< Luuqaasa 4 >

1 Yesuusi Geeshsha Ayyaanan kumidi Yorddaanose Shaafappe simmida mela Ayyaanay iya bazzo efis.
Yesu, wodzazidwa ndi Mzimu Woyera, anachoka ku mtsinje wa Yorodani ndipo anatsogozedwa ndi Mzimu Woyerayo kupita ku chipululu,
2 Yan oytamu gallasinne qamma xalahen paacettis. He gallasatan aykkoka moonna gam77ida gisho wurssethan koshattis.
kumene anayesedwa ndi mdierekezi masiku makumi anayi. Sanadye kena kalikonse pa masiku amenewo, ndipo pa mapeto pake anamva njala.
3 Xalahey iyaakko, “Neeni Xoossaa na7a gidikko ane hayssi shuchchay uythu gido gada kiitta” yaagis.
Mdierekezi anati kwa Iye, “Ngati ndiwe Mwana wa Mulungu, uza mwala uwu kuti usanduke buledi.”
4 Yesuusi zaaridi, “Asi uytha xalaalan deenna geetettidi xaafettis” yaagis.
Yesu anayankha kuti, “Zalembedwa: ‘Munthu sadzakhala ndi moyo ndi chakudya chokha.’”
5 Hessafe guye, Xalahey Yesuusa adussa dere bolla kessidi ha alamiya kawotethata ayfe qiphi zaaranaw bessis.
Mdierekezi anamutengera Iye pamalo aatali ndipo mʼkamphindi namuonetsa maufumu onse a dziko lapansi.
6 Xalahey, “Ha ubbaas maataynne bonchchoy taw imettis. Taani dosida oodeskka immiya gisho new immana.
Ndipo anati kwa Iye, “Ndidzakupatsani ulamuliro ndi ulemerero wawo; pakuti anandipatsa ine, ndipo ndingathe kupereka kwa aliyense amene ndikufuna.
7 Hessa gisho, neeni taw goynniko ubbay new gidana” yaagis.
Ngati mutandilambira, zonsezi zidzakhala zanu.”
8 Yesuusi zaaridi, “Ne Godaa, ne Xoossaa, iya xalaala goynna geetettidi xaafettis” yaagis.
Yesu anayankha kuti, “Zalembedwa: ‘Pembedza Yehova Mulungu wako ndi kumutumikira Iye yekha.’”
9 Wurssethan Xalahey Yesuusa Yerusalaame efidi Xoossa Keethas huu7iya bolla essidi, “Neeni Xoossaa na7a gidikko ane duge sa7an nena yegga.
Mdierekezi anapita naye ku Yerusalemu namuyimiritsa pamwamba penipeni pa Nyumba ya Mulungu. Ndipo anati, “Ngati ndinu Mwana wa Mulungu dziponyeni nokha pansi kuchokera pano.
10 Ays giikko, ‘Nena naagiya Kiitanchchota Xoossay ne gisho kiittana.
Pakuti kwalembedwa, “Adzalamulira angelo ake za iwe kuti akutchinjirize mosamala;
11 Entti ne tohoy shuchchan dhubettonna mela, bantta kushiyan dhoqqu oothidi nena denthana’ geetettidi xaafettis” yaagis.
ndipo adzakunyamula ndi manja awo, kuti phazi lako lisagunde pa mwala.”
12 Yesuusi zaaridi, “Ne Godaa Xoossaa paaccofa geetettidi xaafettis” yaagis.
Yesu anayankha kuti, “Mawu akuti, ‘Musamuyese Yehova Mulungu wanu.’”
13 Xalahey Yesuusa paaciya wurssidaappe guye hara injje wode demmana gakkanaw iyappe shaakettis.
Mdierekezi atamaliza mayesero awa onse, anamusiya Iye kufikira atapeza mpata wina.
14 Yesuusi Ayyaana wolqqan kumidi Galiila simmis. Iya sunthay heeran de7iya biitta ubban keyis.
Yesu anabwerera ku Galileya mu mphamvu ya Mzimu Woyera, ndipo mbiri yake inafalikira ku madera onse a ku midzi.
15 I Ayhude Woosa Keethi gelidi tamaarssis; asay ubbay iya galatidosona.
Iye ankaphunzitsa mʼmasunagoge awo, ndipo aliyense ankamulemekeza.
16 Yaappe I diccida katamaa Naazirete yis. Kase meezetidayssada Sambbaata gallas Ayhude Woosa Keethi gelis. Nabbabanawukka denddi eqqis.
Iye anapita ku Nazareti, kumene anakulira, ndipo pa tsiku la Sabata anakalowa mʼsunagoge, monga mwa chikhalidwe chake. Ndipo anayimirira kuti awerenge malemba.
17 Nabiya Isayaasa maxaafay iyaw imettin, maxaafaa dooyidi, geetettidi xaafettidayssa demmis:
Anamupatsa buku la mneneri Yesaya. Atalitsekula, anapeza pamalo pamene panalembedwa kuti,
18 “Godaa Ayyaanay ta bolla de7ees, manqotas Wonggelaa odana mela Xoossay tana dooris. Qashettidayssatas biletethi, qooqidayssata xeelisanaasinne un77ettidayssata birshshana mela,
“Mzimu wa Ambuye ali pa Ine; chifukwa wandidzoza kuti ndilalikire Uthenga Wabwino kwa osauka. Wandituma kuti ndilalikire kwa a mʼndende kuti amasulidwe ndi kwa osaona kuti apenyenso, kumasulidwa kwa osautsidwa,
19 Xoossay keehanaw qoppida laythaa odana mela tana kiittis” yaagis.
ndi kulalikira za nthawi imene Ambuye adzakomere mtima anthu awo.”
20 Hessafe guye, maxaafaa xaaxidi haggaazeyssas immidi tamaarssanaw uttis. Ayhude Woosa Keethan de7iya asati ubbay caddi xeellosona.
Kenaka Iye anatseka bukulo, nalibwezera kwa wotumikira ndipo anakakhala pansi. Maso a aliyense mʼsunagogemo anali pa Iye,
21 I, “Hayssi hintte haythan hintte si7iya ha maxaafaa qaalay hachchi polettis” yaagis.
ndipo anawawuza kuti, “Lero malemba awa akwaniritsidwa mmene mwamveramu.”
22 Ubbay iyabaa darssidi odettoosona. Qassi iya doonappe keyaa aadho keehatethan kumida qaalan malaalettishe, “Hayssi Yoosefa na7aa gidenneyye?” yaagidosona.
Onse anayankhula zabwino za Iye ndipo anadabwa ndi mawu ogwira moyo amene anatuluka mʼkamwa mwake. Iwo anafunsa kuti, “Kodi uyu si mwana wa Yosefe?”
23 I, “‘Neno dhale aawaw nena ashsha, Qifirnahoomen ne oothidabaa nu si77oyssa qassi hayssan ne kataman ootha’ yaagiya leemisuwan hintte tana gaanayssas sidhey baawa” yaagis.
Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, mudzandiwuza mwambi uwu: Singʼanga, dzichiritse wekha! Chitanso mʼmudzi wa kwanu kuno zimene ife tamva kuti Iwe unazichita ku Kaperenawo.”
24 Qassi, “Tuma odays; nabey ba yelettida biittan bonchchettena.
Iye anapitiriza kuti, “Zoonadi, ndikukuwuzani kuti palibe mneneri amene amavomerezedwa ku mudzi kwawo.
25 “Ta hinttew tuma odays; saloy heedzu laythinne bagga gorddettin mino koshi biitta ubban de7iya Eliyaasa wode daro am77eti Isra7eelen de7oosona.
Ine ndikukutsimikizirani kunali amayi ambiri amasiye mu Israeli mʼnthawi ya Eliya, kumwamba kutatsekedwa kwa zaka zitatu ndi theka ndipo kunali njala yayikulu mʼdziko lonselo.
26 Eliyaasi enttafe issinnekokka kiitettibeenna. Shin Serapitan de7iya am77eeko kiitettis.
Komabe Eliya sanatumidwe kwa mmodzi mwa iwo, koma kwa mkazi wamasiye wa ku Zerefati ku chigawo cha Sidoni.
27 Nabiya Elssa7e wode Isra7eelen daro baro hargganchchoti de7oosona. Shin Soore uraa Ni7imaaneppe attin oonikka paxibeenna” yaagis.
Ndipo kunali akhate ambiri ku Israeli mʼnthawi ya mneneri Elisa, koma panalibe mmodzi mwa iwo anachiritsidwa kupatula Naamani wa ku Siriya.”
28 Ayhude Woosa Keethan de7iya asay ubbay hessa si7ida wode daro yilotidosona.
Anthu onse mʼsunagogemo anapsa mtima atamva izi.
29 Bantta uttida bessaafe denddidi zuma bolla keexettida katamaappe gaxa kessidi sugi yeddanaw aafo doona efidosona.
Anayimirira namutulutsira kunja kwa mzindawo, ndipo anamutengera pamwamba pa phiri pamene mzindawo unamangidwapo, ndi cholinga chakuti amuponyere ku phompho.
30 Shin I entta giddora kanthidi aadhdhis.
Koma Iye anangoyenda pakati pa gulu la anthulo nachokapo.
31 Yaappe Galiila biittan de7iya Qifirnahoome katama bis. Yan Sambbaata gallas asaa tamaarssis.
Kenaka Iye anapita ku Kaperenawo, mudzi wa ku Galileya, ndipo pa Sabata anayamba kuphunzitsa anthu.
32 I tamaarssey maatara gidiya gisho ubbay iya timirttiyan malaalettidosona.
Iwo anadabwa ndi chiphunzitso chake chifukwa uthenga wake unali ndi ulamuliro.
33 Ayhude Woosa Keethan tuna ayyaanay oykkida uray de7ees.
Mʼsunagogemo munali munthu wogwidwa ndi mzimu woyipa. Iye analira ndi mawu akulu, akuti
34 I, “Naazirete Yesuusa nuna ays waaysay nuuppe haakka; neeni yiday nuna dhayssanaaseyye? Neeni ooneekko taani erays. Neeni Xoossaafe yida Geeshsha” yaagidi waassis.
“Aa! Kodi mukufuna chiyani kwa ife, Yesu wa ku Nazareti? Kodi mwabwera kudzatiwononga? Ndikudziwa kuti ndinu ndani, ndinu Woyerayo wa Mulungu!”
35 Yesuusi tuna ayyaanaakko, “Si7i gada ha uraappe keya” yaagidi hanqis. Tuna ayyaanay uraa asaa ubbaa sinthan holi yeggidi aykkoka qohonna yeddidi keyis.
Yesu anachidzudzula kwambiri nati, “Khala chete! Tuluka mwa iye.” Chiwandacho chinamugwetsa munthuyo pansi pamaso pa onse ndipo chinatuluka wosamupweteka.
36 Asa ubbay malaalettidosona. Wolikko, “Hanos, hayssi aybi timirtte? Tuna ayyaanata maataninne wolqqan kiittees; enttika keyosona” yaagidosona.
Anthu onse anadabwa ndipo anati kwa wina ndi mnzake, “Kodi chiphunzitso ichi ndi chotani? Ndi ulamuliro ndi mphamvu Iye akulamulira mizimu yoyipa ndipo ikutuluka!”
37 Iya sunthay heera ubban keyis.
Ndipo mbiri yake inafalikira madera onse ozungulira.
38 Hessafe guye, Yesuusi Ayhude Woosa Keethafe keyidi Simoona soo gelis. Simoona machche aayiya mino qoxo misha harggen sakettasu. Iyo pathana mela Yesuusa woossidosona.
Yesu anatuluka mʼsunagoge ndipo anapita kwa Simoni. Tsopano mpongozi wake wa Simoni amadwala malungo akulu, ndipo anamupempha Yesu kuti amuthandize.
39 I hiixaakko shiiqi hokkidi I harggiya hanqis. Mishay aggin ellesa denddada entta mokkasu.
Ndipo anawerama nadzudzula malungowo ndipo anamusiya. Anadzuka nthawi yomweyo nayamba kuwatumikira.
40 Away wullana hanishin dumma dumma harggiyan oykettida asaa iyaakko ehidosona. I issuwa issuwa bolla ba kushiya wothidi pathis.
Pamene dzuwa linkalowa, anthu anabweretsa kwa Yesu onse amene anali ndi matenda osiyanasiyana, ndipo atasanjika manja ake pa aliyense, anachiritsidwa.
41 Tuna ayyaanati qassi, “Neeni, Xoossaa na7aa” gidi waassishe daro asaappe keyidosona. Shin I enttana hanqis. I Kiristtoosa gideyssa entti eriya gisho, issibaakka odettonna mela diggis.
Komanso ziwanda zinkatuluka mwa anthu ambiri, zikufuwula kuti, “Inu ndinu Mwana wa Mulungu!” Koma Iye anazidzudzula ndipo sanazilole kuyankhula chifukwa zimadziwa kuti Iye ndi Khristu.
42 Buroo wonttiya wode Yesuusi issi geema bessi bis. Asay koyishe I de7iya bessaa yidosona. Enttafe I shaakettidi boonna mela butetidosona.
Kutacha, Yesu anapita ku malo a yekha. Anthu ankamufunafuna Iye ndipo pamene anafika kumene anali, anthuwo anayesetsa kumuletsa kuti asawachokere.
43 Shin I, “Taani hara katamata bada Xoossaa kawotethaa Wonggelaa markkattanaw bessees. Ta kiitettiday hessassa” yaagis.
Koma Iye anati, “Ine ndikuyenera kulalikira Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu ku mizinda inanso chifukwa ichi ndi chimene ananditumira.”
44 Yihuda biittan de7iya Ayhude Woosa Keethan sabbakis.
Ndipo Iye anapitirirabe kulalikira mʼmasunagoge a ku Yudeya.

< Luuqaasa 4 >