< Psalm 119 >

1 Selig die, deren Weg untadelig ist, die in dem Gesetz Jehovahs wandeln.
Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
2 Selig die, die Seine Zeugnisse bewahren, die Ihn von ganzem Herzen suchen.
Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
3 Auch tun sie nichts Verkehrtes. In Seinen Wegen wandeln sie.
Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
4 Du hast geboten, Deine Ordnungen sehr zu halten.
Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
5 Möchten doch meine Wege dahin sich richten, daß ich hielte Deine Satzungen.
Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
6 Dann werde ich nicht beschämt, wenn ich auf alle Deine Gebote blicke.
Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
7 Ich bekenne Dich in Geradheit des Herzens, wenn ich lerne die Rechte Deiner Gerechtigkeit.
Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
8 Deine Satzungen will ich halten; verlasse mich nicht zu sehr.
Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
9 Wie wird ein Jüngling seinen Pfad lauter machen? Daß er sich halte nach Deinem Wort.
Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
10 Von ganzem Herzen suche ich nach Dir. Laß mich von Deinen Geboten nicht fehlgehen.
Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
11 In meinem Herzen verdecke ich Deine Rede, daß ich nicht wider Dich sündige.
Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
12 Gesegnet bist Du, Jehovah, lehre mich Deine Satzungen.
Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
13 Mit meinen Lippen habe ich alle die Rechte Deines Mundes erzählt.
Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
14 Auf dem Weg Deiner Zeugnisse freue ich mich mehr, als über alle Güter.
Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
15 Ich überdenke Deine Ordnungen und blicke auf Deine Pfade.
Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
16 An Deinen Satzungen ergötze ich mich, ich vergesse nicht Deines Wortes.
Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
17 Tue wohl Deinem Knechte, daß ich lebe und halte Dein Wort.
Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
18 Tue meine Augen auf, daß ich Wunder aus Deinem Gesetz erblicke.
Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
19 Ein Fremdling bin ich auf Erden, verbirg Deine Gebote nicht vor mir!
Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
20 Zerdrückt ist meine Seele vor Sehnsucht nach Deinen Rechten alle Zeit.
Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
21 Du bedrohst die verfluchten Vermessenen, die von Deinen Geboten fehlgehen.
Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
22 Wälze von mir Schmach und Verachtung ab; denn Deine Zeugnisse habe ich bewahrt.
Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
23 Selbst Oberste sitzen und bereden sich wider mich; Dein Knecht überdenkt Deine Satzungen.
Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
24 Deine Zeugnisse sind auch mein Ergötzen, die Männer meines Rates.
Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
25 Am Staube klebt meine Seele, belebe mich nach Deinem Worte.
Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
26 Ich erzählte meine Wege, und Du antwortetest mir. Lehre Deine Satzungen.
Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
27 Laß mich den Weg Deiner Ordnungen einsehen, daß ich überdenke Deine Wunder,
Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
28 Es verfließt vor Gram meine Seele, richte mich auf nach Deinem Worte.
Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
29 Den Weg der Lüge wende von mir ab, und mit Deinem Gesetz begnade mich!
Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
30 Den Weg der Wahrheit habe ich erwählt. Ich stelle vor mich Deine Rechte.
Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
31 Ich hafte an Deinen Zeugnissen, Jehovah, lasse mich nicht beschämt werden.
Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
32 Den Weg Deiner Gebote will ich laufen, weil Du mein Herz erweiterst.
Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
33 Weise mich, Jehovah, den Weg Deiner Satzungen, und ich will ihn stets bewahren.
Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
34 Mache mich einsichtsvoll, und ich bewahre Dein Gesetz, und halte es von ganzem Herzen.
Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
35 Lasse mich einhertreten auf dem Steige Deiner Gebote, denn ich habe Lust dazu.
Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
36 Neige mein Herz zu Deinen Zeugnissen, und nicht zum Gewinn.
Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
37 Laß meine Augen vorübergehen, daß sie nicht auf Eitles sehen. Belebe mich auf Deinem Wege.
Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
38 Bestätige Deinem Knecht Deine Rede, daß man Dich fürchte.
Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
39 Laß die Schmach an mir vorübergehen, vor der mir bangt; denn gut sind Deine Rechte.
Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
40 Siehe, ich sehne mich nach Deinen Ordnungen, mit Deiner Gerechtigkeit belebe mich.
Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
41 Laß Deine Barmherzigkeit auf mich kommen, Jehovah, Dein Heil, nach Deiner Rede.
Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
42 Und ich antworte ein Wort denen, die mich schmähen; denn auf Dein Wort vertraue ich.
ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
43 Und entreiße meinem Mund nicht so sehr das Wort der Wahrheit; denn auf Deine Gerichte warte ich;
Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
44 Und will beständig halten Dein Gesetz ewiglich und immerfort.
Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
45 Und will in der Weite wandeln, denn ich frage nach Deinen Ordnungen.
Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
46 Und will reden vor Königen von Deinen Zeugnissen, und nicht mich schämen,
Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
47 Und mich ergötzen an Deinen Geboten, die ich liebe.
popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
48 Und will erheben meine Hände zu Deinen Geboten, die ich liebe, und überdenken Deine Satzungen.
Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
49 Gedenke Deinem Knecht des Wortes, dessen Du mich ließest warten.
Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
50 Das ist mein Trost in meinem Elend, weil mich Deine Rede belebt hat.
Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
51 Mich haben Vermessene gar sehr verspottet; von Deinem Gesetz wende ich mich nicht ab.
Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
52 Ich gedenke Deiner Gerichte von Ewigkeit her, Jehovah, und bin getröstet.
Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
53 Ein Glutwind hat mich ergriffen wegen der Ungerechten, die Dein Gesetz verlassen.
Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
54 Psalmen waren mir Deine Satzungen im Hause meiner Wanderungen.
Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
55 Ich gedenke Deines Namens des Nachts, Jehovah, und halte Dein Gesetz.
Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
56 Das ward mir, weil ich bewahrte Deine Ordnungen.
Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
57 Mein Teil, Jehovah, sprach ich, ist, daß ich Deine Worte halte.
Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
58 Ich flehe an Dein Angesicht von ganzem Herzen: Sei gnädig mir nach Deiner Rede.
Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
59 Ich denke meiner Wege und kehre meinen Fuß zu Deinen Zeugnissen zurück.
Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
60 Ich spute mich und zaudere nicht, Deine Gebote zu halten.
Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
61 Der Ungerechten Stricke haben mich umstrickt, ich vergesse Deines Gesetzes nicht.
Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
62 Ich stehe auf um Mitternacht, Dich zu bekennen, ob der Gerichte Deiner Gerechtigkeit.
Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
63 Ich bin ein Gefährte aller, die Dich fürchten und Deine Ordnungen halten.
Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
64 Jehovah, Deiner Barmherzigkeit ist die Erde voll, lehre mich Deine Satzungen.
Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
65 Du hast, Jehovah, Gutes an Deinem Knecht getan nach Deinem Wort.
Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
66 Das Gut des Verstandes und der Kenntnis lehre mich; denn an Deine Gebote glaube ich.
Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
67 Bevor ich ward gedemütigt, ging ich fehl, nun aber halte ich Deine Rede.
Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
68 Gut bist Du und tust Gutes, lehre mich Deine Satzungen.
Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
69 Die Vermessenen dichten Lüge wider mich, ich bewahre Deine Ordnungen von ganzem Herzen.
Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
70 Ihr Herz ist fühllos, wie Fett. Ich ergötze mich an Deinem Gesetz.
Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
71 Gut war es für mich, daß ich gedemütigt ward, damit ich lernte Deine Satzungen.
Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
72 Besser ist mir das Gesetz Deines Mundes, denn Tausende von Gold und Silber.
Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
73 Deine Hände haben mich gemacht und bereitet. Gib Einsicht mir, und ich lerne Deine Gebote.
Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
74 Mich sehen, die Dich fürchten, und sind froh, denn ich warte auf Dein Wort.
Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
75 Ich weiß, Jehovah, daß Deine Gerichte sind gerecht, und daß in Treue Du mich gedemütigt hast.
Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
76 Laß doch Deine Barmherzigkeit mir zum Troste werden, nach Deiner Rede an Deinem Knecht.
Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
77 Laß Dein Erbarmen kommen über mich, auf daß ich lebe; denn Dein Gesetz ist mein Ergötzen.
Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
78 Beschämt werden die Vermessenen; sie stürzen mich um mit Lügen, ich aber überdenke Deine Ordnungen.
Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
79 Es müssen zurückkehren zu mir die, so Dich fürchten, und Deine Zeugnisse kennen!
Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
80 Untadelig sei mein Herz in Deinen Satzungen, auf daß ich nicht beschämt werde.
Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
81 Nach Deinem Heile verzehrt sich meine Seele, auf Dein Wort habe ich gewartet.
Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
82 Es verzehren sich meine Augen nach Deiner Rede und sagen: Wann tröstest Du mich?
Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
83 Denn wie der Schlauch im Rauch bin ich; doch Deiner Satzungen vergesse ich nicht.
Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
84 Wie viele sind der Tage Deines Knechtes? Wann tust Du Gericht an meinen Verfolgern?
Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
85 Fallgruben graben mir die Vermessenen, die nicht nach Deinem Gesetz sind.
Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
86 Alle Deine Gebote sind Wahrheit. Sie verfolgen mich mit Lügen, stehe Du mir bei.
Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
87 Um ein Kleines hätten sie mich von der Erde aufgerieben; doch verließ ich nicht Deine Ordnungen.
Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
88 Belebe mich nach Deiner Barmherzigkeit, und ich werde das Zeugnis Deines Mundes halten.
Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
89 Ewiglich, o Jehovah, steht fest in den Himmeln Dein Wort.
Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
90 Deine Wahrheit ist zu Geschlecht und Geschlecht. Du festigst die Erde, und sie steht.
Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
91 Nach Deinen Rechten stehen sie heute; denn alles dient Dir.
Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
92 Wäre Dein Gesetz nicht mein Ergötzen, dann wäre ich in meinem Elend vergangen.
Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
93 Ewig vergesse ich nicht Deine Ordnungen; denn durch sie belebst Du mich.
Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
94 Dein bin ich, rette mich, denn Deinen Ordnungen frage ich nach.
Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
95 Die Ungerechten erwarten mich, daß sie mich zerstören, ich habe Einsicht in Deine Ordnungen.
Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
96 Aller Vollkommenheit sah ich ein Ende; doch Dein Gebot ist sehr weit.
Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
97 Wie liebe ich Dein Gesetz! Es ist den ganzen Tag mein Nachsinnen.
Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
98 Weiser denn meine Feinde machen mich Deine Gebote; denn mein sind sie ewiglich.
Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
99 Vor allen meinen Lehrern bin ich verständig geworden; denn Deine Zeugnisse überdenke ich.
Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
100 Einsichtsvoller bin ich, als die Alten; denn Deine Ordnungen bewahre ich.
Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
101 Von jedem bösen Pfade halte ich meine Füße weg, auf daß Dein Wort ich halte.
Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
102 Von Deinen Rechten weiche ich nicht ab, denn Du hast mich unterwiesen.
Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
103 Wie hold ist meinem Gaumen Deine Rede, mehr als Honig meinem Munde.
Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
104 Von Deinen Ordnungen werde ich einsichtsvoll; darum hasse ich jeglichen Pfad der Lüge.
Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
105 Dein Wort ist eine Leuchte meinem Fuß, und ein Licht auf meinem Steig.
Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
106 Ich habe es geschworen und bestätige es, zu halten die Rechte Deiner Gerechtigkeit.
Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
107 Gar sehr bin ich gedemütigt; Jehovah, belebe mich nach Deinem Wort.
Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
108 Das Freiwillige meines Mundes lasse Dir doch wohlgefallen, o Jehovah, und lehre mich Deine Rechte.
Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
109 Meine Seele ist beständig in meinen Händen; und ich vergesse Deines Gesetzes nicht.
Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
110 Die Ungerechten legten Schlingen mir, doch irrte ich nicht ab von Deinen Ordnungen.
Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
111 Deine Zeugnisse sind mir ewiges Erbe; denn sie sind die Freude meines Herzens.
Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
112 Ich neige mein Herz, stets zu tun Deine Satzungen ewiglich.
Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
113 Ich hasse die Zweifler und liebe Dein Gesetz.
Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
114 Mein Schutz und mein Schild bist Du, ich warte auf Dein Wort.
Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
115 Weichet ab von mir, ihr Bösen; und ich will die Gebote meines Gottes bewahren.
Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
116 Sei mir zum Anhalt nach Deiner Rede, und ich werde leben und laß mich beschämt nicht werden mit meiner Erwartung.
Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
117 Labe Du mich, daß ich gerettet werde und beständig schaue auf Deine Satzungen.
Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
118 Alle trittst Du nieder, die fehlgehen von Deinen Satzungen; denn Lüge ist ihr Trug.
Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
119 Als Schlacken schaffst Du alle Ungerechten im Lande weg, darum liebe ich Deine Zeugnisse.
Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
120 Mein Fleisch durchschaudert der Schauer vor Dir, und vor Deinen Gerichten fürchte ich mich.
Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
121 Recht tue ich und Gerechtigkeit. Überlasse mich nicht denen, die mich niederdrükken.
Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
122 Sei Bürge für Deinen Knecht zum Guten, daß die Vermessenen mich nicht niederdrücken.
Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
123 Es verzehren sich meine Augen ob Deines Heils, und ob der Rede Deiner Gerechtigkeit.
Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
124 Tue mit Deinem Knecht nach Deiner Barmherzigkeit, und lehre mich Deine Satzungen.
Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
125 Dein Knecht bin ich, gib Du mir Einsicht, daß Deine Zeugnisse ich wisse.
Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
126 Zeit ist es zum Tun für Jehovah: sie haben Dein Gesetz zunichte gemacht.
Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
127 Darum liebe ich Deine Gebote mehr als Gold, und als feines Gold.
Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
128 Darum halte ich als gerade all Deine Ordnungen gänzlich; ich hasse allen Pfad der Lüge.
ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
129 Deine Zeugnisse sind wunderbar; darum bewahrt meine Seele sie.
Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
130 Die Eröffnung Deiner Worte erleuchtet, sie gibt Einsicht den Einfältigen.
Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
131 Ich öffne meinen Mund weit und lechze, denn nach Deinen Geboten sehne ich mich.
Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
132 Wende Dich zu mir und sei mir gnädig, nach dem Recht gegen die, so Deinen Namen lieben.
Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
133 Festige meine Tritte durch Deine Rede, und laß nicht irgendein Unrecht in mir walten.
Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
134 Erlöse mich von der Niederdrückung des Menschen, daß ich Deine Ordnungen halte.
Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
135 Laß Dein Angesicht leuchten auf Deinen Knecht, und lehre mich Deine Satzungen!
Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
136 Bächlein von Wasser rinnen herab von meinen Augen, über die, so nicht halten Dein Gesetz.
Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
137 Gerecht bist Du, Jehovah, und gerade sind Deine Gerichte.
Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
138 Gerechtigkeit gebietest Du in Deinen Zeugnissen und gar sehr die Wahrheit.
Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
139 Vertilgt hat mich mein Eifer, daß meine Dränger Deiner Worte vergessen haben.
Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
140 Sehr geläutert ist Deine Rede, und Dein Knecht liebt sie.
Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
141 Gering bin ich und verachtet, ich vergesse nicht Deiner Ordnungen.
Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
142 Ewiglich ist gerecht Deine Gerechtigkeit, und Wahrheit Dein Gesetz.
Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
143 Mich haben Drangsal und Angst betroffen; Deine Gebote sind mein Ergötzen.
Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
144 Gerechtigkeit sind Deine Zeugnisse ewiglich. Gib Einsicht mir, auf daß ich lebe.
Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
145 Von ganzem Herzen rufe ich: Antworte mir, Jehovah! Deine Satzungen will ich wahren.
Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
146 Ich rufe zu Dir: Rette mich, und ich halte Deine Zeugnisse!
Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
147 Früh in der Dämmerung stehe ich auf, und schreie, ich warte auf Deine Worte.
Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
148 Es kommen meine Augen den Nachtwachen zuvor, auf daß ich überdenke Deine Rede.
Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
149 Höre meine Stimme nach Deiner Barmherzigkeit, Jehovah, nach Deinem Rechte belebe mich.
Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
150 Es nahen sich die, die den Schandtaten nachsetzen, von Deinem Gesetz sind sie fern.
Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
151 Nahe bist Du, Jehovah, und Wahrheit sind alle Deine Gebote.
Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
152 Von der Vorzeit her weiß ich aus Deinen Zeugnissen, daß Du sie ewiglich gegründet hast.
Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
153 Siehe mein Elend und reiße mich heraus; denn Deines Gesetzes habe ich nicht vergessen.
Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
154 Hadere Du meinen Hader und erlöse mich. Belebe mich nach Deiner Rede.
Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
155 Fern von den Ungerechten ist das Heil, denn sie fragen nicht nach Deinen Satzungen.
Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
156 Viel sind, Jehovah, Deiner Erbarmungen. Nach Deinen Rechten belebe Du mich.
Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
157 Viel sind meiner Verfolger und meiner Dränger; ich wende mich nicht ab von Deinen Zeugnissen.
Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
158 Ich sehe die Treulosen und bin verdrossen, daß sie Deine Rede nicht halten.
Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
159 Siehe, wie ich liebe Deine Ordnungen, Jehovah, nach Deiner Barmherzigkeit belebe Du mich.
Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
160 Die Summe Deines Wortes ist Wahrheit, und ewig ist alles Gericht Deiner Gerechtigkeit.
Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
161 Oberste verfolgen mich ohne Ursache; und mein Herz scheut sich vor Deinen Worten.
Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
162 Ich freue mich Deiner Rede, wie einer, der viel Beute findet.
Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
163 Ich hasse die Lüge, und sie ist mir zum Greuel, ich liebe Dein Gesetz.
Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
164 Des Tages siebenmal lobe ich Dich wegen der Rechte Deiner Gerechtigkeit.
Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
165 Viel Frieden haben die, so Dein Gesetz lieben, und sie straucheln nicht.
Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
166 Ich habe Dein Heil erwartet, Jehovah, und getan nach Deinen Geboten.
Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
167 Meine Seele hält Deine Zeugnisse, und ich liebe sie sehr.
Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
168 Ich habe Deine Ordnungen und Zeugnisse gehalten; denn alle meine Wege sind vor Dir.
Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
169 Lasse meinen Klageruf Dir sich nahen, Jehovah, gib mir Einsicht nach Deinem Worte.
Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
170 Mein Flehen komme vor Dein Angesicht; errette mich nach Deiner Rede.
Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
171 Lasse meine Lippen hervorquellen Lob, denn Du lehrest mich Deine Satzungen.
Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
172 Meine Zunge antworte Deiner Rede; denn Gerechtigkeit sind alle Deine Gebote.
Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
173 Lasse Deine Hand mir zum Beistand sein, denn Deine Ordnungen habe ich erwählt.
Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
174 Nach Deinem Heil sehne ich mich, Jehovah, und Dein Gesetz ist mein Ergötzen.
Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
175 Laß meine Seele leben und Dich loben, und dein Gericht müsse mir beistehen.
Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
176 Wie ein verloren Schaf gehe ich in der Irre; suche Deinen Knecht! denn Deiner Gebote habe ich nicht vergessen.
Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.

< Psalm 119 >