< Sprueche 4 >

1 Gehorchet, ihr Söhne, der väterlichen Zucht und merket auf, damit ihr zu unterscheiden wisset!
Ananu, mverani malangizo a abambo anu; tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
2 Denn ich habe euch eine gute Lehre gegeben; verlasset meine Gebote nicht!
Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino. Choncho musasiye malangizo anga.
3 Denn da ich noch als Sohn bei meinem Vater war, als zartes und einziges Kind unter den Augen meiner Mutter,
Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga; mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
4 da lehrte er mich und sprach zu mir: Dein Herz halte meine Worte fest; bewahre meine Gebote, so wirst du leben!
Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti, “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako, usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
5 Erwirb Weisheit, erwirb Verstand; vergiß die Reden meines Mundes nicht und weiche nicht davon ab!
Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu; usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
6 Verlaß du sie nicht, so wird sie dich bewahren; liebe du sie, so wird sie dich behüten!
Usasiye nzeru ndipo idzakusunga. Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
7 Der Weisheit Anfang ist: Erwirb Weisheit und um allen deinen Erwerb erwirb Verstand!
Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru. Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
8 Halte sie hoch, so wird sie dich erhöhen; sie wird dich ehren, wenn du sie liebst.
Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza; ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
9 Sie wird deinem Haupt einen lieblichen Kranz verleihen, eine prächtige Krone wird sie dir reichen.
Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako; idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”
10 Höre, mein Sohn, nimm meine Lehren an, sie werden dir das Leben verlängern!
Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena, ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
11 Ich will dich den Weg der Weisheit lehren, dich leiten auf gerader Bahn.
Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
12 Gehst du, so wird dein Schritt nicht gehemmt, und wenn du läufst, so wirst du nicht straucheln.
Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana; ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
13 Halte unablässig fest an der Zucht, bewahre sie; denn sie ist dein Leben.
Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi. Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
14 Begib dich nicht auf den Pfad der Gottlosen und tue keinen Schritt auf dem Wege der Bösen!
Usayende mʼnjira za anthu oyipa kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
15 Meide ihn, überschreite ihn nicht einmal, weiche davon und gehe vorüber!
Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo; uzilambalala nʼkumangopita.
16 Denn sie schlafen nicht, sie haben denn Böses getan; der Schlummer flieht sie, wenn sie niemand zu Fall gebracht haben.
Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa; tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
17 Denn sie essen erfreveltes Brot und trinken erpreßten Wein.
Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
18 Aber des Gerechten Pfad ist wie des Lichtes Glanz, das immer heller leuchtet bis zum vollen Tag.
Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
19 Der Gottlosen Weg ist dichte Finsternis; sie wissen nicht, worüber sie straucheln.
Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani; iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
20 Mein Sohn, merke auf meine Worte, neige dein Ohr zu meinen Reden!
Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena; tchera khutu ku mawu anga.
21 Laß sie nie von deinen Augen weichen, bewahre sie im innersten Herzen!
Usayiwale malangizo angawa, koma uwasunge mu mtima mwako.
22 Denn sie sind das Leben denen, die sie finden, und heilsam ihrem ganzen Leib.
Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
23 Mehr als alles andere behüte dein Herz; denn von ihm geht das Leben aus.
Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu pakuti ndiwo magwero a moyo.
24 Enthalte dich falscher Worte, und verdrehte Reden seien fern von dir!
Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota; ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
25 Laß deine Augen geradeaus schauen und deine Augenlider stracks vor dich blicken.
Maso ako ayangʼane patsogolo; uziyangʼana kutsogolo molunjika.
26 Erwäge wohl deine Schritte, und alle deine Wege seien bestimmt;
Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
27 weiche weder zur Rechten noch zur Linken, halte deinen Fuß vom Bösen fern!
Usapatukire kumanja kapena kumanzere; usapite kumene kuli zoyipa.

< Sprueche 4 >