< Zabura 91 >
1 Shi wanda yake zama a wurin Mafi Ɗaukaka zai huta a cikin inuwar Maɗaukaki.
Iye amene amakhala mu mthunzi wa Wammwambamwamba adzapuma mu mthunzi wa Wamphamvuzonse.
2 Zan ce game da Ubangiji, “Shi ne mafakata da kagarata, Allahna, wanda nake dogara.”
Ndidzanena za Yehova, “Iye ndiye pothawira panga ndi linga langa, Mulungu wanga amene ndimadalira.”
3 Tabbatacce zai cece ka daga tarkon mai farauta da kuma daga cututtuka masu kisa.
Ndithu, Iye adzakupulumutsa ku msampha wa mlenje ndi ku mliri woopsa;
4 Zai rufe ka da fikafikansa, a ƙarƙashin fikafikansa kuwa za ka sami mafaka; amincinsa zai zama maka garkuwa da katanga.
Adzakuphimba ndi nthenga zake, ndipo udzapeza malo othawira mʼmapikomo; kukhulupirika kwake kudzakhala chishango chako ndi lihawo.
5 Ba za ka ji tsoron razanar dare, ko kibiyoyi da suke firiya da rana ba,
Sudzachita mantha ndi zoopsa za usiku, kapena muvi wowuluka masana,
6 ko bala’in da yake aukowa cikin duhu, ko annobar da take hallakarwa da tsakar rana.
kapena mliri umene umayenda mu mdima, kapena zowononga za pa nthawi ya masana.
7 Dubu za su iya fāɗuwa a gefenka, dubu goma a hannun damanka, amma ba abin da zai zo kusa da kai.
Anthu 1,000 atha kufa pambali pako, anthu 10,000 kudzanja lako lamanja, koma zoopsazo sizidzafika pafupi ndi iwe.
8 Za ka dai gan da idanunka yadda ake hukunta mugaye.
Udzapenya ndi maso ako ndipo udzaona mmene anthu oyipa amalangidwira.
9 In ka mai da Mafi Ɗaukaka wurin zamanka, har ma Ubangiji wanda yake mafakata,
Pakuti wasankha Wammwambamwamba kukhala malo ako okhalamo; wavomera Yehova kukhala kothawira kwako.
10 to, babu wani mugun abin da zai same ka, ba masifar da za tă zo kusa da tentinka.
Choncho palibe choyipa chimene chidzakugwera, zoopsa sizidzafika pafupi ndi tenti yako.
11 Gama zai umarci mala’ikunsa game da kai don su tsare ka a dukan hanyoyinka;
Pakuti adzalamulira angelo ake za iwe, kuti akutchinjirize mosamala pa njira zako zonse;
12 za su tallafe ka da hannuwansu, don kada ka buga ƙafarka a kan dutse.
ndipo adzakunyamula ndi manja awo, kuti phazi lako lisagunde pa mwala.
13 Za ka taka zaki da gamsheƙa; za ka tattake babban zaki da maciji.
Udzapondaponda mkango ndi njoka, udzapondereza mkango wamphamvu ndiponso chinjoka.
14 Ubangiji ya ce, “Domin ya ƙaunace ni, zan kuɓutar da shi; zan kiyaye shi, gama ya yarda da sunana.
“Chifukwa iye amandikonda,” akutero Yehova, “Ndidzamulanditsa; ndidzamuteteza pakuti wavomereza dzina langa.
15 Zai kira bisa sunana, zan kuma amsa masa; zan kasance tare da shi a lokacin wahala, zan kuɓutar da shi in kuma girmama shi.
Adzandiyitana, ndipo ndidzamuyankha; ndidzakhala naye pa mavuto, ndidzamupulumutsa ndi kumulemekeza.
16 Da tsawon rai zan ƙosar da shi in kuma nuna masa cetona.”
Ndidzamupatsa moyo wautali ndi kumupulumutsa.”