< Psalm 83 >

1 Ein Psalmlied; von Asaph. Bleibe nicht stille, o Gott, schweige nicht und halte nicht inne!
Nyimbo. Salimo la Asafu. Inu Mulungu musakhale chete; musangoti phee, Mulungu musangoti duu.
2 Denn siehe, deine Feinde toben, und die dich hassen, erheben das Haupt.
Onani adani anu akuchita chiwawa, amene amadana nanu autsa mitu yawo.
3 Sie machen listige Anschläge wider dein Volk, verabreden sich wider deine Schutzbefohlenen.
Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu; Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.
4 Sie sprechen: «Kommt, wir wollen sie vertilgen, daß sie kein Volk mehr seien, daß des Namens Israel nicht mehr gedacht werde!»
Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”
5 Ja, sie fassen einen einmütigen Beschluß, sie schließen einen Bund wider dich;
Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu; Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:
6 die Zelte Edoms und die Ismaeliter, Moab und die Hagariter;
Matenti a Edomu ndi Aismaeli, Mowabu ndi Ahagiri,
7 Gebal, Ammon und Amalek, die Philister samt denen zu Tyrus.
Agebala, Aamoni ndi Aamaleki, Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.
8 Auch Assur hat sich mit ihnen befreundet und leiht den Kindern Lots seinen Arm. (Pause)
Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo kupereka mphamvu kwa ana a Loti. (Sela)
9 Tue ihnen wie Midian, wie Sisera, wie Jabin am Bach Kison,
Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani, monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.
10 die vertilgt wurden zu Endor, zu Dünger wurden fürs Ackerfeld.
Amene anawonongedwa ku Endori ndi kukhala ngati zinyalala.
11 Mache ihre Edlen wie Oreb und Seb, wie Sebach und Zalmuna alle ihre Fürsten,
Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,
12 die da sagen: «Wir wollen die Wohnstätten Gottes für uns erobern!»
amene anati, “Tiyeni tilande dziko la msipu la Mulungu.”
13 O Gott, setze sie dem Wirbelsturm aus, mache sie wie Stoppeln vor dem Wind;
Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga, ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.
14 wie ein Feuer, das den Wald verbrennt, und wie eine Flamme, welche die Berge versengt;
Monga moto umatentha nkhalango, kapena malawi a moto kuyatsa phiri,
15 also verfolge sie mit deinem Wetter und schrecke sie mit deinem Sturm!
kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho, ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.
16 Mache ihr Angesicht voll Schande, daß sie deinen Namen suchen, o HERR!
Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.
17 Laß sie beschämt und abgeschreckt werden für immer, laß sie schamrot werden und umkommen,
Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse; awonongeke mwa manyazi.
18 so daß sie erfahren müssen, daß du, der du HERR heißest, allein der Höchste bist über die ganze Erde!
Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova, ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.

< Psalm 83 >