< Αποκαλυψις Ιωαννου 5 >

1 Καὶ εἶδον ἐπὶ τὴν δεξιὰν τοῦ καθημένου ἐπὶ τοῦ θρόνου βιβλίον γεγραμμένον ἔσωθεν καὶ (ὄπισθεν, *NK(o)*) κατεσφραγισμένον σφραγῖσιν ἑπτά.
Kenaka ndinaona buku mʼdzanja la wokhala pa mpando waufumu uja. Bukulo linali lolembedwa mbali zonse ndipo linali lomatidwa ndi zomatira zisanu ndi ziwiri.
2 Καὶ εἶδον ἄγγελον ἰσχυρὸν κηρύσσοντα ἐν φωνῇ μεγάλῃ· τίς (ἐστιν *k*) ἄξιος ἀνοῖξαι τὸ βιβλίον καὶ λῦσαι τὰς σφραγῖδας αὐτοῦ;
Ndipo ndinaona mngelo wamphamvu akulengeza ndi mawu okweza kuti, “Ndani ali woyenera kumatula zomatira ndi kufutukula bukuli?”
3 καὶ οὐδεὶς ἐδύνατο ἐν τῷ οὐρανῷ (ἄνω *O*) (οὐδὲ *NK(o)*) ἐπὶ τῆς γῆς (οὐδὲ *NK(o)*) ὑποκάτω τῆς γῆς ἀνοῖξαι τὸ βιβλίον (οὔτε *N(k)O*) βλέπειν αὐτό.
Koma panalibe ndi mmodzi yemwe kumwamba kapena pa dziko lapansi kapena kunsi kwa dziko lapansi woti afutukule bukulo kapena kuona zamʼkati mwake.
4 καὶ (ἐγὼ *ko*) ἔκλαιον (πολὺ *N(k)O*) ὅτι οὐδεὶς ἄξιος εὑρέθη ἀνοῖξαι (καὶ ἀναγνῶναι *K*) τὸ βιβλίον οὔτε βλέπειν αὐτό.
Ndinalira kwambiri chifukwa panalibe amene anapezeka woyenera kufutukula bukuli kapena kuona zamʼkati mwake.
5 καὶ εἷς ἐκ τῶν πρεσβυτέρων λέγει μοι· μὴ κλαῖε. ἰδοὺ ἐνίκησεν ὁ λέων ὁ (ὢν *k*) ἐκ τῆς φυλῆς Ἰούδα, ἡ ῥίζα Δαυίδ, (ὁ *o*) (ἀνοῖξαι *NK(o)*) τὸ βιβλίον καὶ (λῦσαι *K*) τὰς ἑπτὰ σφραγῖδας αὐτοῦ.
Tsono mmodzi mwa akuluakulu aja anati kwa ine, “Usalire! Taona, Mkango wa fuko la Yuda, Muzu wa Davide, wapambana. Iye angathe kufutukula bukuli ndi kumatula zomatira zisanu ndi ziwirizo.”
6 καὶ εἶδον (καὶ ἰδού, *K*) ἐν μέσῳ τοῦ θρόνου καὶ τῶν τεσσάρων ζῴων καὶ ἐν μέσῳ τῶν πρεσβυτέρων ἀρνίον (ἑστηκὸς *NK(o)*) ὡς ἐσφαγμένον (ἔχων *N(k)O*) κέρατα ἑπτὰ καὶ ὀφθαλμοὺς ἑπτὰ (οἵ *NK(o)*) εἰσιν τὰ ἑπτὰ πνεύματα τοῦ θεοῦ (τὰ *k*) (ἀπεσταλμένοι *NK(o)*) εἰς πᾶσαν τὴν γῆν.
Kenaka ndinaona Mwana Wankhosa akuoneka ngati wophedwa atayimirira pakatikati pa mpando waufumu uja ndi zamoyo zinayi zija ndi akuluakulu aja. Mwana Wankhosayo anali ndi nyanga zisanu ndi ziwiri ndi maso asanu ndi awiri omwe ndi Mizimu isanu ndi iwiri ya Mulungu yomwe anayitumiza ku dziko lonse lapansi.
7 καὶ ἦλθεν καὶ εἴληφεν (τὸ *k*) (βιβλίον *K*) ἐκ τῆς δεξιᾶς τοῦ καθημένου ἐπὶ τοῦ θρόνου.
Iye anabwera natenga buku lija limene linali mʼdzanja lamanja la wokhala pa mpando waufumuyo.
8 καὶ ὅτε ἔλαβεν τὸ βιβλίον, τὰ τέσσαρα ζῷα καὶ οἱ εἴκοσι τέσσαρες πρεσβύτεροι ἔπεσαν ἐνώπιον τοῦ ἀρνίου ἔχοντες ἕκαστος (κιθάραν *N(K)O*) καὶ φιάλας χρυσᾶς γεμούσας θυμιαμάτων αἵ εἰσιν αἱ προσευχαὶ τῶν ἁγίων.
Ndipo atalitenga, zamoyo zinayi zija ndi akuluakulu 24 aja anadzigwetsa pansi pamaso pa Mwana Wankhosa. Aliyense wa akuluakuluwo anali ndi zeze ndiponso mbale zagolide zodzaza ndi lubani. Lubaniyo ndi mapemphero a oyera mtima.
9 καὶ ᾄδουσιν ᾠδὴν καινὴν λέγοντες· ἄξιος εἶ λαβεῖν τὸ βιβλίον καὶ ἀνοῖξαι τὰς σφραγῖδας αὐτοῦ, ὅτι ἐσφάγης καὶ ἠγόρασας τῷ θεῷ (ἡμᾶς *KO*) ἐν τῷ αἵματί σου ἐκ πάσης φυλῆς καὶ γλώσσης καὶ λαοῦ καὶ ἔθνους
Ndipo ankayimba nyimbo yatsopano yakuti, “Inu ndinu woyenera kulandira bukuli ndi kumatula zomatira zake, chifukwa munaphedwa, ndipo magazi anu munagulira Mulungu anthu a fuko lililonse, a chiyankhulo chilichonse, ndi mtundu uliwonse.
10 καὶ ἐποίησας (αὐτοὺς *N(K)O*) τῷ θεῷ ἡμῶν (βασιλείαν *N(K)O*) καὶ ἱερεῖς, καὶ (βασιλεύσουσιν *N(K)(o)*) ἐπὶ τῆς γῆς.
Inu munawasandutsa kukhala mtundu waufumu ndi ansembe otumikira Mulungu, ndipo adzalamulira dziko lapansi.”
11 Καὶ εἶδον καὶ ἤκουσα (ὡς *O*) φωνὴν ἀγγέλων πολλῶν (κύκλῳ *N(k)O*) τοῦ θρόνου καὶ τῶν ζῴων καὶ τῶν πρεσβυτέρων. (καὶ ἦν ὁ ἀριθμὸς αὐτῶν μυριάδες μυριάδων *NO*) καὶ χιλιάδες χιλιάδων
Kenaka nditayangʼananso ndinamva mawu a angelo ambiri, miyandamiyanda kuchulukitsa ndi miyandamiyanda. Anazungulira mpando waufumu pamodzi ndi zamoyo zija ndi akuluakulu aja.
12 λέγοντες φωνῇ μεγάλῃ· ἄξιόν ἐστιν τὸ ἀρνίον τὸ ἐσφαγμένον λαβεῖν τὴν δύναμιν καὶ (τὸν *o*) πλοῦτον καὶ σοφίαν καὶ ἰσχὺν καὶ τιμὴν καὶ δόξαν καὶ εὐλογίαν.
Ndipo angelowo anayimba ndi mawu ofuwula akuti, “Mwana Wankhosa amene anaphedwayu ndi woyenera kulandira ulamuliro, chuma, nzeru, mphamvu, ulemu, ulemerero ndi mayamiko.”
13 καὶ πᾶν κτίσμα ὃ (ἐστιν *k*) ἐν τῷ οὐρανῷ καὶ (ἐπὶ τῆς γῆς *N(k)O*) καὶ ὑποκάτω τῆς γῆς καὶ ἐπὶ τῆς θαλάσσης (ἅ *k*) (ἐστὶν *ko*) καὶ τὰ ἐν αὐτοῖς (πάντα *N(k)O*) ἤκουσα λέγοντας· τῷ καθημένῳ ἐπὶ (τῷ θρόνῳ *N(k)O*) καὶ τῷ ἀρνίῳ ἡ εὐλογία καὶ ἡ τιμὴ καὶ ἡ δόξα καὶ τὸ κράτος εἰς τοὺς αἰῶνας τῶν αἰώνων (ἀμήν. *O*) (aiōn g165)
Kenaka ndinamva mawu a cholengedwa chilichonse kumwamba, pa dziko lapansi, kunsi kwa dziko lapansi, pa nyanja ndi zonse zili mʼmenemo zikuyimba kuti, “Kwa wokhala pa mpando waufumu ndi kwa Mwana Wankhosa, kukhale mayamiko, ulemu, ulemerero ndi mphamvu (aiōn g165)
14 καὶ τὰ τέσσαρα ζῷα (ἔλεγον· *NK(o)*) (τὸ *o*) ἀμήν. καὶ οἱ (εἴκοσιτέσσαρες εἴκοσιτέσσαρες *K*) πρεσβύτεροι ἔπεσαν καὶ προσεκύνησαν (ζῶντι εἰς τοὺς αἰωνας τῶν αἰώνων. *K*)
Zamoyo zinayi zija zinati: “Ameni,” ndipo akuluakulu aja anadzigwetsa pansi napembedza.

< Αποκαλυψις Ιωαννου 5 >