< Psalm 24 >
1 Die Erde ist Jehovahs, und ihre Fülle, die Welt, und die darauf wohnen.
Salimo la Davide. Dziko lapansi ndi la Yehova ndi zonse zimene zili mʼmenemo, dziko ndi onse amene amakhala mʼmenemo;
2 Denn Er hat auf die Meere sie gegründet, und auf den Flüssen sie festgestellt.
pakuti Iye ndiye anayika maziko ake pa nyanja ndi kulikhazika pamwamba pa madzi.
3 Wer wird hinaufgehen auf den Berg Jehovahs, und wer wird aufstehen am Orte Seiner Heiligkeit?
Ndani angakwere phiri la Yehova? Ndani angathe kuyima pa malo ake opatulika?
4 Wer unschuldige Hände hat und lauteren Herzens ist, der seine Seele nicht erhebt auf Eitles und nicht schwört zum Trug.
Iye amene ali ndi mʼmanja moyera ndi mtima woyera, amene sapereka moyo wake kwa fano kapena kulumbira mwachinyengo.
5 Der wird empfangen Segen von Jehovah, und Gerechtigkeit vom Gotte seines Heils.
Iyeyo adzalandira madalitso kwa Yehova ndipo Mulungu mpulumutsi wake adzagamula kuti alibe mlandu.
6 Dies das Geschlecht, das Ihm nachfragt, das Dein Angesicht sucht, o Jakob. (Selah)
Umenewo ndiwo mʼbado wa amene amafunafuna Yehova; amene amafunafuna nkhope yanu, Inu Mulungu wa Yakobo. (Sela)
7 Erhebt eure Häupter, ihr Tore, und erhebt euch, ihr ewigen Pforten, daß einziehe der König der Herrlichkeit.
Tukulani mitu yanu inu zipata; tsekukani, inu zitseko zakalekalenu, kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
8 Wer ist dieser König der Herrlichkeit? Jehovah, der Starke, der Held, Jehovah, der Held im Streite.
Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani? Yehova Wamphamvuzonse, Yehova ndiye wamphamvu pa nkhondo.
9 Erhebt eure Häupter ihr Tore, und erhebt euch, ihr ewigen Pforten, daß einziehe der König der Herrlichkeit.
Tukulani mitu yanu, inu zipata; tsekukani, inu zitseko zakalekalenu, kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
10 Wer ist Er, dieser König der Herrlichkeit? Jehovah der Heerscharen ist es. Er ist der König der Herrlichkeit. (Selah)
Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani? Yehova Wamphamvuzonse, Iye ndiye Mfumu yaulemerero. (Sela)