< Kinohi 11 >

1 HOOKAHI no lehelehe, hookahi hoi olelo a ko ka honua a pau.
Nthawi imeneyo anthu onse a pa dziko lapansi ankayankhula chiyankhulo chimodzi ndipo mawu amene ankayankhula anali amodzi.
2 A i ko lakou hele ana mai ka hikina mai, loaa ia lakou kahi papu ma ka aina o Sinara; a noho iho la lakou ilaila.
Pamene anthu amapita chakummawa anapeza chigwa ku dziko la Sinara nakhazikikako.
3 Olelo ae la kekahi kanaka i kona hoa, Ina kakou, e hana kakou i na pohaku ula, e kahu a moa loa. O ko lakou pohaku, he pohaku ula, a he bitumena ko lakou puna.
Tsono anawuzana kuti, “Tiyeni tiwumbe njerwa ndi kuziwotcha bwinobwino.” Tsono mʼmalo mwa miyala anagwiritsa ntchito njerwa zowotcha, ndipo mʼmalo mwa matope anagwiritsa ntchito phula.
4 Olelo ae la lakou, Ina kakou, e hana kakou i kulanakauhale no kakou, a me ka halepakui e kiekie ae kona welau i ka lani; a e hookaulana i ko kakou inoa, o hoopuehuia'ku kakou maluna o ka honua a pau.
Kenaka anati, “Tiyeni tidzimangire mzinda wokhala ndi nsanja yoti ikafike kumwamba kuti titchuke. Kupanda kutero tibalalikana pa dziko lonse lapansi.”
5 Iho mai la o Iehova ilalo e nana i ke kulanakauhale a me ka halepakui a na keiki a kanaka i hana'i.
Koma Yehova anatsika kudzaona mzindawo ndi nsanja imene anthu aja ankayimanga.
6 I iho la o Iehova, Aia hoi, hookahi no ka poe kanaka, hookahi hoi ko lakou lehelehe; eia ka lakou e hoomaka nei e hana: a mahope aku, aohe mea keakea ia lakou ke hana i na mea a pau a lakou e manao ai.
Yehova anati, “Anthuwa ndi amodzi, ndipo ali ndi chiyankhulo chimodzi. Izi akuchitazi nʼchiyambi chabe cha zomwe akufuna kukwaniritsa kuchita.
7 Ina kakou, e iho iho kakou, a malaila kakou hookahuli ai i ka lakou olelo, i hoomaopopo ole ai lakou i ka olelo a kekahi.
Tiyeni titsikireko tikasokoneze chiyankhulo chawo kuti asamamvetsetsane.”
8 Pela o Iehova i hoopuehu aku ai ia lakou maluna o ka honua a pau: a oki iho la ka lakou hana ana i ua kulanakauhale la.
Choncho Yehova anabalalitsa anthu aja pa dziko lonse lapansi ndipo analeka kumanga mzindawo.
9 No ia mea, ua kapaia ka inoa o ia wahi, o Babela, no ka mea, ilaila o Iehova i hookahuli ai i ka olelo a ko ka honua a pau: a mai ia wahi aku i hoopuehu aku ai o Iehova ia lakou maluna o ka honua a pau.
Nʼchifukwa chake mzindawo unatchedwa Babeli, popeza Yehova anasokoneza chiyankhulo cha anthu onse. Powachotsa kumeneko, Yehova anawabalalitsira pa dziko lonse lapansi.
10 Eia ka mooolelo na Sema: hookani haneri makahiki o Sema, a hanau mai o Arepakada nana, elua makahiki mahope mai o ke kaiakahinalii.
Nayi mibado yochokera kwa Semu. Patapita zaka ziwiri chitatha chigumula, Semu ali ndi zaka 100, anabereka Aripakisadi.
11 Mahope mai o ka hanau ana o Arepakada, alima haneri no makahiki o ko Sema ola ana, a nana mai na keikikane a me na kaikamahine.
Atabereka Aripakisadi, Semu anakhala ndi moyo zaka 500 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
12 He kanakolu na makahiki a me kumamalima o ko Arepakada ola ana, a hanau mai o Sala nana:
Pamene Aripakisadi anali ndi zaka 35, anabereka Sela.
13 Mahope mai o ka hanau ana o Sala, aha haneri na makahiki a me kumamakolu o ko Arepakada ola ana, a nana mai na keikikane a me na kaikamahine.
Atabereka Sela, Aripakisadi anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
14 He kanakolu na makahiki o ko Sala ola ana, a hanau mai o Ebera nana:
Pamene Sela anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Eberi.
15 Mahope mai o ka hanau ana o Ebera, aha haneri na makahiki me kumamakolu o ko Sala ola ana, a nana mai na keikikane a me na kaikamahine.
Atabereka Eberi, Sela anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
16 He kanakolu na makahiki a me kumamaha o ko Ebera ola ana, a hanau mai o Pelega nana:
Pamene Eberi anali ndi zaka 34 anabereka Pelegi.
17 Mahope mai o ka hanau ana o Pelega, aha haneri na makahiki a me kanakolu o ko Ebera ola ana, a nana mai na keikikane a me na kaikamahine.
Atabereka Pelegi, Eberi anakhala ndi moyo zaka zina 430 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
18 He kanakolu na makahiki o ko Pelega ola ana, a hanau mai o Reu nana:
Pamene Pelegi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Reu.
19 Mahope mai o ko Reu hanau ana, alua haneri na makahiki a me kumamaiwa o ko Pelega ola ana, a nana mai na keikikane a me na kaikamahine.
Atabereka Reu, Pelegi anakhala zaka zina 209 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
20 He kanakolu na makahiki a me kumamalua o ko Reu ola ana, a hanau mai o Seruga nana:
Pamene Reu anali ndi zaka 32, anabereka Serugi.
21 Elua haneri na makahiki a me kumamahiku o ko Reu ola ana mahope mai o ka hanau ana o Seruga, a nana mai na keikikane a me na kaikamahine.
Atabereka Serugi, Reu anakhala ndi moyo zaka zina 207 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
22 He kanakolu na makahiki o ko Seruga ola ana, a hanau mai o Nahora nana:
Pamene Serugi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Nahori.
23 Mahope mai o ka hanau ana o Nahora, elua haneri na makahiki o ko Seruga ola ana, a nana mai na keikikane a me na kaikamahine.
Atabereka Nahori, Serugi anakhala ndi moyo zaka zina 200 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
24 He iwakalua na makahiki a me kumamaiwa o ko Nahora ola ana, a hanau mai o Tera nana:
Pamene Nahori anali ndi zaka 29, anabereka Tera.
25 Mahope mai o ka hanau ana o Tera, he haneri na makahiki a me ka umikumamaiwa o ko Nahora ola ana, a nana mai na keikikane a me na kaikamahine.
Atabereka Tera, Nahori anakhala ndi moyo zaka zina 119 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
26 He kanahiku na makahiki o ko Tera ola ana, a hanau mai o Aberama, o Nahora, a o Harana.
Pamene Tera anali ndi zaka 70, anabereka Abramu, Nahori ndi Harani.
27 Eia ka mooolelo no Tera; na Tera o Aberama, o Nahora, a o Harana; na Harana o Lota.
Nayi mibado yochokera mwa Tera. Tera anabereka Abramu, Nahori ndi Harani. Ndipo Harani anabereka Loti.
28 Make iho la o Harana mamua o kona makuakane o Tera, ma kona aina i hanau ai, ma Ura no ko Kaledea.
Abambo ake a Tera akanali ndi moyo, Harani anamwalira ku Uri wa ku Akaldeya kumene anabadwira.
29 Lawe ae la o Aberama laua o Nahora i mau wahine na laua: o Sarai ka inoa o ka wahine a Aberama, a o Mileka ka inoa o ka wahine a Nahora; oia ke kaikamahine a Harana, a ka makuakane o Mileka, a o ka makuakane hoi o Iseka.
Abramu ndi Nahori onse anakwatira. Dzina la mkazi wa Abramu linali Sarai, ndipo la mkazi wa Nahori linali Milika. Iyeyu ndi Isika abambo awo anali Harani.
30 A he pa o Sarai; aohe ana keiki.
Sarai analibe ana chifukwa anali wosabereka.
31 Lawe ae la o Tera i kana keiki ia Aberama, a me kana moopuna ia Lota, ke keiki a Harana, a me Sarai kana hunonawahine, o ka wahine a kana keiki a Aberama; a haele pu mai la lakou mai Ura mai no ko Kaledea, i ka hele ana ma ka aina o Kanaana: hiki mai la lakou i Harana, a noho iho la ilaila.
Tera anatenga mwana wake Abramu, mdzukulu wake Loti, ndi mpongozi wake Sarai, mkazi wa Abramu natuluka mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kupita ku Kanaani. Pamene anafika ku Harani, anakhazikika kumeneko.
32 O na la o Tera, elua ia haneri makahiki a me kumamalima: a make iho la o Tera ma Harana.
Tera anamwalira ku Harani ali ndi zaka 205.

< Kinohi 11 >