< Psalm 82 >

1 Ein Psalm Asaphs. Gott steht in der Gottesversammlung, inmitten der Götter richtet er:
Salimo la Asafu. Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu; Iye akuweruza pakati pa “milungu.”
2 «Wie lange wollt ihr ungerecht richten und die Person des Schuldigen ansehen? (Pause)
“Mudzateteza osalungama mpaka liti, ndi kukondera anthu oyipa?
3 Schafft dem Geringen und Verwaisten Recht, rechtfertigt den Elenden und Armen!
Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye; mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.
4 Lasset den Geringen und Dürftigen frei, errettet ihn aus der Hand der Gottlosen!»
Landitsani anthu ofowoka ndi osowa; apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.
5 Aber sie wollen nichts merken und nichts verstehen, sondern wandeln in der Finsternis; es wanken alle Stützen des Landes!
“Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse. Amayendayenda mu mdima; maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.
6 Ich habe gesagt: «Ihr seid Götter und allzumal Kinder des Höchsten;
“Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu, nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’
7 dennoch sollt ihr sterben wie Menschen und fallen wie einer der Fürsten!»
Koma mudzafa ngati anthu wamba; mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”
8 Mache dich auf, o Gott, richte die Erde; denn du bist Erbherr über alle Nationen!
Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi, pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.

< Psalm 82 >