< Psalm 106 >

1 Hallelujah! Danket dem HERRN, denn er ist gütig, seine Gnade währt ewiglich!
Tamandani Yehova. Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
2 Wer kann die Machttaten des HERRN beschreiben und allen seinen Ruhm verkünden?
Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova kapena kumutamanda mokwanira?
3 Wohl denen, die das Recht beachten, die Gerechtigkeit üben allezeit!
Odala ndi amene amasunga chilungamo, amene amachita zolungama nthawi zonse.
4 Gedenke meiner, o HERR, aus Gnaden gegen dein Volk, suche mich heim mit deinem Heil,
Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu, bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo,
5 daß ich einen Einblick bekomme in das Wohlergehen deiner Auserwählten, mich freue an der Freude deines Volkes und mich deines Erbteils rühme.
kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika, kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani.
6 Wir haben gesündigt samt unsern Vätern, wir haben verkehrt gehandelt, wir haben gefrevelt.
Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu; tachita zolakwa ndipo tachita moyipa.
7 Unsre Väter in Ägypten hatten nicht acht auf deine Wunder, sie gedachten nicht an die Größe deiner Güte und waren widerspenstig am Meer, am Schilfmeer.
Pamene makolo athu anali mu Igupto, sanalingalire za zozizwitsa zanu; iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka, ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira.
8 Aber er half ihnen um seines Namens willen, um seine Stärke kundzutun.
Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake, kuti aonetse mphamvu zake zazikulu.
9 Und er bedrohte das Schilfmeer, daß es vertrocknete, und ließ sie durch die Tiefen gehen wie auf einer Steppe.
Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma; anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu.
10 Und er rettete sie von der Hand des Hassers und erlöste sie aus der Hand des Feindes.
Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo; anawawombola mʼdzanja la mdani.
11 Und das Wasser bedeckte ihre Bedränger, nicht einer von ihnen blieb übrig.
Madzi anamiza adani awo, palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.
12 Da glaubten sie seinen Worten und sangen sein Lob.
Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake ndi kuyimba nyimbo zamatamando.
13 Aber sie vergaßen seine Werke bald, sie warteten nicht auf seinen Rat,
Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita, ndipo sanayembekezere uphungu wake.
14 sondern ließen sich gelüsten in der Wüste und versuchten Gott in der Einöde.
Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo; mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu.
15 Und er gab ihnen, was sie forderten, sandte aber eine Seuche unter sie.
Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha, koma anatumiza nthenda yowondetsa.
16 Und sie wurden eifersüchtig auf Mose im Lager, auf Aaron, den Heiligen des HERRN.
Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni, amene Yehova anadzipatulira.
17 Da tat sich die Erde auf und verschlang Datan und bedeckte die Rotte Abirams;
Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani; inakwirira gulu la Abiramu.
18 und Feuer verzehrte ihre Rotte, die Flamme versengte die Gottlosen.
Moto unayaka pakati pa otsatira awo; lawi lamoto linapsereza anthu oyipa.
19 Sie machten ein Kalb am Horeb und warfen sich nieder vor dem gegossenen Bild.
Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo.
20 Sie vertauschten ihre Herrlichkeit gegen das Abbild eines Stiers, der Gras frißt.
Anasinthanitsa ulemerero wawo ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu.
21 Sie vergaßen Gottes, ihres Retters, der große Dinge in Ägypten getan,
Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa, amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto,
22 Wunder im Lande Hams, Furchtbares am Schilfmeer.
zozizwitsa mʼdziko la Hamu ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira.
23 Und er gedachte sie zu vertilgen, wenn nicht Mose, sein Auserwählter, in den Riß getreten wäre vor seinem Angesicht, um seinen Grimm abzuwenden, daß er sie nicht vertilgte.
Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga, pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa, kuyima pamaso pake, ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge.
24 Sie verachteten das liebliche Land, sie glaubten seinem Worte nicht.
Motero iwo ananyoza dziko lokoma; sanakhulupirire malonjezo ake.
25 Und sie murrten in ihren Zelten, sie gehorchten nicht der Stimme des HERRN.
Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo ndipo sanamvere Yehova.
26 Da erhob er seine Hand [und schwur], sie niederzustrecken in der Wüste
Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake, kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu,
27 und ihren Samen unter die Nationen zu werfen und sie zu zerstreuen in die Länder.
kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse.
28 Und sie hängten sich an den Baal-Peor und aßen Opfer der toten [Götzen],
Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo;
29 und sie erzürnten ihn mit ihrem Tun; da brach die Plage unter ihnen aus.
anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa, ndipo mliri unabuka pakati pawo.
30 Aber Pinehas trat auf und übte Gericht, so daß die Plage aufgehalten ward.
Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo, ndipo mliri unaleka.
31 Das wurde ihm zur Gerechtigkeit gerechnet auf alle Geschlechter, in Ewigkeit.
Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake, kwa mibado yosatha imene ikubwera.
32 Und sie erzürnten ihn am Haderwasser, und es erging Mose übel um ihretwillen.
Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo,
33 Denn sie betrübten seinen Geist, und er redete unbedacht mit seinen Lippen.
pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu, ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera.
34 Sie vertilgten die Völker nicht, von denen der HERR ihnen gesagt hatte;
Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu monga momwe Yehova anawalamulira.
35 sondern ließen sich ein mit den Heiden und lernten ihre Weise.
Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo ndi kuphunzira miyambo yawo.
36 Und sie dienten ihren Götzen, und diese wurden ihnen zum Fallstrick.
Ndipo anapembedza mafano awo, amene anakhala msampha kwa iwowo.
37 Und sie opferten ihre Söhne und ihre Töchter den bösen Geistern.
Anapereka nsembe ana awo aamuna ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.
38 Und sie vergossen unschuldiges Blut, das Blut ihrer Söhne und ihrer Töchter, welche sie den Götzen Kanaans opferten, und so wurde das Land durch Blutschulden entweiht.
Anakhetsa magazi a anthu osalakwa, magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi, amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani, ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo.
39 Und sie befleckten sich mit ihren Werken und hurten mit ihrem Tun.
Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita; ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo.
40 Da entbrannte der Zorn des HERRN wider sein Volk, und er faßte einen Abscheu gegen sein Erbe.
Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.
41 Und er gab sie in die Hand der Nationen, daß ihre Hasser über sie herrschten.
Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina, ndipo adani awo anawalamulira.
42 Und ihre Feinde bedrückten sie, und sie wurden gedemütigt unter ihre Hand.
Adani awo anawazunza ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.
43 Er errettete sie oftmals; aber sie widerstrebten ihm mit ihren Anschlägen und kamen herunter durch eigene Schuld.
Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri, koma iwo ankatsimikiza za kuwukira ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.
44 Aber er sah ihre Not an, als er ihr Schreien hörte,
Koma Iye anaona kuzunzika kwawo pamene anamva kulira kwawo;
45 und gedachte seines Bundes mit ihnen und empfand Mitleid nach seiner großen Huld
Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.
46 und ließ sie Erbarmen finden bei denen, die sie gefangen hielten.
Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo awamvere chisoni.
47 Hilf uns, HERR, unser Gott, sammle uns aus den Heiden, daß wir deinem heiligen Namen danken und uns glücklich preisen, zu deinem Ruhm!
Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu, ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera ndi kunyadira mʼmatamando anu.
48 Gelobt sei der HERR, der Gott Israels, von Ewigkeit zu Ewigkeit, und alles Volk soll sagen: Amen! Hallelujah!
Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, Kuyambira muyaya mpaka muyaya. Anthu onse anene kuti, “Ameni!” Tamandani Yehova.

< Psalm 106 >