< Psalm 119 >

1 Wohl denen, deren Weg unsträflich ist, die da wandeln nach dem Gesetze des HERRN!
Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
2 Wohl denen, die seine Zeugnisse beobachten, die ihn von ganzem Herzen suchen,
Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
3 die auch kein Unrecht getan haben, die auf seinen Wegen gegangen sind!
Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
4 Du hast deine Befehle gegeben, daß man sie fleißig beobachte.
Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
5 O daß meine Wege dahin zielten, deine Satzungen zu befolgen!
Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
6 Dann werde ich nicht zuschanden, wenn ich auf alle deine Gebote sehe.
Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
7 Ich werde dir mit aufrichtigem Herzen danken, wenn ich die Verordnungen deiner Gerechtigkeit lerne.
Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
8 Deine Satzungen will ich befolgen; verlaß mich nicht ganz und gar!
Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
9 Wie wird ein Jüngling seinen Weg unsträflich gehen? Wenn er sich hält nach deinem Wort!
Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
10 Ich habe dich von ganzem Herzen gesucht; laß mich nicht abirren von deinen Geboten!
Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
11 Ich habe dein Wort in meinem Herzen geborgen, auf daß ich nicht an dir sündige.
Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
12 Gelobt seist du, o HERR! Lehre mich deine Satzungen.
Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
13 Mit meinen Lippen zähle ich alle Verordnungen deines Mundes auf.
Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
14 Ich freue mich des Weges deiner Zeugnisse, wie über lauter Reichtümer.
Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
15 Ich will über deine Wege nachsinnen und auf deine Pfade achten.
Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
16 Ich habe meine Lust an deinen Satzungen und vergesse deines Wortes nicht.
Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
17 Gewähre deinem Knecht, daß ich lebe und dein Wort befolge!
Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
18 Öffne meine Augen, daß ich erblicke die Wunder in deinem Gesetz!
Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
19 Ich bin ein Gast auf Erden; verbirg deine Gebote nicht vor mir!
Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
20 Meine Seele ist zermalmt vor Sehnsucht nach deinen Verordnungen allezeit.
Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
21 Du hast die Übermütigen gescholten, die Verfluchten, welche von deinen Geboten abirren.
Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
22 Wälze Schimpf und Schande von mir ab; denn ich habe deine Zeugnisse bewahrt!
Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
23 Sogar Fürsten sitzen und bereden sich wider mich; aber dein Knecht sinnt über deine Satzungen.
Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
24 Ja, deine Zeugnisse sind meine Freude; sie sind meine Ratgeber.
Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
25 Meine Seele klebt am Staube; belebe mich nach deiner Verheißung!
Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
26 Ich habe meine Wege erzählt, und du hast mir geantwortet; lehre mich deine Satzungen!
Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
27 Laß mich den Weg deiner Befehle verstehen und deine Wunder betrachten!
Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
28 Meine Seele weint vor Kummer; richte mich auf nach deinem Wort!
Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
29 Entferne von mir den falschen Weg und begnadige mich mit deinem Gesetz!
Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
30 Ich habe den Weg der Wahrheit erwählt und deine Verordnungen vor mich hingestellt.
Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
31 HERR, ich hange an deinen Zeugnissen; laß mich nicht zuschanden werden!
Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
32 Ich laufe den Weg deiner Gebote; denn du machst meinem Herzen Raum.
Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
33 Zeige mir, HERR, den Weg deiner Satzungen, daß ich ihn bewahre bis ans Ende.
Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
34 Unterweise mich, so will ich dein Gesetz bewahren und es von ganzem Herzen befolgen.
Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
35 Laß mich wandeln auf dem Pfad deiner Gebote; denn ich habe Lust daran.
Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
36 Neige mein Herz zu deinen Zeugnissen und nicht zur Habsucht!
Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
37 Wende meine Augen ab, daß sie nicht nach Eitlem sehen; erquicke mich auf deinen Wegen!
Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
38 Erfülle an deinem Knechte deine Verheißung, die denen gilt, die dich fürchten.
Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
39 Wende die Beschimpfung von mir ab, die ich fürchte; denn deine Verordnungen sind gut!
Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
40 Siehe, ich sehne mich nach deinen Befehlen; erquicke mich durch deine Gerechtigkeit!
Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
41 Deine Gnade, o HERR, komme über mich, dein Heil nach deinem Wort!
Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
42 Damit ich dem antworten kann, der mich schmäht; denn ich verlasse mich auf dein Wort.
ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
43 Und entziehe nicht allzusehr meinem Munde das Wort der Wahrheit; denn ich harre auf deine Verordnungen!
Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
44 Und ich will dein Gesetz stets bewahren, immer und ewiglich.
Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
45 Und ich möchte auf weitem Raum wandeln; denn ich habe deine Befehle erforscht.
Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
46 Und ich will von deinen Zeugnissen reden vor Königen und mich nicht schämen.
Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
47 Und ich will mich an deinen Befehlen vergnügen; denn ich liebe sie.
popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
48 Und ich will meine Hände nach deinen Befehlen ausstrecken, weil ich sie liebe, und will nachdenken über deine Satzungen.
Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
49 Gedenke des Wortes an deinen Knecht, auf welches du mich hoffen ließest!
Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
50 Das ist mein Trost in meinem Elend, daß dein Wort mich erquickt.
Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
51 Die Übermütigen haben mich arg verspottet; dennoch bin ich von deinem Gesetz nicht abgewichen.
Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
52 Ich gedachte deiner Verordnungen, HERR, die von Ewigkeit her sind, und das tröstete mich.
Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
53 Zornglut hat mich ergriffen wegen der Gottlosen, die dein Gesetz verlassen.
Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
54 Deine Satzungen sind meine Lieder geworden im Hause meiner Wallfahrt.
Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
55 HERR, des Nachts habe ich an deinen Namen gedacht und dein Gesetz bewahrt.
Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
56 Das ist mir zuteil geworden, daß ich deine Befehle befolgen darf.
Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
57 Ich sage: Das ist mein Teil, o HERR, die Beobachtung deiner Worte!
Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
58 Ich flehe von ganzem Herzen um deine Gunst: Sei mir gnädig, wie du verheißen hast!
Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
59 Als ich meine Wege überlegte, wandte ich meine Füße zu deinen Zeugnissen.
Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
60 Ich habe mich beeilt und nicht gesäumt, deine Gebote zu befolgen.
Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
61 Als die Schlingen der Gottlosen mich umgaben, vergaß ich deines Gesetzes nicht.
Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
62 Mitten in der Nacht stehe ich auf, dir zu danken für die Verordnungen deiner Gerechtigkeit.
Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
63 Ich bin verbunden mit allen, die dich fürchten, und die deine Befehle befolgen.
Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
64 HERR, die Erde ist voll deiner Gnade; lehre mich deine Satzungen!
Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
65 Du hast deinem Knechte wohlgetan, o HERR, nach deinem Wort.
Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
66 Lehre mich rechte Einsicht und Verständnis; denn ich vertraue deinen Befehlen.
Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
67 Ehe ich gedemütigt ward, irrte ich, nun aber befolge ich dein Wort.
Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
68 Du bist gut und wohltätig; lehre mich deine Satzungen!
Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
69 Die Stolzen haben mich mit Lügen besudelt; ich beobachte von ganzem Herzen deine Befehle.
Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
70 Ihr Herz ist stumpf wie von Fett; ich aber vergnüge mich an deinem Gesetz.
Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
71 Es war gut für mich, daß ich gedemütigt wurde, auf daß ich deine Satzungen lernte.
Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
72 Das Gesetz deines Mundes ist besser für mich als Tausende von Gold und Silberstücken.
Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
73 Deine Hände haben mich gemacht und bereitet; gib mir Verstand, daß ich deine Befehle lerne!
Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
74 Die dich fürchten, werden mich sehen und sich freuen, daß ich auf dein Wort gewartet habe.
Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
75 HERR, ich weiß, daß deine Verordnungen gerecht sind und daß du mich in Treue gedemütigt hast.
Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
76 Laß doch deine Gnade mir zum Trost gereichen, wie du deinem Knechte zugesagt hast!
Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
77 Laß mir deine Barmherzigkeit widerfahren, daß ich lebe! Denn dein Gesetz ist meine Lust.
Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
78 Laß die Stolzen zuschanden werden, weil sie mir mit Lügen Unrecht getan; ich aber denke über deine Befehle nach.
Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
79 Mir wird zufallen, wer dich fürchtet und deine Zeugnisse anerkennt.
Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
80 Mein Herz soll sich gänzlich an deine Satzungen halten, damit ich nicht zuschanden werde.
Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
81 Meine Seele schmachtet nach deinem Heil; ich harre auf dein Wort.
Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
82 Meine Augen schmachten nach deinem Wort und fragen: Wann wirst du mich trösten?
Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
83 Bin ich auch geworden wie ein Schlauch im Rauch, so habe ich doch deiner Satzungen nicht vergessen.
Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
84 Wieviel sind noch der Tage deines Knechtes? Wann willst du an meinen Verfolgern das Urteil vollziehen?
Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
85 Die Übermütigen haben mir Gruben gegraben, sie, die sich nicht nach deinem Gesetze richten.
Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
86 Alle deine Gebote sind Wahrheit; sie aber verfolgen mich mit Lügen; hilf mir!
Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
87 Sie hätten mich fast umgebracht auf Erden; dennoch verließ ich deine Befehle nicht.
Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
88 Erhalte mich am Leben nach deiner Gnade, so will ich die Zeugnisse deines Mundes bewahren.
Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
89 Auf ewig, o HERR, steht dein Wort im Himmel fest;
Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
90 von einem Geschlecht zum andern währt deine Treue! Du hast die Erde gegründet, und sie steht;
Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
91 nach deinen Ordnungen stehen sie noch heute; denn es muß dir alles dienen!
Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
92 Wäre dein Gesetz nicht meine Lust gewesen, so wäre ich vergangen in meinem Elend.
Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
93 Ich will deine Befehle auf ewig nicht vergessen; denn durch sie hast du mich belebt.
Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
94 Ich bin dein; rette mich, denn ich habe deine Befehle gesucht!
Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
95 Die Gottlosen lauern mir auf, um mich zu verderben; aber ich merke auf deine Zeugnisse.
Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
96 Von aller Vollkommenheit habe ich ein Ende gesehen; aber dein Gebot ist unbeschränkt.
Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
97 Wie habe ich dein Gesetz so lieb! Ich denke darüber nach den ganzen Tag.
Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
98 Dein Gebot macht mich weiser als meine Feinde; denn es bleibt ewiglich bei mir.
Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
99 Ich bin verständiger geworden als alle meine Lehrer, denn deine Zeugnisse sind mein Sinnen.
Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
100 Ich bin einsichtiger als die Alten; denn ich achte auf deine Befehle.
Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
101 Von allen schlechten Wegen habe ich meine Füße abgehalten, um dein Wort zu befolgen.
Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
102 Von deinen Verordnungen bin ich nicht abgewichen; denn du hast mich gelehrt.
Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
103 Wie süß ist deine Rede meinem Gaumen, mehr denn Honig meinem Mund!
Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
104 Von deinen Befehlen werde ich verständig; darum hasse ich jeden Lügenpfad.
Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
105 Dein Wort ist meines Fußes Leuchte und ein Licht für meinen Pfad.
Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
106 Ich habe geschworen und werde es halten, daß ich die Verordnungen deiner Gerechtigkeit bewahren will.
Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
107 Ich bin tief gebeugt; HERR, erquicke mich nach deinem Wort!
Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
108 HERR, laß dir wohlgefallen die freiwilligen Opfer meines Mundes und lehre mich deine Verordnungen!
Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
109 Meine Seele ist beständig in meiner Hand, und ich vergesse deines Gesetzes nicht.
Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
110 Die Gottlosen haben mir eine Schlinge gelegt; aber ich bin von deinen Befehlen nicht abgeirrt.
Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
111 Deine Zeugnisse sind mein ewiges Erbe; denn sie sind meines Herzens Wonne.
Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
112 Ich habe mein Herz geneigt, deine Satzungen auf ewig zu erfüllen.
Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
113 Ich hasse die Unentschiedenen; aber dein Gesetz habe ich lieb.
Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
114 Du bist mein Schirm und mein Schild; ich harre auf dein Wort.
Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
115 Weichet von mir, ihr Übeltäter, daß ich die Gebote meines Gottes befolge!
Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
116 Unterstütze mich nach deiner Verheißung, daß ich lebe und nicht zuschanden werde mit meiner Hoffnung!
Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
117 Stärke du mich, so ist mir geholfen und ich werde mich an deinen Satzungen stets ergötzen!
Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
118 Du wirst alle zu leicht erfinden, die von deinen Satzungen abweichen; denn eitel Betrug ist ihre Täuschung.
Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
119 Wie Schlacken räumst du alle Gottlosen von der Erde fort; darum liebe ich deine Zeugnisse.
Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
120 Mein Fleisch schaudert aus Furcht vor dir, und ich habe Ehrfurcht vor deinen Verordnungen!
Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
121 Ich habe Recht und Gerechtigkeit geübt; überlaß mich nicht meinen Unterdrückern!
Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
122 Stehe ein zum Besten deines Knechtes, daß mich die Übermütigen nicht unterdrücken!
Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
123 Meine Augen schmachten nach deinem Heil und nach dem Wort deiner Gerechtigkeit.
Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
124 Handle mit deinem Knecht nach deiner Gnade und lehre mich deine Satzungen!
Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
125 Ich bin dein Knecht; unterweise mich, daß ich deine Zeugnisse verstehe!
Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
126 Es ist Zeit, daß der HERR handle; sie haben dein Gesetz gebrochen!
Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
127 Darum liebe ich deine Befehle mehr als Gold und als feines Gold;
Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
128 darum lobe ich mir alle deine Gebote und hasse jeden trügerischen Pfad.
ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
129 Wunderbar sind deine Zeugnisse; darum bewahrt sie meine Seele.
Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
130 Die Erschließung deiner Worte erleuchtet und macht die Einfältigen verständig.
Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
131 Begierig öffne ich meinen Mund; denn mich verlangt nach deinen Befehlen.
Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
132 Wende dich zu mir und sei mir gnädig nach dem Rechte derer, die deinen Namen lieben.
Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
133 Mache meine Schritte fest durch dein Wort und laß kein Unrecht über mich herrschen!
Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
134 Erlöse mich von der Bedrückung durch Menschen, so will ich deine Befehle befolgen!
Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
135 Laß dein Angesicht leuchten über deinen Knecht und lehre mich deine Satzungen!
Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
136 Tränenströme fließen aus meinen Augen, weil man dein Gesetz nicht befolgt.
Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
137 HERR, du bist gerecht, und deine Verordnungen sind richtig!
Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
138 Du hast deine Zeugnisse gerecht und sehr treu abgefaßt.
Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
139 Mein Eifer hat mich verzehrt, weil meine Feinde deine Worte vergessen haben.
Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
140 Deine Rede ist wohlgeläutert, und dein Knecht hat sie lieb.
Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
141 Ich bin gering und verachtet; deine Befehle habe ich nicht vergessen.
Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
142 Deine Gerechtigkeit ist auf ewig gerecht, und dein Gesetz ist Wahrheit.
Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
143 Angst und Not haben mich betroffen; aber deine Befehle sind meine Lust.
Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
144 Deine Zeugnisse sind auf ewig gerecht; unterweise mich, so werde ich leben!
Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
145 Ich rufe von ganzem Herzen: HERR, erhöre mich; deine Satzungen will ich befolgen!
Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
146 Ich rufe zu dir; errette mich, so will ich deine Zeugnisse bewahren!
Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
147 Vor der Morgendämmerung komme ich und schreie; ich harre auf dein Wort.
Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
148 Meine Augen kommen den Nachtwachen zuvor, daß ich über deine Reden nachdenke.
Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
149 Höre meine Stimme nach deiner Gnade, o HERR, erquicke mich nach deinem Recht!
Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
150 Die dem Laster nachjagen, sind nah; von deinem Gesetz sind sie fern.
Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
151 Du bist nahe, o HERR, und alle deine Gebote sind wahr.
Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
152 Längst weiß ich aus deinen Zeugnissen, daß du sie auf ewig gegründet hast.
Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
153 Siehe mein Elend an und errette mich; denn ich habe deines Gesetzes nicht vergessen!
Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
154 Führe meine Sache und erlöse mich; erquicke mich durch dein Wort!
Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
155 Das Heil ist fern von den Gottlosen; denn sie fragen nicht nach deinen Satzungen.
Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
156 Deine Barmherzigkeit ist groß, o HERR; erquicke mich nach deinen Verordnungen!
Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
157 Meiner Verfolger und Widersacher sind viele; dennoch habe ich mich nicht von deinen Zeugnissen abgewandt.
Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
158 Wenn ich die Abtrünnigen ansehe, so ekelt mir, weil sie dein Wort nicht beachten.
Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
159 Siehe, ich liebe deine Befehle; o HERR, erquicke mich nach deiner Gnade!
Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
160 Die Summe deines Wortes ist Wahrheit, und alle Verordnungen deiner Gerechtigkeit bleiben ewig.
Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
161 Fürsten verfolgen mich ohne Ursache; aber vor deinem Wort fürchtet sich mein Herz.
Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
162 Ich freue mich über dein Wort wie einer, der große Beute findet.
Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
163 Ich hasse Lügen und habe Greuel daran; aber dein Gesetz habe ich lieb.
Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
164 Ich lobe dich des Tages siebenmal wegen der Ordnungen deiner Gerechtigkeit.
Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
165 Großen Frieden haben, die dein Gesetz lieben, und nichts bringt sie zu Fall.
Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
166 Ich warte auf dein Heil, o HERR, und erfülle deine Befehle.
Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
167 Meine Seele bewahrt deine Zeugnisse und liebt sie sehr.
Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
168 Ich habe deine Befehle und deine Zeugnisse bewahrt; denn alle meine Wege sind vor dir.
Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
169 HERR, laß mein Schreien vor dich kommen; unterweise mich nach deinem Wort!
Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
170 Laß mein Flehen vor dich kommen; errette mich nach deiner Verheißung!
Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
171 Meine Lippen sollen überfließen von Lob, wenn du mich deine Satzungen lehrst.
Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
172 Meine Zunge soll deine Rede singen; denn alle deine Gebote sind gerecht.
Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
173 Deine Hand komme mir zu Hilfe; denn ich habe deine Befehle erwählt.
Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
174 Ich habe Verlangen nach deinem Heil, o HERR, und dein Gesetz ist meine Lust.
Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
175 Meine Seele soll leben und dich loben, und deine Verordnungen seien meine Hilfe!
Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
176 Ich bin verirrt wie ein verlorenes Schaf; suche deinen Knecht! Denn deine Gebote habe ich nicht vergessen!
Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.

< Psalm 119 >