< 1 Thessalonicher 5 >
1 Über Zeit und Zeitumstände, Brüder, ist nicht Not, euch zu schreiben;
Tsono abale, za nthawi ndi nyengo yake nʼkosafunikira kuti tikulembereni,
2 Ihr wißt ja selbst genau, daß der Tag des Herrn kommen wird wie ein Dieb in der Nacht.
chifukwa mukudziwa bwino lomwe kuti tsiku la Ambuye lidzafika ngati mbala usiku.
3 Denn wenn sie sagen: Es ist Friede, ist keine Gefahr, so steht plötzlich das Verderben vor der Tür, wie die Wehen vor dem Weib, das gebären soll; und sie können nicht entfliehen.
Pamene anthu akunena kuti, “Mtendere ndi chitetezo,” chiwonongeko chidzafika pa iwo mwadzidzidzi, monga zowawa za amayi pobereka, ndipo sadzathawa.
4 Ihr aber, Brüder, seid nicht in Finsternis, so daß euch der Tag wie der Dieb überfalle.
Koma inu abale, simuli mu mdima kuti tsiku limeneli lidzakudzidzimutseni ngati mbala.
5 Ihr alle seid ja Kinder des Lichts und Kinder des Tags; wir sind nicht von der Nacht, noch von der Finsternis.
Nonse ndinu ana a kuwunika ndi ana a usana. Sindife anthu a usiku kapena mdima.
6 So laßt uns denn nicht schlafen, wie die anderen, sondern wachen und nüchtern sein.
Chomwecho tsono, tisafanane ndi ena amene akugona koma tikhale maso ndi odzisunga.
7 Denn die da schlafen, schlafen in der Nacht, und die da trunken sind, sind trunken in der Nacht.
Pakuti amene akugona, amagona usiku, ndi amene amaledzera, amaledzera usiku.
8 Wir aber, die wir vom Tage sind, wollen nüchtern sein, mit dem Panzer des Glaubens und der Liebe angetan, und mit dem Helm der Hoffnung zur Seligkeit.
Koma popeza ndife a usana, tikhale odzisunga, titavala chikhulupiriro ndi chikondi ngati chovala pachifuwa, ndi chiyembekezo cha chipulumutso ngati chipewa.
9 Denn Gott hat uns nicht gesetzt zum Zorn, sondern zur Erlangung der Seligkeit durch unseren Herrn Jesus Christus, Der für uns gestorben ist.
Pakuti Mulungu sanatisankhe kuti tikavutike ndi mkwiyo koma kuti tilandire chipulumutso kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu.
10 Auf daß wir, ob wir wachen oder schlafen, zugleich mit Ihm leben sollen.
Iye anatifera ndi cholinga chakuti, kaya tili ndi moyo kapena tagona, tikhale naye pamodzi.
11 Darum ermahnt einander und erbaue einer den anderen, wie ihr denn auch tut.
Choncho limbikitsanani wina ndi mnzake ndi kuthandizana kukula mu mzimu, monga momwe mukuchitira.
12 Wir bitten euch aber, Brüder, daß ihr sorgt für die, welche an euch arbeiten und euch vorstehen in dem Herrn und euch vermahnen.
Tsopano tikukupemphani abale kuti muziwalemekeza amene akugwira ntchito pakati panu, amene amakuyangʼanirani mwa Ambuye ndi amene amakulimbikitsani.
13 Und haltet sie hoch in eurer Liebe, um ihres Werkes willen. Haltet Frieden untereinander.
Muziwachitira ulemu kwambiri mwachikondi chifukwa cha ntchito yawo. Mukhale pa mtendere wina ndi mnzake.
14 Wir ermahnen euch aber, liebe Brüder, weiset zurecht die Unordentlichen, tröstet die Kleinmütigen, nehmt euch der Schwachen an, seid langmütig gegen alle.
Ndipo tikukupemphani abale, muwachenjeze amene akungokhala osagwira ntchito, alimbikitseni amanyazi, thandizani ofowoka ndipo muzilezera mtima aliyense.
15 Seht darauf, daß keiner Böses mit Bösem vergelte, sondern jagt allezeit dem Guten nach, beides, untereinander und gegen jedermann.
Onetsetsani kuti wina asabwezere choyipa kwa omuchitira choyipa koma nthawi zonse yesetsani kukhala okoma mtima kwa wina ndi mnzake; ndiponso ndi kwa anthu ena onse.
16 Seid allezeit frohen Mutes.
Kondwerani nthawi zonse.
18 Seid dankbar in allen Dingen, denn das ist der Wille Gottes in Christus Jesus an euch.
Yamikani mu zonse, pakuti ichi ndi chifuniro cha Mulungu kwa inu mwa Khristu Yesu.
19 Den Geist dämpfet nicht.
Musazimitse moto wa Mzimu Woyera.
20 Mißachtet nicht Weissagungen,
Musanyoze mawu a uneneri.
21 Sondern prüft alles, das Gute behaltet!
Yesani zinthu zonse. Gwiritsitsani chimene ndi chabwino.
22 Meidet allen bösen Schein.
Mupewe choyipa cha mtundu wina uliwonse.
23 Er aber, der Gott des Friedens, heilige euch durch und durch, und Geist, Seele und Leib möge an euch völlig unsträflich erhalten werden für die Zukunft unseres Herrn Jesus Christus.
Mulungu mwini, Mulungu wamtendere, akuyeretseni kotheratu. Mzimu wanu wonse, moyo ndi thupi zisungidwe zopanda cholakwa mpaka kubwera kwa Ambuye athu Yesu Khristu.
24 Treu ist Er, Der euch ruft, und wird es auch vollbringen.
Amene anakuyitanani ndi wokhulupirika ndipo Iye adzachita zimenezi.
25 Brüder, betet für uns!
Abale, mutipempherere.
26 Grüßet alle Brüder mit dem heiligen Kuß.
Perekani moni wachikondi kwa onse.
27 Ich beschwöre euch bei dem Herrn, daß ihr diesen Brief alle heiligen Brüder lesen lasset.
Pamaso pa Ambuye ndikulamula kuti kalatayi iwerengedwe kwa abale onse.
28 Die Gnade unseres Herrn Jesu Christi sei mit euch! Amen.
Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu chikhale nanu.