< Psalm 150 >
1 Hallelujah! Lobet Gott in seinem Heiligtum, lobet ihn in der Feste seiner Macht!
Tamandani Yehova. Tamandani Mulungu mʼmalo ake opatulika; mutamandeni ku thambo lake lamphamvu.
2 Lobet ihn wegen seiner mächtigen Taten, lobet ihn ob seiner großen Majestät!
Mutamandeni chifukwa cha machitidwe ake amphamvu; mutamandeni chifukwa cha ukulu wake wopambana.
3 Lobet ihn mit Posaunenschall, lobet ihn mit Psalter und Harfe!
Mutamandeni poyimba malipenga, mutamandeni ndi pangwe ndi zeze.
4 Lobet ihn mit Pauken und Reigen, lobet ihn mit Saitenspiel und Flöte!
Mutamandeni ndi matambolini ndi kuvina, mutamandeni ndi zingwe ndi zitoliro.
5 Lobet ihn mit hellen Zimbeln, lobet ihn mit lauten Zimbeln!
Mutamandeni ndi ziwaya zolira za malipenga, mutamandeni ndi ziwaya zolira kwambiri.
6 Alles, was Odem hat, lobe den HERRN! Hallelujah!
Chamoyo chilichonse chopuma chitamande Yehova. Tamandani Yehova.