< 4 Mose 33 >
1 Dies sind die Reisen der Kinder Israel, die unter Mose und Aaron nach ihren Heerscharen aus Ägypten gezogen sind.
Malo otsatirawa ndi omwe Aisraeli anayima pa maulendo awo atatuluka mʼdziko la Igupto mʼmagulu awo motsogozedwa ndi Mose ndi Aaroni.
2 Und Mose beschrieb ihren Auszug und ihre Tagereisen auf Befehl des HERRN. Folgendes sind ihre Reisen nach ihrem Auszug:
Mose analemba malo amene anayambira maulendo awo molamulidwa ndi Yehova. Maulendo awo ndi malo omwe anayambira ndi awa:
3 Sie brachen auf von Raemses im ersten Monat, am fünfzehnten Tage des ersten Monats; am Tage nach dem Passah zogen die Kinder Israel aus durch höhere Hand, vor den Augen aller Ägypter,
Aisraeli ananyamuka kuchokera ku Ramesesi pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, itangotha Paska. Iwo anatuluka nayenda molimba mtima Aigupto onse akuona,
4 während die Ägypter alle Erstgeburt begruben, welche der HERR unter ihnen geschlagen hatte; auch hatte der HERR an ihren Göttern Gerichte geübt.
pamene ankayika maliro a ana awo oyamba kubadwa, omwe Yehova anawakantha pakati pawo chifukwa Yehova anaweruza milungu yawo.
5 Und die Kinder Israel brachen auf von Raemses und lagerten sich in Sukkot.
Aisraeli atachoka ku Ramesesi, anamanga misasa yawo ku Sukoti.
6 Und sie brachen auf von Sukkot und lagerten sich in Etam, welches am Rand der Wüste liegt.
Atachoka ku Sukoti anakamanga misasa yawo ku Etamu, mʼmbali mwa chipululu.
7 Von Etam brachen sie auf und wandten sich gegen Pi-Hahirot, welches vor Baal-Zephon liegt, und lagerten sich vor Migdol.
Ndipo atachoka ku Etamu, anabwerera ku Pihahiroti, kummawa kwa Baala-Zefoni, ndipo anamanga misasa yawo pafupi ndi Migidoli.
8 Von Pi-Hahirot brachen sie auf und gingen mitten durch das Meer in die Wüste, und reisten drei Tagesreisen weit in die Wüste Etam und lagerten sich bei Mara.
Atachoka ku Pihahiroti anadutsa mʼkati mwa nyanja kupita ku chipululu ndipo atayenda masiku atatu mʼchipululu cha Etamu, anamanga misasa yawo ku Mara.
9 Von Mara brachen sie auf und kamen gen Elim, wo zwölf Wasserbrunnen und siebzig Palmen waren, und lagerten sich daselbst.
Atachoka ku Mara anafika ku Elimu, kumene kunali akasupe a madzi khumi ndi awiri ndi mitengo ya migwalangwa 70 ndipo anamanga misasa yawo kumeneko.
10 Von Elim brachen sie auf und lagerten sich an das Schilfmeer.
Atachoka ku Elimu anakamanga misasa yawo mʼmbali mwa Nyanja Yofiira.
11 Vom Schilfmeer brachen sie auf und lagerten sich in der Wüste Sin.
Atachoka ku Nyanja Yofiira anakamanga misasa yawo mʼchipululu cha Sini.
12 Von der Wüste Sin brachen sie auf und lagerten sich in Dophka.
Atachoka ku chipululu cha Sini anakamanga ku Dofika.
13 Von Dophka brachen sie auf und lagerten sich in Alus.
Atachoka ku Dofika anakamanga misasa yawo ku Alusi.
14 Von Alus brachen sie auf und lagerten sich in Raphidim; daselbst hatte das Volk kein Wasser zu trinken.
Atachoka ku Alusi anakamanga misasa yawo ku Refidimu, kumene kunalibe madzi woti anthu ndi kumwa.
15 Von Raphidim brachen sie auf und lagerten sich in der Wüste Sinai.
Atachoka ku Refidimu anakamanga ku chipululu cha Sinai
16 Von der Wüste Sinai brachen sie auf und lagerten sich bei den Lustgräbern.
Atachoka ku chipululu cha Sinai anakamanga misasa yawo ku Kiburoti-Hataava.
17 Von den Lustgräbern brachen sie auf und lagerten sich in Hazerot.
Atachoka ku Kiburoti-Hataava anakamanga misasa yawo ku Heziroti.
18 Von Hazerot brachen sie auf und lagerten sich in Ritma.
Atachoka ku Heziroti anakamanga ku Ritima.
19 Von Ritma brachen sie auf und lagerten sich in Rimmon-Parez.
Atachoka ku Ritima anakamanga ku Rimoni-Perezi.
20 Von Rimmon-Parez brachen sie auf und lagerten sich in Libna.
Atachoka ku Rimoni-Perezi anakamanga ku Libina.
21 Von Libna brachen sie auf und lagerten sich in Rissa.
Atachoka ku Libina anakamanga ku Risa.
22 Von Rissa brachen sie auf und lagerten sich in Kehelata.
Atachoka ku Risa anakamanga ku Kehelata.
23 Von Kehelata brachen sie auf und lagerten sich am Berge Sapher.
Atachoka ku Kehelata anakamanga ku phiri la Seferi.
24 Vom Berge Sapher brachen sie auf und lagerten sich in Harada.
Atachoka ku phiri la Seferi anakamanga ku Harada.
25 Von Harada brachen sie auf und lagerten sich in Makhelot.
Atachoka ku Harada anakamanga ku Mekheloti.
26 Von Makhelot brachen sie auf und lagerten sich in Tahat.
Atachoka ku Mekheloti anakamanga ku Tahati.
27 Von Tahat brachen sie auf und lagerten sich in Tarach.
Atachoka ku Tahati anakamanga ku Tera.
28 Von Tarach brachen sie auf und lagerten sich in Mitka.
Atachoka ku Tera anakamanga ku Mitika.
29 Von Mitka brachen sie auf und lagerten sich in Hasmona.
Atachoka ku Mitika anakamanga ku Hasimona.
30 Von Hasmona brachen sie auf und lagerten sich in Moserot.
Atachoka ku Hasimona anakamanga ku Moseroti.
31 Von Moserot brachen sie auf und lagerten sich in Bnejaakan.
Atachoka ku Moseroti anakamanga ku Beni Yaakani.
32 Von Bnejaakan brachen sie auf und lagerten sich in Hor-Hagidgad.
Atachoka ku Beni Yaakani anakamanga ku Hori-Hagidigadi.
33 Von Hor-Hagidgad brachen sie auf und lagerten sich in Jothbata.
Atachoka ku Hori-Hagidigadi anakamanga ku Yotibata.
34 Von Jothbata brachen sie auf und lagerten sich in Abrona.
Atachoka ku Yotibata anakamanga ku Abirona.
35 Von Abrona brachen sie auf und lagerten sich in Ezjon-Geber.
Atachoka ku Abirona anakamanga ku Ezioni-Geberi.
36 Von Ezjon-Geber brachen sie auf und lagerten sich in der Wüste Zin, das ist in Kadesch.
Atachoka ku Ezioni-Geberi anakamanga ku Kadesi, mʼchipululu cha Zini chimene ndi Kadesi.
37 Von Kadesch brachen sie auf und lagerten sich am Berge Hor, an der Grenze des Landes Edom.
Anachoka ku Kadesi ndi kukamanga ku phiri la Hori, mʼmalire mwa dziko la Edomu.
38 Da ging Aaron, der Priester, auf den Berg Hor, nach dem Befehl des HERRN, und starb daselbst im vierzigsten Jahre des Auszugs der Kinder Israel aus Ägyptenland, am ersten Tage des fünften Monats.
Molamulidwa ndi Yehova, wansembe Aaroni anakwera ku phiri la Hori kumene anakamwalirira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu, mʼchaka cha makumi anayi, Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.
39 Und Aaron war hundertdreiundzwanzig Jahre alt, als er starb auf dem Berge Hor.
Aaroni anamwalira pa phiri la Hori ali ndi zaka 123.
40 Da hörte der Kanaaniter, der König zu Arad, welcher gegen Mittag des Landes Kanaan wohnte, daß die Kinder Israel kämen.
Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi yomwe inkakhala ku Negevi kummwera kwa Kanaani, inamva kuti Aisraeli akubwera.
41 Und sie brachen auf von dem Berge Hor und lagerten sich in Zalmona.
Atachoka ku phiri la Hori anakamanga ku Zalimoni.
42 Von Zalmona brachen sie auf und lagerten sich in Punon.
Atachoka ku Zalimoni anakamanga ku Punoni.
43 Von Punon brachen sie auf und lagerten sich in Obot.
Atachoka ku Punoni anakamanga ku Oboti.
44 Von Obot brachen sie auf und lagerten sich in Jje-Abarim, an der Grenze von Moab.
Atachoka ku Oboti anakamanga ku Iye-Abarimu.
45 Von Jje-Abarim brachen sie auf und lagerten sich in Dibon-Gad.
Atachoka ku Iye-Abarimu anakamanga ku Diboni Gadi.
46 Von Dibon-Gad brachen sie auf und lagerten sich in Almon-Diblataim.
Atachoka ku Diboni Gadi anakamanga ku Alimoni-Dibulataimu.
47 Von Almon-Diblataim brachen sie auf und lagerten sich am Gebirge Abarim, vor dem Nebo.
Atachoka ku Alimoni-Dibulataimu anakamanga mʼmapiri a Abarimu, pafupi ndi Nebo.
48 Vom Gebirge Abarim brachen sie auf und lagerten sich in der Ebene der Moabiter am Jordan, gegenüber Jericho.
Atachoka ku mapiri a Abarimu anakamanga ku zigwa za Mowabu mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi Yeriko.
49 Sie lagerten sich aber am Jordan, von Beth-Jesimot bis nach Abel-Sittim, in der Ebene der Moabiter.
Ali ku zigwa za Mowabu anamanga mʼmbali mwa Yorodani kuchokera ku Beti-Yesimoti mpaka ku Abeli-Sitimu.
50 Und der HERR redete zu Mose in der Ebene der Moabiter am Jordan, Jericho gegenüber, und sprach:
Pa zigwa za Mowabu, mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi ku Yeriko, Yehova anawuza Mose kuti,
51 Rede mit den Kindern Israel und sprich zu ihnen: Wenn ihr über den Jordan in das Land Kanaan gegangen seid,
“Nena kwa Aisraeli kuti, ‘Pamene muwoloka Yorodani kulowa mʼdziko la Kanaani,
52 so sollt ihr alle Einwohner des Landes vor eurem Angesicht vertreiben und alle ihre Bildsäulen zerstören; auch alle ihre gegossenen Bilder sollt ihr zerbrechen und alle ihre Höhen verwüsten;
mukathamangitse nzika zonse za mʼdzikomo pamaso panu. Mukawononge mafano awo onse a miyala ndi osula ndi malo awo achipembedzo.
53 also sollt ihr das Land in Besitz nehmen und darin wohnen; denn euch habe ich das Land gegeben, daß ihr es besitzet.
Mukalande dzikolo ndi kukhalamo chifukwa ndakupatsani dziko limenelo kuti mukhalemo.
54 Und ihr sollt das Land durchs Los als Erbe unter eure Geschlechter teilen. Den Zahlreichen sollt ihr ein größeres Erbteil geben, den Kleinen ein kleineres; wohin einem jeden das Los fällt, das soll er besitzen; nach den Stämmen eurer Väter sollt ihr erben.
Mukagawane dzikolo pochita maere monga mwa mafuko anu. Kwa omwe ali ambiri, cholowa chambiri, ndipo amene ali ocheperapo, chocheperanso. Chilichonse chimene chidzawagwere iwo mwa maere chidzakhala chawo. Mukaligawane monga mwa mafuko a makolo anu.
55 Werdet ihr aber die Einwohner des Landes nicht vor eurem Angesicht vertreiben, so sollen euch die, welche ihr übrigbleiben lasset, zu Dornen werden in euren Augen und zu Stacheln in euren Seiten, und sie sollen euch befehden in dem Lande, darin ihr wohnet.
“‘Koma ngati simukathamangitsa nzika zimene zili mʼdzikomo, amene mukawalole kukhalamo adzakhala ngati zisonga mʼmaso mwanu ndi ngati minga mʼmbali mwanu. Adzakubweretserani mavuto mʼdziko limene mudzakhalemolo.
56 So wird es dann geschehen, daß ich euch tun werde, was ich ihnen zu tun gedachte.
Ndipo pamenepo ndidzachitira inu zomwe ndinaganiza kuwachitira iwowo.’”