< Psalm 29 >

1 Ein Psalm Davids. Gebt dem HERRN, ihr Gottessöhne, gebt dem HERRN Ehre und Macht!
Salimo la Davide. Perekani kwa Yehova, inu anthu amphamvu, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
2 Gebt dem HERRN seines Namens Ehre, betet den HERRN an in heiligem Schmuck!
Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake, pembedzani Yehova mwa kukongola kwa chiyero chake.
3 Die Stimme des HERRN schallt über den Wassern, der Gott der Ehren donnert, der HERR über großen Wassern.
Liwu la Yehova lili pamwamba pa madzi; Mulungu waulemerero abangula, Yehova abangula pamwamba pa madzi amphamvu.
4 Die Stimme des HERRN ist stark, die Stimme des HERRN ist herrlich.
Liwu la Yehova ndi lamphamvu; liwu la Yehova ndi laulemerero.
5 Die Stimme des HERRN zerbricht die Zedern, der HERR zerbricht die Zedern des Libanon
Liwu la Yehova limathyola mikungudza; Yehova amathyolathyola mikungudza ya ku Lebanoni.
6 und macht sie hüpfen wie ein Kälbchen, den Libanon und den Sirjon wie einen jungen Büffel.
Iye amachititsa Lebanoni kulumphalumpha ngati mwana wangʼombe, Siriyoni ngati mwana wa njati:
7 Die Stimme des HERRN sprüht Feuerflammen,
Liwu la Yehova limakantha ngati kungʼanima kwa mphenzi.
8 die Stimme des HERRN erschüttert die Wüste, der HERR erschüttert die Wüste Kadesch.
Liwu la Yehova limagwedeza chipululu; Yehova amagwedeza chipululu cha Kadesi.
9 Die Stimme des HERRN macht Hindinnen gebären und entblättert Wälder, und in seinem Tempel ruft ihm jedermann Ehre zu.
Liwu la Yehova limapindapinda mibawa ndi kuyeretsa nkhalango. Ndipo mʼNyumba mwake onse amafuwula kuti, “Ulemerero!”
10 Der HERR regierte zur Zeit der Sündflut, und der HERR herrscht als König in Ewigkeit.
Yehova amakhala pamwamba pa madzi osefukira, Yehova ndiye mfumu kwamuyaya.
11 Der HERR wird seinem Volke Kraft verleihen, der HERR wird sein Volk segnen mit Frieden!
Yehova amapereka mphamvu kwa anthu ake; Yehova amadalitsa anthu ake ndi mtendere.

< Psalm 29 >