< II Na Lii 15 >
1 I KA makahiki iwakaluakumamahiku o Ieroboama ke alii o ka Iseraela, i lilo ai o Azaria ke keiki a Amazia ke alii o ka Iuda, i alii.
Mʼchaka cha 27 cha Yeroboamu mfumu ya Israeli, Azariya mwana wa Amaziya mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
2 He umikumamaono kona mau makahiki i ka wa i lilo ai ia i alii, a he kanalimakumamalua na makahiki ana i alii ai ma Ierusalema. A o Iekolia ka inoa o kona makuwahine no Ierusalema.
Iye anakhala mfumu ali ndi zaka 16 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 52. Amayi ake anali Yekoliya wa ku Yerusalemu.
3 A hana pono aku la no ia imua o Iehova e like me na mea a pau a Amazia kona makuakane i hana'i.
Iyeyo anachita zabwino pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Amaziya abambo ake.
4 Aka hoi, aole i laweia'ku na heiau: kaumaha aku no na kanaka, a kuni hoi i ka mea ala ma na heiau.
Komabe malo opembedzerako mafano sanawachotse ndipo anthu anapitirizabe kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
5 A hahau mai o Iehova i ke alii, a lilo ia i lepera, a hiki i ka la o kona make ana, a noho ia ma ka hale no ka poe mai: a o Iotama ke keiki a ke alii, maluna o ka hale no oia e hooponopono ana i na kanaka o ka aina.
Ndipo Yehova analanga mfumu ndi nthenda ya khate mpaka tsiku limene inamwalira. Tsono mfumuyo inkakhala mʼnyumba yakeyake yapadera. Mwana wake Yotamu ndiye amene ankayangʼanira nyumba ya mfumu ndiponso ndiye amene ankalamulira anthu mʼdzikomo.
6 A o na hana i koe a Azaria, a me na mea a pau ana i hana'i, aole anei i kakauia lakou iloko o ka buke oihanaalii a na'lii o ka Iuda?
Ntchito zina za Azariya ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
7 A hiamoe iho la o Azaria me kona poe kupuna; a kanu iho la lakou ia ia me kona poe kupuna ma ke kulanakauhale o Davida; a noho alii iho la o Iotama, kana keiki, ma kona hakahaka.
Azariya anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Yotamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
8 I ka makahiki kanakolukumamawalu o Azaria ke alii o ka Iuda, i noho alii ai o Zakaria ke keiki a Ieroboama maluna o ka Iseraela ma Samaria i na malama eono.
Mʼchaka cha 38 cha Azariya mfumu ya Yuda, Zekariya mwana wa Yeroboamu anakhala mfumu ya Israeli ku Samariya ndipo analamulira miyezi isanu ndi umodzi.
9 Hana ino aku la ia imua o Iehova, e like me ka mea a kona mau kupuna i hana'i: aole ia i haalele i na hewa o Ieroboama ke keiki a Nebata, nana i hoolilo ka Iseraela i ka hewa.
Ndipo iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira makolo ake. Iye sanaleke machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
10 A o Saluma, ke keiki a Iabesa, kipi ae la oia ia ia, a pepehi aku la ia ia imua o na kanaka, a make iho la ia, a lilo ia i alii ma kona hakahaka.
Salumu mwana wa Yabesi anachitira chiwembu Zekariya. Anamukantha anthu akuona, namupha, ndipo analowa ufumu mʼmalo mwake.
11 A o na hana i koe a Zakaria, aia hoi, ua kakauia lakou iloko o ka buke oihanaalii a na'lii o ka Iseraela.
Ntchito zina za Zekariya, zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
12 Oia ka olelo a Iehova ana i olelo mai ai ia Iehu, i mai la, E noho kau poe keiki maluna o ka nohoalii o ka Iseraela, a hiki i ke kualua. A pela io no.
Awa ndiwo mawu a Yehova amene anayankhula kwa Yehu kuti, “Ana ako adzalamulira Israeli mpaka mʼbado wachinayi.”
13 O Saluma, ke keiki a Iabesa, noho alii iho la ia i ka makahiki kanakolukumamaiwa o Uzia ke alii o ka Iuda; a o na la ana i noho alii ai ma Samaria, hookahi ia malama.
Salumu mwana wa Yabesi anakhala mfumu mʼchaka cha 39 cha ulamuliro wa Uziya mfumu ya Yuda ndipo analamulira mu Samariya mwezi umodzi.
14 No ka mea, pii ae la o Menahema, ke keiki a Gadi mai Tireza aku, a hele mai i Samaria, a pepehi aku la ia Saluma ke keiki a Iabesa ma Samaria, a make, a noho alii iho la ia ma kona hakahaka.
Ndipo Menahemu mwana wa Gadi anachoka ku Tiriza napita ku Samariya nakantha Salumu mwana wa Yabesi ku Samariya, namupha ndipo iye analowa ufumu mʼmalo mwake.
15 A o na hana i koe a Saluma, a me kona kipi ana i kipi ai, aia hoi, ua kakauia lakou iloko o ka buke oihanaalii a na'lii o ka Iseraela.
Ntchito zina za Salumu ndiponso za chiwembu chimene anachita, zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
16 Ia manawa luku aku la o Menahema i Tipesa, a me na mea a pau iloko ona, a me kolaila mau mokuna mai Tireza mai: no ka mea, aole lakou i wehe ae, no ia mea, luku aku la ia; a kaha aku la ia i kolaila poe wahine hapai a pau.
Nthawi imeneyo Menahemu, kuchokera ku Tiriza, anakathira nkhondo mzinda wa Tipisa ndi anthu onse amene anali mʼmenemo ndi dera lonse lozungulira chifukwa iwo anakana kutsekula zipata zawo. Iye anatenga katundu yense mu mzinda wa Tipisa ndi kutumbula akazi onse oyembekezera.
17 I ka makahiki kanakolukumamaiwa o Azaria ke alii o ka Iuda, i lilo ai o Menahema ke keiki a Gadi i alii maluna o ka Iseraela, he umi makahiki ana i noho alii ai ma Samaria.
Mʼchaka cha 39 cha Azariya mfumu ya Yuda, Menahemu mwana wa Gadi anakhala mfumu ya Israeli ndipo analamulira mu Samariya zaka khumi.
18 A hana ino aku la ia imua o Iehova: i kona mau la a pau, aole ia i haalele i na hewa o Ieroboama ke keiki a Nebata, nana i hoolilo ka Iseraela i ka hewa.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova. Nthawi yonse ya ulamuliro wake sanasiye machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
19 Hele mai o Pula ke alii o Asuria i ka aina; a haawi aku la o Menahema ia Pula i hookahi tausani talena kala, i kokua mai ai kela ia ia e hookupaa i ke aupuni iloko o kona lima.
Tsono Puli mfumu ya ku Asiriya inadzathira nkhondo dzikolo ndipo Menahemu anapatsa Puliyo makilogalamu 34,000 a siliva kuti amuthandize ndi kulimbikitsa ufumu wake.
20 A auhau aku la o Menahema i ke kala i ka Iseraela, i ka poe mea waiwai nui, i keia kanaka kela kanaka he kanaliina sekela e haawi aku i ke alii o Asuria: a hoi aku la ke alii o Asuria, aole ia i hookaulua malaila iloko o ka aina.
Menahemu anapeza ndalamazo kudzera mu msonkho umene ankakhometsa Aisraeli. Munthu aliyense wachuma ankapereka masekeli a siliva makumi asanu kwa mfumu ya ku Asiriya. Choncho mfumu ya ku Asiriya inabwerera ndipo sinakhalenso mʼdzikomo.
21 A o na hana i koe a Menahema, a me na mea a pau ana i hana'i, aole anei i kakauia lakou iloko o ka buke oihanaalii a na'lii o ka Iseraela?
Ntchito zina za Menahemu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
22 A hiamoe iho la o Menahema me kona poe kupuna: a noho alii iho la o Pekahia kana keiki ma kona hakahaka.
Menahemu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Pekahiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
23 I ka makahiki kanalima o Azaria ke alii o ka Iuda, i lilo ai o Pekahia ke keiki a Menahema i alii maluna o ka Iseraela, ma Samaria, elua makahiki ana i alii ai.
Mʼchaka cha makumi asanu a Azariya mfumu ya Yuda, Pekahiya mwana wa Menahemu anakhala mfumu ya Israeli mu Samariya ndipo analamulira zaka ziwiri.
24 Hana ino aku la ia imua o Iehova; aole ia i haalele i na hewa o Ieroboama ke keiki a Nebata nana i hoolilo ka Iseraela i ka hewa.
Pekahiya anachita zoyipa pamaso pa Yehova. Iye sanaleke machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, omwe anachimwitsa nawo Israeli.
25 A o Peka ke keiki a Remalia, he luna koa nona, kipi mai la oia ia ia, a pepehi iho la ia ia ma Samaria iloko o kahi paa o ka halealii, a me Aregoba, a me Arie, a i na kanaka he kanalima me ia no Gileada; a make iho la ia, a lilo kela i alii ma kona hakahaka.
Ndipo Peka mwana wa Remaliya, mtsogoleri wake wa ankhondo, anamuchita chiwembu. Iye pamodzi ndi anthu makumi asanu a ku Giliyadi anapha Pekahiya pamodzi ndi Arigobu ndi Ariyeli mʼchipinda choteteza nyumba ya mfumu mu Samariya. Kotero Peka anapha Pekahiya ndipo analowa ufumu mʼmalo mwake.
26 A o na hana i koe a Pekahia, a o na mea a pau ana i hana'i, aia hoi, ua kakauia lakou iloko o ka buke oihanaalii a na'lii o ka Iseraela.
Ntchito zina za Pekahiya ndi zonse zimene anachita zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
27 I ka makahiki kanalimakumamalua o Azaria ke alii o ka Iuda, i lilo ai o Peka ke keiki a Remalia i alii maluna o ka Iseraela ma Samaria, he iwakalua na makahiki ana i alii ai.
Mʼchaka cha 52 cha Azariya mfumu ya Yuda, Peka mwana wa Remaliya anakhala mfumu ya Israeli ku Samariya ndipo analamulira zaka makumi awiri.
28 A hana ino aku la ia imua o Iehova; aole ia i haalele i na hewa a Ieroboama ke keiki a Nebata, nana i hoolilo ka Iseraela i ka hewa.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova. Sanaleke machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
29 I ka manawa ia Peka ke alii o ka Iseraela, hele mai o Tigelatepilesera ke alii o Asuria, a hoopio i ko Iiona, a me ko Abelebetemaaka, a me ko Ianoa, a me ko Kadesa, a me ko Hazora, a me ko Gileada, a me ko Galilaia, i ko ka aina a pau o Napetali, a lawe pio aku la ia lakou i Asuria.
Nthawi ya Peka mfumu ya Israeli, Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya anabwera ndi kudzalanda Iyoni, Abeli-Beti-Maaka, Yanowa, Kedesi ndi Hazori. Mfumu ya ku Asiriya inatenga Giliyadi ndi Galileya, kuphatikizanso madera onse a Nafutali ndipo anatumiza Aisraeli ku Asiriya.
30 A kipi ae la o Hosea, ke keiki a Ela, ia Peka, ke keiki a Remalia, a pepehi aku la ia ia, a noho alii iho la ia ma kona wahi, i ka makahiki iwakalua o Iotama, ke keiki a Uzia.
Kenaka Hoseya mwana wa Ela anachitira chiwembu Peka mwana wa Remaliya. Anamukantha ndi kumupha ndipo anakhala mfumu mʼmalo mwake mʼchaka makumi awiri cha Yotamu mwana wa Uziya.
31 A o na hana i koe a Peka, a o na mea a pau ana i hana'i, aia hoi, ua kakauia lakou iloko o ka buke oihanaalii a na'lii o ka Iseraela.
Ntchito zina za Peka ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
32 I ka lua o ka makahiki o Peka ke keiki a Remalia ke alii o ka Iseraela, i lilo ai o Iotama, ke keiki a Uzia, ke alii o ka Iuda i alii.
Mʼchaka chachiwiri cha Peka mwana wa Remaliya mfumu ya Israeli, Yotamu mwana wa Uziya mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
33 He iwakaluakumamalima na makahiki ona i kona manawa i lilo ai i alii, a he umikumamaono na makahiki ana i alii ai ma Ierusalema. A o Ierusa ka inoa o kona makuwahine, ke kaikamahine ia na Zadoka.
Iye anakhala mfumu ali ndi zaka 25 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 16. Amayi ake anali Yerusa mwana wa Zadoki.
34 A hana pono aku la ia imua o Iehova, e like me na mea a pau a Uzia kona makuakane i hana'i.
Iye anachita zabwino pamaso pa Yehova monga anachitira Uziya abambo ake.
35 Aka hoi, aole i laweia'ku na heiau: kaumaha aku no na kanaka, a kuni hoi i ka mea ala ma na heiau. Hana aku no ia i ka puka kiekie o ka hale o Iehova.
Komabe malo opembedzera mafano sanawachotse ndipo anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
36 A o na hana i koe a Iotama, a o na mea a pau ana i hana'i, aole anei i kakauia lakou iloko o ka buke oihanaalii a na'lii o ka Iuda?
Ntchito zina za Yotamu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
37 Ia mau la hoomaka iho la o Iehova e hoouna aku ia Rezina ke alii o Suria, a me Peka ke keiki a Remalia e ku e i ka Iuda.
(Nthawi imeneyo, Yehova anayamba kumatuma Rezini mfumu ya Aaramu ndi Peka mwana wa Remaliya kudzamenyana ndi Yuda).
38 A hiamoe iho la o Iotama me kona poe kupuna, a kanuia oia me kona poe kupuna ma ke kulanakauhale o Davida kona kupuna; a noho alii iho la o Ahaza kana keiki ma kona wahi.
Yotamu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide abambo ake. Ndipo Ahazi mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.