamangitsa amphawi onse mʼdziko.
5 Aia hoi, me na hoki hihiu ma ka waonahele, hele aku lakou i ka lakou hana; E imi ana i ka mea pio; O ka waonahele oia ka ai na lakou, a na ka lakou poe keiki.
Amphawiwo amakhala ngati mbidzi mʼchipululu, amayendayenda kufuna chakudya; dziko lowuma limapereka chakudya cha ana awo.
6 Ma ka mahinaai, oki kela mea keia mea i kana ai; A hoiliili lakou ma ka pawaina o ka mea hewa,
Iwo amakolola za mʼminda ya eni ake, ndipo amakunkha mphesa mʼminda ya anthu oyipa.
7 Waiho lakou i ka poe olohelohe i moe lakou me ka kapa ole, Aohe mea uhi iloko o ke anu.
Amagona maliseche usiku wonse kusowa zovala; pa nthawi yozizira amasowa chofunda.
8 Ua pulu lakou i ka ua nui o oa mauna, A no ka hale ole, ua pili lakou i ka pohaku.
Amavumbwa ndi mvula ya mʼmapiri ndipo amakangamira ku matanthwe kusowa pobisalapo.
9 Kaili lakou i ka mea makua ole mai ka u aku, A lawe lakou i ka aahu o ka ilihune i uku panei
Amatsomphola mwana wamasiye wa ku bere; ndipo amagwira mwana wakhanda wa mʼmphawi kuti akhale chikole.
10 Hoohele lakou i ka mea olohelohe me ke kapa ole, A lawe aku lakou i ka poa palaoa mai ka pololi;
Amphawi amangoyenda maliseche kusowa zovala; amasenza mitolo ya tirigu, koma nʼkumagonabe ndi njala.
11 Kaomi lakou i ka aila mawaena o ko lakou meu papohaku, Hahi lakou i na wahi kaomi waina, a makewai lakou.
Iwo amayenga mafuta a olivi mʼminda ya anthu oyipa; amapsinya mphesa, koma nʼkumamvabe ludzu.
12 Kunukunu na kanaka mai ke kulanakauhale aku, A o ka naau i houia ke kahea aku; Aole ke Akua i manao mai i ka mea lapuwale,
Kubuwula kwa anthu amene akufa kumamveka kuchokera mu mzinda, anthu ovulala akulirira chithandizo. Koma Mulungu sakuyimba mlandu wina aliyense.
13 O lakou ka poe e kipi ana i ka malamalama, Aole lakou i ike i kona mau kuamoo, Aole lakou i nobo ma kona mau alanui.
“Pali ena amene amakana kuwala, amene safuna kuyenda mʼkuwalako kapena kukhala mʼnjira zake.
14 I ka malamalama ala mai ka pepehi kanaka, A pepehi aku i ka poe ilihune a me ka poe nele, A i ka po ua like ia me ka aihue.
Dzuwa likalowa, wopha anzake amadzuka ndipo amakapha osauka ndi amphawi; nthawi ya usiku iye amasanduka mbala.
15 Ke kali ae la ka make o ka mea moe kolohe i ke ahiahi poeleele, I iho la, Aole e ike mai ka make ia'u; A kau i ka pale ma ka make.
Munthu wachigololo amadikira chisisira; iyeyo amaganiza kuti, ‘Palibe amene akundiona,’ ndipo amaphimba nkhope yake.
16 I ka pouli wawahi lakou i na hale, I ke ao hoopaa lakou ia lakou iho iloko: Aole lakou i ike i ka malamalama.
Mbala zimathyola nyumba usiku, koma masana zimadzitsekera; izo zimathawa kuwala.
17 No ka mea, o kakahiaka, ua like pu ia no lakou me ka malu make; Ina ikeia, ua kau mai na mea weliweli o ka malu make.
Pakuti kwa onsewa mdima wandiweyani ndiye kuti kwawachera. Iwo amachita ubale ndi zoopsa za mdima.
18 Ua like lakou me ka mea mama maluna o ka wai; Ua hoinoia ko lakou kuleana ma ka honua; Aole lakou e huli ae ma ke ala o na pawaina,
“Komatu iwowo ndi thovu loyandama pa madzi; minda yawo ndi yotembereredwa pa dzikolo kotero kuti palibe amene amapita ku minda ya mpesa.
19 Na ka maloo a me ka wela e hoopau aku i na wai o ka hau; Pela no ka po i ka poe hana hewa. (Sheol h7585)
Monga momwe kutentha ndi chilala zimasungunulira madzi owundana ndi momwemonso mmene manda amachotsera omwe achimwa. (Sheol h7585)
20 E hoopoina ka opu ia ia; E ai wale ka ilo ia ia; Aole loa e hoomanaoia oia; A e haki ka mea hewa me he laau la.
Mayi wowabereka amawayiwala, mphutsi zimasangalala powadya; anthu oyipa sakumbukiridwanso koma amathyoka ngati mtengo.
21 Hookaumaha oia i ka mea pa hanau ole, Aole ia i hana maikai aku i ka wahinekanemake,
Amachitira nkhanza mayi wosabala ndi mayi amene alibe mwana, ndipo sakomera mtima mkazi wamasiye.
22 Lawe aku no ia i ka poe alii ma kona ikaika; A ka mai oia, aohe malu ke ola o kekahi.
Koma Mulungu amawononga munthu wamphamvu mwa mphamvu zake; ngakhale munthuyo atakhazikika, alibe chiyembekezo cha moyo wake.
23 Ina e haawiia none e maluhia, a e hilinai; Aka, o kona mau make aia maluna o ko lakou mau aoao.
Mulungu atha kuwalola kuti akhale mosatekeseka, koma amakhala akupenyetsetsa njira zawo.
24 Ua hookiekieia lakou i ka wa pokole, Aka, oa ole lakou, a ua hoonalowaleia lakou; E like me na mea a pau, ua hoiia lakou, Ua okiia lakou e like me na piko huhui palaoa.
Kwa kanthawi kochepa oyipa amakwezedwa ndipo kenaka saonekanso; amatsitsidwa ndipo amachotsedwa monga ena onse; amadulidwa ngati ngala za tirigu.
25 Ina i ole pela ano, Owai la ka mea e hoike mai, he hoopunipuni ka'u, A e hoolilo i ka'u olelo i mea ole?
“Ngati zimenezi sizoona, ndani angaonetse kuti ndine wabodza ndi kusandutsa mawu anga kukhala wopanda pake?”

< Ioba 24 >