< Jòb 5 >

1 “Rele koulye a; èske gen moun ki pou reponn? A kilès nan sen fidèl yo ke ou va vire?
“Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe? Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?
2 Paske rankin va touye moun ki plen foli, e jalouzi va touye moun senp lan.
Mkwiyo umapha chitsiru, ndipo njiru imawononga wopusa.
3 Mwen te wè moun san konprann ki t ap pran rasin, e byen vit, mwen te denonse kay li.
Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu, koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.
4 Fis li yo pa jwenn sekirite ditou; menm nan pòtay la, yo oprime, ni pa gen moun pou delivre yo.
Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe; amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.
5 Moun grangou yo devore rekòlt li, e mennen l yon kote plen pikan. Epi pelen an rete ovèt pou sezi tout byen yo.
Anthu anjala amamudyera zokolola zake, amamutengera ndi za pa minga pomwe, ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.
6 Paske malè pa sòti nan pousyè, ni gwo twoub pa pouse soti nan tè;
Pakuti masautso satuluka mʼfumbi, ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.
7 paske lòm fèt pou gwo twoub, tankou etensèl dife vole anlè.
Komatu munthu amabadwira kuti azunzike monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.
8 “Men pou mwen, mwen ta chache Bondye, pou m ta plede kòz mwen devan Bondye.
“Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu; ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.
9 Bondye Ki konn fè gwo bagay ki depase konesans lan; mèvèy ki pa kab menm konte yo.
Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.
10 Li bay lapli sou tè a, e voye dlo sou chan yo,
Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi, ndipo amathirira minda ya anthu.
11 Jiskaske Li leve sila ki enb yo, e sila ki an dèy yo, li leve bay sekou.
Iye amakweza anthu wamba, ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
12 Li anile manèv a sila ki gen riz yo pou men yo pa reyisi.
Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera, kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.
13 Li kaptire saj yo nan pwòp riz pa yo, e konsèy a moun k ap twonpe moun nan vin kontrekare byen vit.
Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo, ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.
14 Nan gwo lajounen, yo jwenn ak tenèb, e yo egare gwo midi tankou se te lannwit.
Mdima umawagwera nthawi yamasana; nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.
15 Men li sove yo de nepe a pwop bouch yo, e menm malere a chape nan men pwisan an.
Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo; amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.
16 Akoz sa, sila ki san sekou a gen espwa, e inikite oblije pe bouch li.
Choncho osauka ali ndi chiyembekezo, ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.
17 “Gade byen kijan nonm ke Bondye bay chatiman an gen kè kontan. Konsa, pa meprize disiplin Toupwisan an.
“Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula; nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.
18 Paske se Li menm ki blese, e se Li menm ki retire blesè a; Li fè donmaj la, e pwòp men L ki geri l.
Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo; Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.
19 Soti sis fwa, Li va delivre ou de twoub ou yo; Menm nan sèt fwa, mal la p ap kab touche ou.
Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi, mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.
20 Nan gwo grangou Li va delivre ou devan lanmò, e nan lagè, devan pouvwa nepe a.
Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa, ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.
21 Ou va pwoteje devan blese a lang lan, e ou p ap pè vyolans lan lè l vin parèt.
Adzakuteteza kwa anthu osinjirira, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.
22 Ou va ri devan vyolans ak grangou, e ou p ap pè bèt sovaj yo.
Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.
23 Paske ou va fè alyans ak wòch chan yo, e bèt sovaj yo va anpè avèk ou.
Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako, ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.
24 Ou va konnen ke tant ou an pwoteje, paske ou va vizite lakay ou san krent ni pèt.
Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa; udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.
25 Anplis, ou va konnen ke desandan ou yo va anpil, e sila ki sòti nan ou yo anpil tankou zèb latè.
Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri, ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.
26 Ou va rive nan tonbo a ak tout fòs ou, tankou gwo sak ble nan sezon li.
Udzafika ku manda utakalamba, monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.
27 Gade sa byen; nou te fè ankèt li, e se konsa li ye. Tande sa e konnen l pou kont ou.”
“Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona, choncho uzimvere ndi kuzitsata.”

< Jòb 5 >