< Yayqooba 1 >
1 Xoossaanne Godaa Yesuus Kiristtoosa aylley, Yayqoobi, biitta ubban laalettida tammanne nam77u sheeshatas kiittida kiita. Saro, ay mela de7eetii?
Yakobo, mtumiki wa Mulungu ndi wa Ambuye Yesu Khristu, kulembera mafuko khumi ndi awiri obalalikana ku mayiko osiyanasiyana. Landirani moni.
2 Ta ishato, hinttena dumma dumma paacey gakkiya wode hintte lo77obaa demmidaada kumetha ufayssan ekkite.
Abale, muchiyese ngati chimwemwe chenicheni nthawi zonse pamene mukukumana ndi mayesero amitundumitundu.
3 Hintte ammanuwa paacetethay dandda7a hinttew immeyssa ereeta.
Inu mukudziwa kuti kuyesedwa kwa chikhulupiriro chanu kumabweretsa chipiriro.
4 Hintte wurssethi gakkanaw dandda7ikko aybi pacey baynna polonne kumethi gideta.
Chipiriro chiyenera kugwira ntchito yake kuti mukhale okhwima ndi angwiro, osasowa kanthu kalikonse.
5 Hinttefe oodeskka cinccatethi dhayikko Xoossaa woosso. Iyaw imettana. Xoossay oonakka boronna ubbaas keehatethan immiya Xoosse.
Ngati wina pakati panu akusowa nzeru, apemphe kwa Mulungu amene amapereka kwa onse mwaulere ndi mosatonzera, ndipo adzapatsidwa.
6 Shin I woossiya wode sidhonna ammanon Xoossaa woosso. Sidhiya oonikka carkkoy sugin qaaxxiya abbaa zule mela.
Koma pamene mupempha, muyenera kukhulupirira osakayika, chifukwa amene amakayika ali ngati mafunde pa nyanja amene amawinduka nakankhika ndi mphepo.
7 Nam77u qofi de7eynne ba ogiyan eqqonna oonikka Godaappe aykkoka demmana gidi qoppofo.
Munthu wotere asayembekezere kulandira kalikonse kuchokera kwa Ambuye.
Iyeyu ndi munthu wa mitima iwiri, wosakhazikika pa zimene akuchita.
9 Ammaniya manqo asati, Xoossay enttana dhoqqu oothiya wode ufaytto.
Abale omwe ndi anthu wamba anyadire pamene akwezedwa.
10 Qassi ammaniyaa dure asati Xoossay enttana ziqqi oothiya wode ufaytto. Dure asati ciishshada dhayana.
Koma olemera anyadire pamene atsitsidwa, chifukwa adzatha ngati duwa lakuthengo.
11 Away ba mishaara keyidi maataa melisin, ciishshay serees; iya lo77otethayka dhayees. Hessadakka, dure asati bantta oosuwan daaburishe dhayana.
Pakuti dzuwa limatuluka nʼkutentha kwake, ndipo limafotetsa zomera. Duwa lake limathothoka ndipo kukongola kwake kumatheratu. Momwemonso munthu wachuma adzazimirira ngakhale atamachitabe malonda ake.
12 Metuwa xoonidi aadhdhidaappe guye, Xoossay bana siiqeyssatas immana gidi qaala gelida de7o kallachcha ekkana gisho, meton gencciya asi anjjettidayssa.
Wodala ndi munthu amene amapirira mʼmayesero, chifukwa akapambana adzalandira chipewa cha ulemerero chimene Mulungu analonjeza anthu amene amamukonda.
13 Oonikka paacettiya wode, “Tana Xoossay paaces” gooppo. Xoossay iitan paacettenna; qassi I oonakka paaccenna.
Munthu akayesedwa asanene kuti, “Mulungu akundiyesa.” Pakuti Mulungu sangayesedwe ndi choyipa kapena Iyeyo kuyesa munthu aliyense.
14 Shin issi issi asi ba iita amuwaan gooshettiya wodenne cimettiya wode paacettees.
Koma munthu aliyense amayesedwa akakokedwa ndi zilakolako zake zoyipa ndi kukopedwa nazo.
15 Hessafe guye, amotethi qanthattidi nagara yelees; qassi nagari diccidi hayqo yelees.
Pamenepo, chilakolako chikakula chimabala tchimo; ndipo tchimo likakhwima limabereka imfa.
16 Ta siiqo ishato, cimettofite.
Musanyengedwe abale anga okondedwa.
17 Lo77o imoynne kumetha anjjo ubbay saloppenne saluwa poo7uwa medhdhida Xoossaa aawappe yees. Xoossay kuyada ubba wode laamettenna.
Mphatso iliyonse yabwino ndi yangwiro imachokera kumwamba, kwa Atate mwini kuwala, amene sasintha ngati mthunzi woyendayenda.
18 Nuuni, iya medhetethaas koyro gidana mela nuna tuma qaalan ba shenen yelis.
Iye anasankha kutibereka ife kudzera mʼmawu a choonadi, kuti pakati pa zolengedwa zake zonse, tikakhale ngati zipatso zoyamba.
19 Ta siiqo ishato, hayssa akeekite. Asi ubbay si7anaw elleso, shin odettanawunne hanqettanaw ellesoppo.
Abale anga okondedwa, gwiritsitsani mawu awa: munthu aliyense azifulumira kumva, koma asamafulumire kuyankhula, ndipo asamafulumirenso kupsa mtima.
20 Asa hanqoy Xoossay koyaa xillotethaa ehenna.
Pakuti mkwiyo wa munthu subweretsa chilungamo chimene amafuna Mulungu.
21 Hessa gisho, tuna hanotanne iitatetha ubbaa diggidi, Xoossay hintte wozanan tokkida hintte shemppuwa ashshanaw dandda7iya qaala aadatethan ekkite.
Choncho chotsani chizolowezi choyipa ndi khalidwe loyipa pakati panu, ndipo modzichepetsa landirani mawu amene anadzalidwa mwa inu, amene akhoza kukupulumutsani.
22 Shin Xoossaa qaala ooson peeshshiteppe attin sissa xalaalan hinttena cimmofite.
Musamangomvetsera chabe mawu, ndi kumadzinyenga nokha. Chitani zimene mawuwo amanena.
23 Qaalaa si7idi oothonna asi, I ba som77uwa masttoten be7iya asa mela.
Munthu aliyense amene amangomva mawu koma osachita zimene mawuwo amanena, ali ngati munthu amene amayangʼana nkhope yake pa galasi.
24 I ba som77uwa be7idi bees, shin I ay daaniyakko ellesi dogees.
Akadziyangʼana amachoka, nthawi yomweyo nʼkuyiwala mmene akuonekera.
25 Shin oonikka aylletethafe kessiya polo higgiya akeekan be7idi, kaallidi naagey, si7idayssa dogonna ooson peeshshiya uray, ba ooso ubban anjjettana.
Koma munthu amene amayangʼana mwachidwi lamulo langwiro limene limapatsa ufulu ndi kupitiriza kutero, osayiwala chimene wamva koma kuchita adzadalitsika pa zimene amachita.
26 Ba inxarssaa naagonna ammanays giya uray bana cimmees; iya ammanoy hada.
Ngati wina amadziyesa ngati ndi wachipembedzo, koma chonsecho saletsa lilime lake, amadzinyenga yekha ndipo chipembedzo chakecho ndi cha chabechabe.
27 Xoossaa Aawa sinthan borey baynna geeshsha ammanoy hayssa: aaya aawu baynna naytanne am77eta maadonne alamiya tunaappe bana naago.
Chipembedzo chimene Mulungu Atate athu amachivomereza kuti ndi changwiro ndi chopanda zolakwika ndi ichi: kusamalira ana amasiye ndi akazi amasiye pa mavuto awo, ndi kudzisunga bwino kuopa kudetsedwa ndi dziko lapansi.