< Ioba 21 >

1 A OLELO mai la o loba, i mai la,
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 E hoolohe pono oukou i ka'u olelo, A o keia ko oukou hooluolu ana.
“Mvetserani bwino mawu anga; ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.
3 E ae mai oukou ia'u e olelo aku ai au, A mahope o kuu olelo, e hoomaewaewa oukou.
Ndiloleni ndiyankhule ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.
4 Owau hoi, i ke kanaka anei kuu ulono ana? A ina pela, no ke aha la ka huhu ole o kuu uhane?
“Kodi ine ndikudandaulira munthu? Tsono ndilekerenji kupsa mtima?
5 E nana oukou ia'u a e pihoihoi, A e kau oukou i ka lima maluna o ka waha.
Ndipenyeni ndipo mudabwe; mugwire dzanja pakamwa.
6 A ina e hoomanao wau, ua weliweli au, A loohia kuu io e ka haalulu.
Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri; thupi langa limanjenjemera.
7 No ke aha la e ola ana ka poe hewa, E elemakule ana, e nui ana hoi i ka waiwai?
Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo, amakalamba ndi kusanduka amphamvu?
8 O ko lakou hua, ua hookupaaia me lakou imua o ko lakou alo, A o ka lakou poe keiki imua o ko lakou maka.
Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo, zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.
9 Ua maluhia ko lakou mau hale, aohe makau, Aole hoi ka laau hahau o ke Akua maluna o lakou.
Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha; mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.
10 Hapai no ka lakou bipi, aole hoi i hemahema; Hua mai no ka lakou bipiohi, aole i hanau hapa.
Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa; ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.
11 Kuu aku lakou i ka lakou poe kamalii me he kumu hipa la, A lelele no ka lakou poe keiki.
Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa; makanda awo amavinavina pabwalo.
12 Hoomaka lakou me ka pahu kani a me ka lira, A olioli lakou i ke kani ana o ka hokiokio.
Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze; amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.
13 Noho lakou i ko lakou mau la me ka pomaikai, A iho koke lakou i ka po. (Sheol h7585)
Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. (Sheol h7585)
14 A olelo iho lakou i ke Akua, E hele oe mai o makou aku; A o ka ike i kou mau aoao, aohe makou makemake.
Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’ Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.
15 Owai ka Mea mana, i malama ai kakou ia ia? Heaha ka mea e loaa ai, ke nonoi kakou ia ia?
Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire? Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?
16 Aia hoi, aole ma ko lakou lima ko lakou pomaikai: O ke kuka ana o ka poe hewa, ua mamao aku ia ia'u.
Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo, koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.
17 He pinepine i pio ai ke kukui o ka poe hewa, A e hiki koke mai hoi ko lakou make maluna o lakou, A ua hooili mai ia i na eha ma kona inaina.
“Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa? Nʼkangati kamene tsoka limawagwera? Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?
18 Ua like lakou me ka mauu maloo imua o ka makani, E like hoi me ka opala a ka puahiohio i lawe aku.
Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo, ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?
19 Ua hoomau ke Akua i kona hewa no kana poe keiki: Ua uku mai ia ia ia, a e ike auanei oia.
Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’ Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.
20 E ike no kona maka i kona popilikia. E inu no ia i ka huhu o ka Mea mana.
Mulole kuti adzionere yekha chilango chake, kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.
21 No ka mea, heaha la kana hana iloko o kona hale mahope ona, I ka manawa e okiia'i mawaena ka huina o kona mau malama?
Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo, pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?
22 K ao mai anei kekahi i ke Akua i ka ike, I ka mea hooponopono i ka poe kiekie?
“Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru, poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?
23 Make no kekahi iwaena o kona pomaikai, E noho nanea ana a me ka oluolu.
Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse, ali pa mtendere ndi pa mpumulo,
24 Ua piha kona mau aoao i ka momona, Ua mau kona mau iwi i ka lolo.
thupi lake lili lonenepa, mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.
25 A make no kekahi me ka naau ehaeha, Aole ia i hoao i ka lealea.
Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima, wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.
26 E moe pu laua i ka lepo, A e paapu na ilo maluna o laua.
Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda ndipo onse amatuluka mphutsi.
27 Aia hoi, ua ike no wau i ko oukou mau noonoo ana, A me ko oukou mau manao a oukou i hoino ai ia'u.
“Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza, ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.
28 No ka mea, ke olelo nei oukou, Auhea ka hale o ke alii? Auhea hoi ka uhi o na halelewa o ka poe hewa?
Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti, matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’
29 Aole anei oukou i ninau i ka poe e maalo ae ana ma ke ala? A ike ole anei oukou i ko lakou mau hoailona?
Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo? Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?
30 No ka mea, ua waihoia ka poe hewa no ka la popilikia, A e laweia mai lakou no ka la e inaina ai.
Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka, kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?
31 Owai ka mea e hoike aku i kona aoao imua ona? A owai ka mea e uku aku ia ia i kana mea i hana'i?
Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo? Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?
32 A e laweia aku oia i ka luakupapau, A e kiaiia oia ma ka hale kupapau.
Iye amanyamulidwa kupita ku manda ndipo anthu amachezera pa manda ake.
33 E kau oluolu maluna ona na papaa lepo o ke awawa, A mahope ona e hahai aku na kanaka a pau, E like me ka poe mamua ona he lehulehu no.
Dothi la ku chigwa limamukomera; anthu onse amatsatira mtembo wake, ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.
34 A pehea la ko oukou hooluolu make hewa ana mai ia'u, A ua hewa ka oukou olelo ana mai?
“Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”

< Ioba 21 >