< Psalm 137 >
1 An den Strömen Babels saßen wir und weinten, wenn wir Zions gedachten.
Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira pamene tinakumbukira Ziyoni.
2 An den Weiden, die dort sind, hängten wir unsre Harfen auf.
Kumeneko, pa mitengo ya misondozi tinapachika apangwe athu,
3 Denn die uns daselbst gefangen hielten, forderten Lieder von uns, und unsre Peiniger, daß wir fröhlich seien: «Singet uns eines von den Zionsliedern!»
pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo. Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo; iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”
4 Wie sollten wir des HERRN Lied singen auf fremdem Boden?
Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova mʼdziko lachilendo?
5 Vergesse ich deiner, Jerusalem, so verdorre meine Rechte!
Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu, dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.
6 Meine Zunge müsse an meinem Gaumen kleben, wenn ich deiner nicht gedenke, wenn ich Jerusalem nicht über meine höchste Freude setze!
Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu, ngati sindiyesa iwe chimwemwe changa chachikulu.
7 Gedenke, HERR, den Kindern Edoms den Tag Jerusalems, wie sie sprachen: «Zerstöret, zerstöret sie bis auf den Grund!»
Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita pa tsiku limene Yerusalemu anagonja. Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi mpaka pa maziko ake!”
8 Tochter Babel, du Verwüsterin! Wohl dem, der dir vergilt, was du uns angetan!
Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa, wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera pa zimene watichitira.
9 Wohl dem, der deine Kindlein nimmt und sie zerschmettert am Felsgestein!
Amene adzagwira makanda ako ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.