< Zabura 63 >
1 Zabura ta Dawuda. Sa’ad da yake a hamadar Yahuda. Ya Allah, kai ne Allahna, da nacewa na neme ka; raina yana ƙishinka, jikina yana marmarinka, cikin busasshiyar ƙasar da ta zozaye inda babu ruwa.
Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda. Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga, moona mtima ine ndimakufunafunani; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu, thupi langa likulakalaka inu, mʼdziko lowuma ndi lotopetsa kumene kulibe madzi.
2 Na gan ka a wuri mai tsarki na kuma dubi ikonka da ɗaukakarka.
Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.
3 Domin ƙaunarka ta fi rai kyau, leɓunana za su ɗaukaka ka.
Chifukwa chikondi chanu ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.
4 Zan yabe ka muddin raina, kuma a cikin sunanka zai ɗaga hannuwana.
Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga, ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.
5 Raina zai ƙoshi kamar da abinci mafi kyau; da leɓunan rerawa bakina zai yabe ka.
Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona. Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.
6 A gadona na tuna da kai; ina tunaninka dukan dare.
Pa bedi panga ndimakumbukira inu; ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.
7 Domin kai ne mai taimakona, ina rera a cikin inuwar fikafikanka.
Chifukwa ndinu thandizo langa, ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.
8 Raina ya manne maka; hannunka na dama yana riƙe da ni.
Moyo wanga umakangamira Inu; dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.
9 Su da suke neman raina za su hallaka; za su gangara zuwa zurfafan duniya.
Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa; adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.
10 Za a bayar da su ga takobi su kuma zama abincin karnukan jeji.
Iwo adzaperekedwa ku lupanga ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.
11 Amma sarki zai yi farin ciki ga Allah; dukan waɗanda suke rantse da sunan Allah za su yabe shi, amma za a rufe bakunan maƙaryata.
Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu; onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo, koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.