< Kekahuna 1 >

1 O NA olelo a ke kahuna, a ke keiki a Davida, oia ke alii ma Ierusalema.
Mawu a Mlaliki, mwana wa Davide, mfumu ya ku Yerusalemu:
2 Lapuwale o na lapuwale, wahi a ke kahuna; lapuwale o na lapuwale, pau loa na mea i ka lapuwale.
“Zopandapake! Zopandapake!” atero Mlaliki. “Zopandapake kotheratu! Zopandapake.”
3 Heaha ka uku i ke kanaka i ka hana a pau ana i hana'i malalo iho o ka la?
Kodi munthu amapindulanji pa ntchito zake zonse zimene amasautsidwa nazo pansi pano?
4 Hele aku la kekahi hanauna, a hele mai la kekahi hanauna; aka, ua mau no ka honua.
Mibado imabwera ndipo mibado imapita, koma dziko lapansi limakhalapobe nthawi zonse.
5 Puka mai ka la, a napoo ka la, a wikiwiki aku la ia ma kona wahi i puka mai ai.
Dzuwa limatuluka ndipo dzuwa limalowa ndipo limapita mwamsanga kumene limatulukira.
6 Puhi aku la ka makani i ke kukulu hema, a huli mai la ia i ke kukulu akau; huli ae la ia io, a io; a hoi hou ka makani i kona wahi i puhi ai.
Mphepo imawombera cha kummwera ndi kukhotera cha kumpoto; imawomba mozungulirazungulira, kumangobwererabwerera komwe yachokera.
7 Kahe aku la na muliwai a pau i ke kai, aole nae i piha ke kai; i kahi a lakou i kahe mai ai, malaila lakou e hoi hou aku ai.
Mitsinje yonse imakathira ku nyanja, koma nyanjayo sidzaza; kumene madziwo amachokera, amabwereranso komweko.
8 He mea luhi na olelo a pau, aole hiki i ke kanaka ke hai aku; aole i ana ka maka i ka ike ana, aole hoi i piha ka pepeiao i ka lohe ana.
Zinthu zonse ndi zotopetsa, kutopetsa kwake ndi kosaneneka. Maso satopa ndi kuona kapena khutu kukwaniritsidwa ndi kumva.
9 O na mea mamua, oia na mea e hiki mai ana; a o na mea i hanaia, oia na mea e hanaia mahope aku nei: aohe mea hou malalo iho o ka la.
Zomwe zinalipo kale zidzakhalaponso, zomwe zinachitika kale zidzachitikanso. Ndiye kuti chatsopano palibiretu pansi pano.
10 No kekahi mea e hiki anei ke olelo mai, Eia! he mea hou keia? he mea no ia i ka wa kahiko mamua loa o kakou.
Kodi chilipo chinthu chimene wina anganene kuti, “Taona! Ichi ndiye chatsopano?” Chinalipo kale, kalekale; chinalipo ife kulibe.
11 Aole i hoomanaoia mai na mea kahiko; a o na mea e hiki mai ana, aole e hoomanaoia ia mau mea e ka poe mahope aku.
Anthu akale sakumbukiridwa, ngakhale amene adzabwera mʼtsogolomu sadzakumbukiridwa ndi iwo amene adzabwere pambuyo pawo.
12 Owau o ke kahuna, ua noho au i alii maluna o ka Iseraela ma Ierusalema.
Ine, Mlalikine, ndinali mfumu ya Israeli mu Yerusalemu.
13 Ua haawi au i ko'u naau e imi, a e huli me ka noeau i na mea a pau i hanaia malalo iho o ka lani. He mea kaumaba loa keia a ke Akua i haawi mai ai i na keiki a kanaka e hana'i.
Ndinayika mtima wanga pophunzira ndi kufunafuna mwa nzeru zinthu zonse zimene zimachitika pansi pa thambo. Ndi ntchito yolemetsa ndithu imene Mulungu anayipereka kwa anthu!
14 Ua ike au i na mea a pau i hanaia malalo iho o ka lani, aia hoi, he mau mea lapuwale ia a pau a me ka luhi hewa.
Ine ndaona zinthu zonse zochitika pansi pano; zinthu zonsezo ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.
15 O na mea kekee, aole ia e hoopololeiia; a o ka mea nele, aole hiki ke helu aku.
Chinthu chokhota sichingathe kuwongoledwa; chimene palibe sichingathe kuwerengedwa.
16 Ua kukakuka au me ko'u naau iho, a i iho la, Ka! ua hookiekieia'ku au, a ua hoonui au i ka naauao mamua o na mea a pau ma Ierusalema; a ua hoomaopopo aku ko'u naau i ka noeau, a me ka ike.
Ine ndinaganiza mu mtima mwanga, “Taona, ine ndakula ndi kukhala wa nzeru zochuluka kupambana aliyense amene analamulirapo Yerusalemu ndisanabadwe; ndaphunzira nzeru zochuluka ndi luntha.”
17 A haawi au i ko'u naau e ike i ka naauao, a e ike no hoi i ka uhauha, a me ka lapuwale; a ike iho la au, he mea luhi hewa ia.
Ndipo ndinadzipereka kuti ndithe kumvetsa kuti nzeru nʼchiyani, misala nʼchiyani, uchitsiru nʼchiyani, koma ndinazindikira ichi, kuti kuteronso nʼkungodzivuta chabe.
18 No ka mea, ma ka naauao nui, malaila ke kaumaha; a o ka mea i hoonui i ka ike, hoonui no ia i ka eha.
Pakuti nzeru zochuluka zimabweretsa chisoni chochulukanso: chidziwitso chochuluka, zowawa zochulukanso.

< Kekahuna 1 >