< Psalm 94 >

1 Gott der Rache, o HERR, du Gott der Rache, brich hervor!
Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango, Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.
2 Erhebe dich, du Richter der Erde, gib den Stolzen ihren Lohn!
Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi; bwezerani kwa odzikuza zowayenera.
3 Wie lange sollen die Gottlosen, o HERR, wie lange sollen die Gottlosen frohlocken?
Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova, mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?
4 Sie halten viele und freche Reden; stolz überheben sich alle Übeltäter.
Amakhuthula mawu onyada; onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.
5 Sie knebeln dein Volk, o HERR, und unterdrücken dein Erbteil.
Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova; amapondereza cholowa chanu.
6 Sie erwürgen Witwen und Fremdlinge und ermorden Waisen;
Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko; amapha ana amasiye.
7 und dann sagen sie: «Der HERR sieht es nicht, und der Gott Jakobs achtet es nicht!»
Iwo amati, “Yehova sakuona; Mulungu wa Yakobo salabadirako.”
8 Nehmt doch Verstand an, ihr Unvernünftigen unter dem Volk, ihr Toren, wann wollt ihr klug werden?
Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu; zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?
9 Der das Ohr gepflanzt hat, sollte der nicht hören? Der das Auge gebildet hat, sollte der nicht sehen?
Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva? Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?
10 Der die Nationen züchtigt, sollte der nicht strafen, er, der die Menschen Erkenntnis lehrt?
Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga? Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?
11 Der HERR kennt die Anschläge der Menschen, [weiß, ] daß sie vergeblich sind.
Yehova amadziwa maganizo a munthu; Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.
12 Wohl dem Mann, den du, HERR, züchtigst und den du aus deinem Gesetze belehrst,
Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza, munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;
13 ihm Ruhe zu geben vor den Tagen des Unglücks, bis dem Gottlosen die Grube gegraben wird.
mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto, mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.
14 Denn der HERR wird sein Volk nicht verstoßen und sein Erbteil nicht verlassen;
Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake; Iye sadzasiya cholowa chake.
15 denn zur Gerechtigkeit kehrt das Gericht zurück, und alle aufrichtigen Herzen werden ihm folgen!
Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo, ndipo onse olungama mtima adzachitsata.
16 Wer steht mir bei wider die Bösen, wer tritt für mich ein wider die Übeltäter?
Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa? Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?
17 Wäre der HERR nicht meine Hilfe, wie bald würde meine Seele in der Totenstille wohnen!
Yehova akanapanda kundithandiza, bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.
18 Sooft ich aber auch sprach: «Mein Fuß ist wankend geworden», hat deine Gnade, o HERR, mich gestützt.
Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,” chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.
19 Bei den vielen Sorgen in meinem Herzen erquickten deine Tröstungen meine Seele.
Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga, chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.
20 Sollte mit dir Gemeinschaft haben der Thron des Verderbens, der Unheil schafft; durch Gesetz?
Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?
21 Sie greifen die Seele des Gerechten an und verdammen unschuldiges Blut.
Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.
22 Aber der HERR ward mir zur festen Burg, zum Felsen, wo ich Zuflucht fand.
Koma Yehova wakhala linga langa, ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.
23 Und er ließ ihr Unrecht auf sie selber fallen, und er wird sie durch ihre eigene Bosheit vertilgen; der HERR, unser Gott, wird sie vertilgen.
Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo; Yehova Mulungu wathu adzawawononga.

< Psalm 94 >