+ Kinohi 1 >
1 I KINOHI hana ke Akua i ka lani a me ka honua.
Pachiyambi Mulungu analenga kumwamba ndi dziko lapansi.
2 He ano ole ka honua, ua olohelohe; a maluna no o ka hohonu ka pouli. Hoopunana iho la ka Uhane o ke Akua maluna o ka wai.
Dziko lapansi linali losakonzedwa ndi lopanda kanthu. Mdima wandiweyani unakuta nyanja ndipo Mzimu wa Mulungu unkayendayenda pamwamba pa madziwo.
3 I iho la ke Akua, I malamalama; a ua malamalama ae la.
Pamenepo Mulungu anati, “Kuwale” ndipo kunawaladi.
4 Nana ae la ke Akua i ka malamalama, ua maikai: a hookaawale ae la ke Akua mawaena o ka malamalama, a me ka pouli.
Mulungu anaona kuti kuwalako kunali bwino ndipo Iye analekanitsa kuwala ndi mdima.
5 Kapa mai la ke Akua i ka malamalama, he Ao, a kapa mai hoi ia i ka pouli, he Po. A o ke ahiahi a me ke kakahiaka, o ka la mua ia.
Mulungu anatcha kuwalako “usana” ndipo mdima anawutcha “usiku.” Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku loyamba.
6 I iho la ke Akua, I aouli mawaena o na wai, i mea hookaawale i kekahi wai me kekahi wai.
Kenaka Mulungu anati, “Pakhale thambo pakati pa madzi kuti lilekanitse madzi a mʼmwamba ndi madzi a pansi.”
7 Hana iho la ke Akua i ke aouli; a hookaawale ae la ia i ka wai malalo o ke aouli, me ka wai maluna o ke aouli: a pela io no.
Ndipo Mulungu anapanga thambo nalekanitsa madzi amene anali pansi ndi pamwamba pa thambo lija, ndipo zinachitikadi.
8 Kapa iho la ke Akua i ke aouli, he Lani. A o ke ahiahi a me ke kakahiaka, o ka lua ia o ka la.
Mulungu anatcha thambo lija “kumwamba.” Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachiwiri.
9 I iho la ke Akua, E hui pu na wai malalo o ka lani i kahi hookahi, i ikea ai kahi maloo: a pela io no.
Mulungu anati, “Madzi a pansi pa thambo asonkhane pa malo amodzi kuti mtunda uwoneke,” ndipo zinachitikadi.
10 Kapa iho la ke Akua i kahi maloo, he Aina; a kapa iho la oia i na wai i hui pu ia 'i, o na moana: a nana ae la ke Akua, ua maikai.
Mulungu anawutcha mtundawo “dziko,” madzi osonkhana pamodziwo anawatcha “nyanja.” Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
11 I iho la ke Akua, E hooulu mai ka honua i ka mauu, a me ka launahele e hua ana i ka hua, a me ka laau hua e hua ana hoi ma kona ano iho, iloko ona iho kona hua maluna o ka honua: a pela io no.
Kenaka Mulungu anati, “Dziko libereke zomera zobala mbewu, mitengo yobala zipatso za mbewu, molingana ndi mitundu yake.” Ndipo zinachitikadi.
12 A hooulu mai la ka honua i ka mauu, a me ka launahele e hua ana i ka hua ma kona ano iho, a me ka laau e hua ana i ka hua, iloko ona kona hua ma kona ano iho: nana iho la hoi ke Akua, ua maikai.
Dziko linabereka zomera zokhala ndi mbewu monga mwa mitundu yake ndi mitengo yokhala ndi zipatso za mbewu mʼkati mwake monga mwa mitundu yake. Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
13 A o ke ahiahi a me ke kakahiaka, o ke kolu ia o ka la.
Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachitatu.
14 I iho la ke Akua, I mau malamalama iloko o ke aouli o ka lani, i mea hookaawale i ke ao a me ka po; i mau hoailona lakou no na kau, a no na la, a me na makahiki:
Mulungu anati, “Pakhale zowunikira kuthambo kuti zilekanitse usana ndi usiku. Ndipo zimenezi zikhale zizindikiro zoonetsa nyengo, masiku ndi zaka;
15 I mau kukui hoi lakou iloko o ke aouli o ka lani, e hoomalamalama mai ai i ka honua: a pela io no.
zikhale kuthambo kuti ziwunikire pa dziko lapansi. Ndipo zinachitikadi.”
16 Hana iho la ke Akua i na malamalama nui elua: o ka malamalama nui, e alii ai maluna o ke ao, a o ka malamalama uuku iho, e alii ai maluna o ka po, a me na hoku hoi.
Mulungu anapanga zowunikira zazikulu ziwiri; chachikulu chilamulire usana ndi chachingʼono chilamulire usiku. Iye anapanganso nyenyezi.
17 Kau aku la ke Akua ia mau mea ma ke aouli o ka lani, e hoomalamalama mai ai i ka honua,
Mulungu anaziyika mlengalenga kuti ziziwunikira pa dziko lapansi,
18 E hooalii hoi maluna o ke ao a me ka po, a e hookaawale ae i ka malamalama a me ka pouli: a nana iho la ke Akua, ua maikai.
kuti zilamulire usana ndi usiku, ndi kuti zilekanitse kuwala ndi mdima. Mulungu anaona kuti zinali bwino.
19 A o ke ahiahi a me ke kakahiaka, o ka ha ia o ka la.
Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachinayi.
20 I iho la ke Akua, E hoohua nui mai na wai i na mea ola e holo ana, a me na manu e lele ae maluna o ka honua, ma ka lewa akea o ka lani.
Mulungu anati, “Mʼmadzi mukhale zamoyo zochuluka ndipo mbalame ziwuluke mlengalenga pamwamba pa dziko lapansi.”
21 Hana iho la ke Akua i na ia nui, a me na mea ola a pau e holo ana, a ka wai i hoohua nui mai ai ma ko lakou ano iho a me na mea eheu hoi a pau ma ko lakou ano iho: a nana iho la ke Akua, ua maikai.
Choncho Mulungu analenga zamoyo zikuluzikulu za mʼnyanja ndi chamoyo chamtundu uliwonse chokhala mʼmadzi ndi mbalame iliyonse ya mapiko monga mwa mtundu wake. Mulungu anaona kuti zinali bwino.
22 Hoomaikai iho la ke Akua ia mau mea, i iho la, E hoohua ae oukou e hoolaha nui hoi, a e hoopiha i na wai o na moana; a e hoolaha ae na manu maluna o ka honua.
Mulungu anazidalitsa nati, “Muswane, ndi kudzaza mʼmadzi a mʼnyanja, ndipo mbalame zichuluke pa dziko lapansi.”
23 O ke kakahiaka a me ke ahiahi, o ka lima ia o ka la.
Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachisanu.
24 I iho la ke Akua, E hoohua mai ka honua i ka mea ola ma kona ano iho, i ka holoholona laka, me ka mea kolo, a me ka holoholona hihiu ma kona ano iho: a pela io no.
Kenaka Mulungu anati, “Dziko lapansi litulutse zolengedwa zamoyo monga mwa mitundu yawo: ziweto, zolengedwa zokwawa ndi nyama zakuthengo, iliyonse monga mwa mtundu wake.” Ndipo zinaterodi.
25 Hana iho la ke Akua i ka holoholona hihiu ma kona ano iho, me na holoholona laka ma ko lakou ano iho, a me na mea kolo a pau o ka honua ma ko lakou ano iho: a nana iho la ke Akua, ua maikai.
Mulungu anapanga nyama zakuthengo monga mwa mitundu yawo, nyama zoweta monga mwa mitundu yawo ndi nyama zokwawa monga mwa mitundu yawo. Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
26 I iho la ke Akua, E hana kakou i ke kanaka o ku ia kakou, ma ka like ana me kakou iho: a e hooalii ia ia maluna o na ia o ke kai, maluna hoi o na manu o ka lewa, maluna hoi o na holoholona laka, a maluna hoi o ka honua a pau, a maluna no hoi o na mea kolo a pau e kolo ana ma ka honua.
Zitatha izi Mulungu anati, “Tipange munthu mʼchifanizo chathu, mofanana ndi ife kuti alamulire nsomba za mʼnyanja, mbalame zamlengalenga, nyama zonse zoweta ndi zonse zokwawa za pa dziko lapansi ndi zamoyo zonse zakutchire.”
27 Hana iho la ke Akua i ke kanaka ma kona ano iho, ma ke ano o ke Akua oia i hana'i ia ia; hana mai la ia i kane a i wahine.
Ndipo Mulungu analenga munthu mʼchifanizo chake. Anawalengadi mʼchifanizo cha Mulungu; analenga iwo, mwamuna ndi mkazi.
28 Hoomaikai mai la ke Akua ia laua, i mai la hoi ke Akua ia laua, E hoohua ae olua, e hoolaha hoi, e hoopiha i ka honua, a e lanakila maluna, a e noho alii maluna o na ia o ke kai, a me na manu o ka lewa, a me na mea a pau e kolo ana maluna o ka honua.
Mulungu anawadalitsa nati kwa iwo, “Muberekane, muchulukane, mudzaze dziko lapansi ndipo muligonjetse. Mulamulire nsomba zamʼnyanja, mbalame zamlengalenga ndi cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimayenda mokwawa pa dziko lapansi.”
29 I mai la ke Akua, Aia hoi, na haawi aku au na olua i na launahele a pau e hua ana i ka hua maluna o ka honua a pau, a me na laau a pau iloko ona ka hua o ka laau e hua ana i ka hua; he mea ai ia na olua.
Kenaka Mulungu anati, “Ine ndakupatsani chomera chilichonse cha pa dziko lapansi chimene chili ndi mbewu komanso mtengo uliwonse wobala zipatso zokhala ndi mbewu mʼkati mwake kuti zikhale chakudya chanu.
30 A na ka poe holoholona a pau o ka honua, me na manu a pau o ka lewa, a me na mea a pau e kolo ana ma ka honua, na mea e ola ana, na lakou ka nahelehele a pau i mea ai: a pela io no.
Ndaperekanso msipu kwa nyama zonse za pa dziko lapansi ndi kwa mbalame zamlengalenga ndi kwa cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimakwawa, chilichonse chimene chili ndi moyo.” Ndipo zinachitikadi.
31 Nana iho la ke Akua i na mea a pau ana i hana'i, aia hoi, ua maikai wale no. A o ke ahiahi a me ke kakahiaka, o ke ono ia o ka la.
Mulungu anaona zonse zimene anazilenga kuti zinali zabwino kwambiri. Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa, tsiku lachisanu ndi chimodzi.