< Ezayi 32 >

1 Gade byen, yon wa va renye ak ladwati e prens yo va renye ak jistis.
Taonani, kudzakhala mfumu ina imene idzalamulira mwachilungamo, ndipo akalonga ake adzaweruza molungama.
2 Yon nonm va tankou yon abri kont van ak yon pwotèj kont tanpèt, tankou sous dlo nan yon peyi sèch, tankou lonbraj a yon gwo wòch nan yon peyi ki deseche.
Munthu aliyense adzakhala ngati pothawirapo mphepo ndi malo obisalirapo namondwe, adzakhala ngati mitsinje ya mʼchipululu, ngati mthunzi wa thanthwe lalikulu la mʼdziko lowuma.
3 Alò, zye a sila ki wè yo, p ap vin avegle; zòrèy a sila ki tande yo, va koute.
Ndipo maso a anthu openya sadzakhalanso otseka, ndipo makutu a anthu akumva adzamvetsetsa.
4 Kè a sila ki aji san reflechi a va konprann verite, e lang lan a sila ki bege a va pale klè.
Anthu a mtima wopupuluma adzadziwa ndi kuchita zinthu mofatsa, ndipo anthu ovutika kuyankhula adzayankhula mosadodoma ndi momveka.
5 Li p ap rive ankò ke yo rele moun fou, prens; ni rele vakabon, moun bon kè.
Chitsiru sichidzatchedwanso munthu waulemu wake ndipo munthu woyipa sadzalemekezedwa.
6 Paske moun fou a pale foli, e kè li apiye vè mechanste: pou fè sa ki kont Bondye e pale mal kont SENYÈ a, pou kenbe moun grangou a san satisfè, e pou anpeche moun swaf la bwè.
Pakuti munthu opusa amayankhula zauchitsiru, amaganiza kuchita zoyipa: Iye amachita zoyipira Mulungu, ndipo amafalitsa zolakwika zokhudza Yehova; anjala sawapatsa chakudya ndipo aludzu sawapatsa madzi.
7 Pou vakabon an, zam li se mechanste. Li fòme plan mechan pou detwi moun aflije a ak kout lang, malgre sila ki nan bezwen an pale sa ki bon.
Munthu woyipa njira zake ndi zoyipanso, iye kwake nʼkulingalira zinthu zoyipa. Amalingalira zakuti awononge anthu aumphawi ndi mabodza ake ngakhale kuti waumphawiyo akuyankhula zoona.
8 Men sila ki prens toujou fòme plan ki bèl; epi pa bèl plan an, ap kanpe.
Koma munthu wolemekezeka amalingaliranso kuchita zinthu zabwino, Iye amakhazikika pa zinthu zabwinozo.
9 Leve ou menm, O fanm ki alèz e tande vwa mwen! Prete zòrèy a pawòl mwen, fi ki alèz, san pwoblèm yo.
Khalani maso, inu akazi amene mukungokhala wopanda kulingalira kuti kunja kulinji ndipo imvani mawu anga. Inu akazi odzitama, imvani zimene ndikunena!
10 Nan yon ane ak kèk jou, nou va twouble, O fi ki san pridans yo; paske, afè fwi diven an va fini, ni rekòlt la p ap rive.
Pakapita chaka ndi masiku pangʼono inu akazi amatama mudzanjenjemera; chifukwa mitengo ya mphesa idzakanika ndipo zipatso sizidzaoneka.
11 Tranble, fanm alèz yo; twouble, nou menm ki san pridans! Retire rad nou, dezabiye nou e mete twal sak nan senti nou.
Nthunthumirani inu okhala mosatekesekanu; ndipo njenjemerani, inu akazi omadzikhulupirira nokhanu. Vulani zovala zanu, ndipo valani ziguduli mʼchiwuno mwanu.
12 Bat lestomak nou pou bèl chan jaden yo, pou chan ki plen ak fwi rezen yo.
Dzigugudeni pachifuwa mwachisoni chifukwa minda yachonde, ndi mphesa yawonongeka.
13 Anplispou peyi a pèp mwen an, kote pikan ak raje va pouse monte; wi pou tout kay plen ak jwa yo ak gran vil kè kontan yo.
Mʼdziko la anthu anga mwamera minga ndi mkandankhuku. Zoona, mulilire nyumba zonse zachikondwerero ndi mzinda uno umene unali wachisangalalo.
14 Paske palè a vin vid, e gran vil plen moun yo vin abandone. Kolin ak fò ki wo yo vin tounen kav yo jis pou tout tan, yon plezi pou bourik mawon, yon patiraj pou bann mouton yo;
Nyumba yaufumu idzasiyidwa, mzinda waphokoso udzakhala wopanda anthu; malinga ndi nsanja zidzasanduka chipululu mpaka muyaya. Abulu adzasangalalamo ndipo ziweto zidzapezamo msipu.
15 jiskaske Lespri a vide sou nou soti anwo, epi savann nan vin fè yon chan fètil, e chan fètil la va vin konsidere kon yon forè.
Yehova adzatipatsa mzimu wake, ndipo dziko lachipululu lidzasanduka munda wachonde, ndipo munda wachonde udzakhala ngati nkhalango.
16 Nan lè sa a lajistis va demere nan dezè a e ladwati nan chan fètil la.
Tsono mʼchipululu mudzakhala chiweruzo cholungama ndipo mʼminda yachonde mudzakhala chilungamo.
17 Epi zèv ladwati a va lapè, e sèvis ladwati a va kalm ak konfyans k ap dire jis pou tout tan.
Mtendere udzakhala chipatso chachilungamo; zotsatira za chilungamo zidzakhala bata ndi kudzidalira mpaka muyaya.
18 Nan lè sa a, pèp mwen an va viv nan yon abitasyon lapè, ak sekirite ki san twoub nan plas repo san pwoblèm.
Anthu anga adzakhala mʼmidzi yamtendere, mʼnyumba zodalirika, ndi malo osatekeseka a mpumulo.
19 Malgre lagrèl tonbe kraze forè a, e gran vil la va vin devaste nèt.
Ngakhale nkhalango idzawonongedwa ndi matalala ndipo mzinda udzagwetsedwa mpaka pansi,
20 A la beni nou va beni, nou menm ki simen akote tout dlo yo, ki lage pye bèf ak bourik la.
inutu mudzakhala odalitsika ndithu. Mudzadzala mbewu zanu mʼmbali mwa mtsinje uliwonse, ndipo ngʼombe zanu ndi abulu anu zidzadya paliponse.

< Ezayi 32 >