< Zabura 118 >
1 Ku gode wa Ubangiji, gama nagari ne shi; ƙaunarsa madawwamiya ce har abada.
Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
2 Bari Isra’ila yă ce, “Ƙaunarsa madawwamiya ce har abada.”
Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
3 Bari gidan Haruna yă ce, “Ƙaunarsa madawwamiya ce har abada.”
Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
4 Bari waɗanda suke tsoron Ubangiji su ce, “Ƙaunarsa madawwamiya ce har abada.”
Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
5 Cikin azabata na yi kuka ga Ubangiji, ya kuwa amsa ta wurin’yantar da ni.
Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
6 Ubangiji yana tare da ni; ba zan ji tsoro ba. Me mutum zai yi mini?
Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
7 Ubangiji yana tare da ni; shi ne mai taimakona. Zan yi nasara a kan abokan gābana.
Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
8 Ya fi kyau in nemi mafaka a wurin Ubangiji da in dogara ga mutum.
Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
9 Ya fi kyau in nemi mafaka a wurin Ubangiji da in dogara ga sarakuna.
Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
10 Dukan al’ummai sun kewaye ni, amma a cikin sunan Ubangiji na hallaka su.
Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
11 Sun kewaye ni a kowane gefe, amma a cikin sunan Ubangiji na hallaka su.
Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
12 Sun rufe ni kamar ƙudan zuma, amma suka mutu nan da nan kamar ƙayayyuwa masu cin wuta; a cikin sunan Ubangiji na hallaka su.
Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
13 An ture ni baya na kusa fāɗuwa, amma Ubangiji ya taimake ni.
Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
14 Ubangiji ne ƙarfina da waƙata; ya zama mai cetona.
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
15 Sowa ta farin ciki da nasara sun fito a cikin tentunan adalai, “Hannun dama na Ubangiji ya aikata manyan abubuwa!
Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
16 An ɗaga hannun dama na Ubangiji sama; hannun dama na Ubangiji ya aikata manyan abubuwa!”
Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
17 Ba zan mutu ba amma zan rayu, zan kuwa yi shelar abin da Ubangiji ya yi.
Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
18 Ubangiji ya hore ni sosai, amma bai ba da ni ga mutuwa ba.
Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
19 Buɗe mini ƙofofin adalci; zan shiga in kuma yi godiya ga Ubangiji.
Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
20 Wannan ne ƙofar Ubangiji inda adalai za su shiga.
Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
21 Zan yi maka godiya, domin ka amsa mini; ka zama mai cetona.
Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
22 Zabura Dutsen da magina suka ƙi ya zama mai amfani;
Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
23 Ubangiji ne ya yi haka, kuma abu mai daraja ne a idanunmu.
Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
24 Wannan ita ce ranar da Ubangiji ya yi; bari mu yi farin ciki mu kuma yi murna a cikinta.
Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
25 Ya Ubangiji, ka cece mu; Ya Ubangiji, ka ba mu nasara.
Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
26 Mai albarka ne shi mai zuwa cikin sunan Ubangiji. Daga gidan Ubangiji muna sa muku albarka.
Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
27 Ubangiji shi ne Allah ya kuma sa haskensa ya haskaka a kanmu. Da kwanoni a hannunmu, muka shiga jerin gwanon biki ku kai su ƙahoni na bagade.
Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
28 Kai ne Allahna, zan kuwa yi maka godiya; kai ne Allahna, zan kuwa ɗaukaka ka.
Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
29 Ku gode wa Ubangiji, gama nagari ne shi; ƙaunarsa madawwamiya ce har abada.
Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.