< Zabura 148 >

1 Yabi Ubangiji. Yabi Ubangiji daga sammai, yabe shi a bisa sammai.
Tamandani Yehova. Tamandani Yehova, inu a kumwamba, mutamandeni Iye, inu a mlengalenga.
2 Yabe shi, dukanku mala’ikunsa, yabe shi, dukanku rundunarsa na sama.
Mutamandeni, inu angelo ake onse, mutamandeni, mutamandeni, inu zolengedwa za mmwamba.
3 Yabe shi, rana da wata, yabe shi, dukanku taurari masu haskakawa.
Mutamandeni, inu dzuwa ndi mwezi, mutamandeni, inu nonse nyenyezi zowala.
4 Yabe shi, ku bisa sammai da kuma ku ruwan bisa sarari.
Mutamandeni, inu thambo la kumwambamwamba ndi inu madzi a pamwamba pa thambo.
5 Bari su yabi sunan Ubangiji, gama ya umarta aka kuwa halicce su.
Zonse zitamande dzina la Yehova pakuti Iye analamula ndipo zinalengedwa.
6 Ya sa su a wurarensu har abada abadin; ya ba da umarnin da ba zai taɓa shuɗe ba.
Iye anaziyika pa malo ake ku nthawi za nthawi; analamula ndipo sizidzatha.
7 Yabi Ubangiji daga duniya, ku manyan halittun teku da kuma dukan zurfafan teku,
Tamandani Yehova pa dziko lapansi, inu zolengedwa zikuluzikulu za mʼnyanja, ndi nyanja zonse zakuya,
8 walƙiya da ƙanƙara, dusar ƙanƙara da gizagizai, hadirin iskar da suke biyayya da umarnansa,
inu zingʼaningʼani ndi matalala, chipale ndi mitambo, mphepo yamkuntho imene imakwaniritsa mawu ake,
9 ku duwatsu da dukan tuddai, itatuwa masu’ya’ya da dukan al’ul,
inu mapiri ndi zitunda zonse, inu mitengo ya zipatso ndi mikungudza yonse,
10 namun jeji da dukan dabbobin gida, ƙanana halittu da tsuntsaye masu firiya,
inu nyama zakuthengo ndi ngʼombe zonse, inu zolengedwa zingʼonozingʼono ndi mbalame zowuluka.
11 sarakunan duniya da dukan al’ummai, ku sarakuna da dukan masu mulkin duniya,
Inu mafumu a dziko lapansi ndi anthu a mitundu yonse, inu akalonga ndi olamulira a dziko lapansi.
12 samari da’yan mata, tsofaffi da yara.
Inu anyamata ndi anamwali, inu nkhalamba ndi ana omwe.
13 Bari su yabi sunan Ubangiji, gama sunansa ne kaɗai mafi ɗaukaka; darajarsa ta fi ƙarfin duniya da sammai.
Onsewo atamande dzina la Yehova pakuti dzina lake lokha ndi lolemekezeka; ulemerero wake ndi woopsa pa dziko lapansi pano ndi kumwamba komwe.
14 Ya tayar wa mutanensa ƙaho, yabon dukan tsarkakansa, na Isra’ila, mutanen da suke kurkusa da zuciyarsa. Yabi Ubangiji.
Iye wakwezera nyanga anthu ake, matamando a anthu ake onse oyera mtima, Aisraeli, anthu a pamtima pake. Tamandani Yehova.

< Zabura 148 >