< Ishaya 17 >

1 Abin da Allah ya faɗa game da Damaskus. “Duba, Damaskus ba za tă ƙara zama birni ba amma za tă zama tsibin juji.
Uthenga wonena za Damasiko: “Taonani, mzinda wa Damasiko sudzakhalanso mzinda, koma udzasanduka bwinja.
2 Za a watse a bar biranen Arower a bar wa tumaki da shanu, waɗanda za su kwanta, ba tare da wani wanda zai tsorata su ba.
Mizinda ya Aroeri idzakhala yopanda anthu ndipo idzakhala ya ziweto, zimene zidzagona pansi popanda wina woziopseza.
3 Birni mai katanga za tă ɓace daga Efraim, ikon sarauta kuma daga Damaskus; raguwar Aram za tă zama kamar darajar Isra’ila,” in ji Ubangiji Maɗaukaki.
Ku Efereimu sikudzakhalanso linga, ndipo ku Damasiko sikudzakhalanso ufumu; Otsalira a ku Siriya adzachotsedwa ulemu monga anthu a ku Israeli,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
4 “A wannan rana ɗaukakar Yaƙub za tă ƙare; kitsen jikinsa zai lalace.
“Tsiku limenelo ulemerero wa Yakobo udzazimirira; ndipo chuma chake chidzasanduka umphawi.
5 Zai zama kamar sa’ad da mai girbi ya tara hatsin da yake tsaye ya kuma girbe hatsin da hannunsa kamar sa’ad da mutum ya yi kala kawunan hatsi a Kwarin Refayim.
Israeli adzakhala ngati munda wa tirigu umene anatsiriza kukolola. Adzakhalanso ngati munda wa mʼchigwa cha Refaimu anthu atatha kukunkha ngala za tirigu.
6 Duk da haka waɗansu kala za su ragu, sai ka ce sa’ad da an karkaɗe itace zaitun, aka bar’ya’yan zaitun biyu ko uku a can ƙwanƙolin rassan, ko kuma aka bar huɗu ko biyar a rassa na gefe na itace mai’ya’ya,” in ji Ubangiji, Allah na Isra’ila.
Komabe Aisraeli ochepa okha ndiwo ati adzatsale monga mʼmene zimatsalira zipatso ziwiri kapena zitatu pa nthambi ya pamwamba penipeni kapena zipatso zisanu pa nthambi za mʼmunsi mwa mtengo wa olivi akawugwedeza,” akutero Yehova, Mulungu wa Israeli.
7 A wannan rana mutane za su nemi Mahaliccinsu su kuma juye idanunsu ga Mai Tsarkin nan na Isra’ila.
Tsiku limenelo anthu adzayangʼana Mlengi wawo ndipo adzatembenukira kwa Woyerayo wa Israeli.
8 Ba za su dubi bagade ba, waɗanda suke aikin hannuwansu, ba za su kuma kula da ginshiƙan Ashera ba da kuma bagadan turaren da yatsotsinsu suka yi.
Iwo sadzakhulupiriranso maguwa ansembe, ntchito ya manja awo, ndipo sadzadaliranso mitengo ya mafano a Asera, ndiponso maguwa ofukizirapo lubani amene manja awo anapanga.
9 A wannan rana biranensu masu ƙarfi, waɗanda suka bari saboda Isra’ilawa, za su zama kamar wuraren da aka ƙyale suka zama kufai a jeji. Za su kuma zama kango.
Tsiku limenelo mizinda yawo yamphamvu, imene anasiya chifukwa cha Aisraeli, idzakhala ngati malo osiyidwa kuti awirire ndi kumera ziyangoyango. Ndipo yonse idzakhala mabwinja.
10 Kun manta da Allah Mai Cetonku; ba ku tuna da Dutse, kagararku ba. Saboda haka, ko da yake kun fita ku shuka tsire-tsire mafi kyau kuka kuma shuka inabin da aka sayo daga waje,
Inu mwayiwalatu Mulungu Mpulumutsi wanu; simunakumbukire Thanthwe, linga lanu. Choncho, ngakhale munadzala mbewu zabwino, ndi kuyitanitsa kunja mitengo ya mpesa,
11 ko da yake a ranar kun shuka su, kuka sa su yi girma, da safe kuma sa’ad da kuka shuka su, kuka sa suka yi toho suka yi fure, duk da haka girbin ba zai zama kome ba a ranar cuta da zafin da ba ta da magani.
nimuyembekeza kuti zikule tsiku lomwelo ndi kuphukira maluwa mmawa mwake, komabe zimenezi sizidzakupindulirani pa tsiku la mavuto.
12 Kash, ga hayaniyar al’ummai masu yawa suna hayaniya kamar rurin teku! Kash, ga fushin mutane suna ruri kamar rugugi kamar manyan ruwaye!
Aa, mkokomo wa anthu a mitundu yambiri, akusokosa ngati kukokoma kwa nyanja! Aa, phokoso la anthu a mitundu ina, akusokosa ngati mkokomo wa madzi amphamvu!
13 Ko da yake mutane suna ruri kamar sukuwar raƙuman ruwa, sa’ad da ya tsawata musu za su gudu can da nisa, aka kore su kamar yayinda iska ya hura a kan tuddai, kamar tattake kuma a cikin guguwa.
Ngakhale ankhondo a mitundu ina akubwera ndi mkokomo ngati wa madzi ambiri, koma adzathawira kutali Mulungu akadzawadzudzula. Yehova adzawapirikitsa ngati mankhusu owuluka ndi mphepo pa phiri, ndi ngati fumbi la kamvuluvulu asanayambe.
14 Da yamma, sai razana ba tsammani! Kafin safiya, duk sun ɓace! Wannan ne rabon waɗanda suka washe mu, rabon waɗanda suka yi mana ƙwace.
Pofika nthawi yamadzulo zoopsa zidzayamba kuchitika, ndipo zidzakhala zitatha pofika mmawa. Izi ndizo zidzachitikire anthu otilanda zinthu, gawo la amene amatibera zinthu zathu.

< Ishaya 17 >