< Psalm 103 >
1 Segne Jehovah, meine Seele, und all mein Inneres den Namen Seiner Heiligkeit.
Salimo la Davide. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga; ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.
2 Segne, Jehovah, meine Seele, und vergiß nicht aller Seiner Wohltaten.
Tamanda Yehova, iwe moyo wanga, ndipo usayiwale zabwino zake zonse.
3 Der dir vergibt alle deine Missetaten, Der alle deine Krankheiten heilt.
Amene amakhululuka machimo ako onse ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,
4 Der aus der Grube dein Leben erlöset, Der dich krönt mit Barmherzigkeit und Erbarmen.
amene awombola moyo wako ku dzenje ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,
5 Der deinen Mund mit Gutem sättigt, daß deine Jugend gleich dem Adler sich erneut.
amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino, kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.
6 Jehovah tut Gerechtigkeit und Gericht allen Niedergedrückten.
Yehova amachita chilungamo ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.
7 Kund tat Er Mose Seine Wege, Seine Handlungen den Söhnen Israels.
Iye anadziwitsa Mose njira zake, ntchito zake kwa Aisraeli.
8 Erbarmungsvoll und gnädig ist Jehovah, langmütig und von großer Barmherzigkeit.
Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.
9 Er hadert nicht immerdar, noch trägt Er ewiglich nach.
Iye sadzatsutsa nthawi zonse, kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;
10 Nicht hat Er uns nach unseren Sünden getan, noch vergalt Er uns nach unseren Missetaten.
satichitira molingana ndi machimo athu, kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.
11 Denn so hoch der Himmel über der Erde ist, so mächtig ist Seine Barmherzigkeit für die, so Ihn fürchten.
Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;
12 So fern der Aufgang ist vom Abend, so weit von uns entfernt Er unsere Übertretungen.
monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo, koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.
13 Wie sich ein Vater über die Söhne erbarmt, erbarmt Jehovah derer Sich, so Ihn fürchten.
Monga bambo amachitira chifundo ana ake, choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa;
14 Denn Er kennt, was für ein Gebilde wir sind, Er gedenkt, daß wir sind Staub.
pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira, amakumbukira kuti ndife fumbi.
15 Der Mensch, wie Gras sind seine Tage; wie des Feldes Blume, also blüht er.
Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu, amaphuka ngati duwa la mʼmunda;
16 Wenn der Wind über sie dahingeht, ist sie nicht mehr, und man erkennt nicht mehr ihren Ort.
koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso ndipo malo ake sakumbukirikanso.
17 Jehovahs Barmherzigkeit aber ist von Ewigkeit zu Ewigkeit über die, so Ihn fürchten, und Seine Gerechtigkeit auf der Söhne Söhne,
Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa, ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo;
18 Auf die, so halten Seinen Bund und Seiner Ordnungen gedenken, daß sie danach tun.
iwo amene amasunga pangano lake ndi kukumbukira kumvera malangizo ake.
19 Jehovah hat im Himmel Seinen Thron bereitet, und Sein Reich herrscht über alles.
Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba ndipo ufumu wake umalamulira onse.
20 Segnet Jehovah, ihr, Seine Engel, ihr Helden der Kraft, die Sein Wort tun, auf daß man auf die Stimme Seines Wortes höre!
Tamandani Yehova, inu angelo ake, amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula, amene mumamvera mawu ake.
21 Segnet Jehovah, alle Seine Heerscharen, Seine Diener, die nach Seinem Wohlgefallen tun!
Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba, inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake.
22 Segnet Jehovah, alle Seine Werke an allen Orten Seiner Herrschaft! Segne, meine Seele, den Jehovah!
Tamandani Yehova, ntchito yake yonse kulikonse mu ulamuliro wake. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.