< Ioba 12 >
1 OLELO mai ia o Ioba, i mai la,
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 He oiaio, o oukou ka poe kanaka, A e make pu ka noiau me oukou.
“Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
3 Aka, he naauao ko'u e like me oukou; Aole au i emi malalo iho o oukou: A owai la ka mea ike ole i na mea like me keia mau mea?
Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
4 Ua lilo au i mea heneheneia e kona hoalauna, E kahea ana i ke Akua, a hoolohe mai oia ia ia; O ka mea pono a me ka hala ole, ua akaakaia oia.
“Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
5 Me ka ipukukui i hoowahawahaia i ka manao o ka mea e noho nanea ana, Pela ka mea ua kokoke pahee kona mau wawae.
Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
6 Ua pomaikai na halelewa o ka poe luku wale, A ua noho maluhia ka poe hoonaukiuki aku i ke Akua; Iloko o ko lakou lima na ke Akua i haawi mai.
Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
7 Aka, ano e ninau i na holoholona, a e ao mai lakou ia oe; A me na manu o ka lewa, a e hoike mai lakou ia oe;
“Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
8 E olelo aku paha i ka honua, a e ao mai no ia ia oe: A o na ia o ke kai e hoakaka mai no lakou ia oe,
kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
9 Owai la ka mea ike ole i keia mau mea a pau, Na ka lima o Iehova i hana keia?
Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
10 Iloko o kona lima ka uhane o na mea ola a pau, A me ka hanu o na kanaka a pau.
Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
11 Aole anei e hoao ke pepeiao i na olelo? A e hoao ka waha i ka ai nona iho?
Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
12 Me ka poe kahiko ka maiau, A me ke ola loihi ka naauao.
Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
13 Ia ia ka naauao, a me ka ikaika; Nona ka oleloao, a me ke akamai.
“Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
14 Aia hoi, ke wawahi nei oia, aole e kukulu hou ia; Ke hahao aku ia i ke kanaka iloko, aole e hookuuia'ku.
Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
15 Aia hoi, ke hoopaa nei oia i na wai, a ua maloo lakou: A hookuu aku oia ia lakou, a luku lakou i ko ka honua.
Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
16 Me ia ka ikaika, a me ka naauao: Nona ka mea i hoopuniia, a me ka mea hoopuni.
Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
17 Ua lawe pio aku ia i na kakaolelo, A hoolilo i na lunakanawai i poe hawawa.
Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
18 Kala aku no ia i ka mea paa o na'lii, A kaei aku ia i ko lakou puhaka i ke kaei.
Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
19 Alakai pio aku ia i na kahuna, A hookahuli i ka poe ikaika.
Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
20 Hoopau aku ia i ka olelo a ka poe oiaio, A lawe aku ia i ka naauao, mai ka poe kahiko aku.
Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
21 Ninini iho ia i ka hoino maluna o na'lii, A kala ae no ia i ke kaei o ka poe ikaika.
Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
22 Hoike mai ia i na mea hohonu mailoko mai o ka pouli, A hoopuka no ia i ka malamalama mai ka malu make mai.
Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
23 Hoomahuahua no ia i na lahuikanaka, a luku aku no hoi ia lakou: Hoonui aku no ia i na lahuikanaka, a hoemi hou iho ia lakou.
Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
24 Lawe aku ia i ka naauao o na luna o kanaka ma ka honua; A hooauwana ia lakou ma ka waonahele, aohe alauui.
Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
25 Haha lakou iloko o ka pouli aohe malamalama, A e hoohikaka aku oia ia lakou, me he mea ona la.
Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.