< Nehemia 7 >
1 Als nun die Mauern gebaut waren, setzte ich die Türflügel ein; und es wurden die Torhüter, Sänger und Leviten bestellt.
Khoma linamangidwa ndipo zitseko zinayikidwa. Pambuyo pake alonda a Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo ndiponso Alevi anasankhidwa.
2 Und ich gab meinem Bruder Hanani und Hananja, dem Obersten der Burg, den Oberbefehl über Jerusalem; denn er war ein zuverlässiger Mann und gottesfürchtig vor vielen [andern].
Kenaka ine ndinasankha mʼbale wanga Hanani pamodzi ndi Hananiya woyangʼanira nsanja yankhondo kukhala olamulira Yerusalemu chifukwa iyeyu anali munthu odalirika ndi woopa Mulungu kuposa anthu ena.
3 Und ich sprach zu ihnen: Man soll die Tore Jerusalems nicht öffnen, ehe die Sonne heiß scheint; und während sie noch [Wache] stehen, soll man die Türen schließen und verriegeln! Und bestellet Wachen aus den Bürgern Jerusalems, einen jeden auf seinen Posten, und zwar jeden gegenüber seinem Hause!
Ine ndinawawuza kuti, “Musalole kuti zipata za Yerusalemu zitsekulidwe mpaka dzuwa litatentha, ndipo alonda asanaweruke aonetsetse kuti atseka zitseko ndi kuzipiringidza. Musankhe alonda pakati pa anthu okhala mu Yerusalemu, ena akhale pa malo pawo ndi ena akhale moyangʼanana ndi nyumba zawo.”
4 Nun war die Stadt weit und groß, das Volk darin aber spärlich, und die Häuser waren noch nicht aufgebaut.
Tsono mzinda wa Yerusalemu unali wotambasuka ndiponso waukulu koma munali anthu ochepa ndipo nyumba zinali zisanamangidwe.
5 Da gab mir mein Gott ins Herz, die Vornehmsten und die Vorsteher und das Volk zu versammeln, um sie nach ihren Geschlechtern aufzuzeichnen; und ich fand ein Geschlechtsregister derer, die zuerst heraufgezogen waren, und fand darin geschrieben:
Ndipo Mulungu wanga anayika mu mtima mwanga maganizo oti ndisonkhanitse anthu olemekezeka, akuluakulu ndi anthu onse kuti alembetse mayina mwa mabanja awo. Ndinapeza buku limene munalembedwa mayina a mabanja a iwo amene anayamba kubwera kuchokera ku ukapolo. Izi ndi zimene ndinazipeza zitalembedwa mʼmenemo:
6 Folgendes sind die Landeskinder, die aus der Gefangenschaft heraufgekommen sind, welche Nebukadnezar, der König von Babel, hinweggeführt hatte, und die wieder nach Jerusalem und Juda gekommen sind, ein jeder in seine Stadt;
Awa ndi anthu a mʼchigawo cha Yuda amene anabwerera kuchokera ku ukapolo amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawatenga ukapolo. Iwo anabwerera ku Yerusalemu ndi ku Yuda, aliyense ku mzinda wa makolo ake.
7 die gekommen sind mit Serubbabel, Jesua, Nehemia, Asarja, Raamja, Nahemani, Mordechai, Bilsan, Misperet, Bigvai, Nehum und Baana. Dies ist die Zahl der Männer vom Volke Israel:
Anabwera pamodzi ndi atsogoleri awa: Zerubabeli, Yesuwa, Nehemiya, Azariya, Raamiya, Nahamani, Mordekai, Bilisani, Misipereti, Bigivai, Nehumu ndi Baana. Tsono chiwerengero cha anthu a ku Israeli chinali chotere:
8 Der Kinder Parhos waren 2172;
Zidzukulu za Parosi 2,172
9 der Kinder Sephatjas: 372; (der Kinder Arachs: 652);
Zidzukulu za Sefatiya 372
10 der Kinder Pachat-Moabs,
Zidzukulu za Ara 652
11 von den Kindern Jesuas und Joabs: 2818;
Zidzukulu za Pahati-Mowabu (kudzera mu mʼbado wa Yesuwa ndi Yowabu) 2,818
12 der Kinder Elams: 1254;
Zidzukulu za Elamu 1,254
13 der Kinder Sattus: 854;
Zidzukulu za Zatu 845
14 der Kinder Sakkais: 760;
Zidzukulu za Zakai 760
15 der Kinder Binnuis: 648;
Zidzukulu za Binuyi 648
16 der Kinder Bebais: 628;
Zidzukulu za Bebai 628
17 der Kinder Asgads: 2322;
Zidzukulu za Azigadi 2,322
18 der Kinder Adonikams: 667;
Zidzukulu za Adonikamu 667
19 der Kinder Bigvais: 2067;
Zidzukulu za Abigivai 2,067
20 der Kinder Adins: 655; (der Kinder Aters, von Hiskia: 98);
Zidzukulu za Adini 655
21 der Kinder Hasums: 328;
Zidzukulu za Ateri (kudzera mwa Hezekiya) 98
22 der Kinder Bezais: 324;
Zidzukulu za Hasumu 328
23 der Kinder Hariphs: 112;
Zidzukulu za Bezayi 324
24 der Kinder Gibeons: 95;
Zidzukulu za Harifu 112
25 der Männer von Bethlehem und Netopha: 188;
Zidzukulu za Gibiyoni 95.
26 der Männer von Anatot: 128;
Anthu a ku Betelehemu ndi Netofa 188
27 der Männer von Beth-Asmavet: 42;
Anthu a ku Anatoti 128
28 der Männer von Kirjat-Jearim,
Anthu a ku Beti-Azimaveti 42
29 Kephira und Beerot: 743;
Anthu a ku Kiriati Yeyarimu Kefira ndi Beeroti 743
30 der Männer von Rama und Gaba: 621;
Anthu a ku Rama ndi Geba 621
31 der Männer von Michmas: 122;
Anthu a ku Mikimasi 122
32 der Männer von Bethel und Ai: 123;
Anthu a ku Beteli ndi Ai 123
33 der Männer des andern Nebo: 52;
Anthu a ku Nebo winayo 52
34 der Kinder des andern Elam: 1254;
Ana a Elamu wina 1,254
35 der Kinder Harims: 320;
Zidzukulu za Harimu 320
36 der Kinder Jerichos: 345;
Zidzukulu za Yeriko 345
37 der Kinder Lods, Hadids und Onos: 721;
Zidzukulu za Lodi, Hadidi ndi Ono 721
38 der Kinder Senaas: 3930.
Zidzukulu za Senaya 3,930.
39 Von den Priestern: der Kinder Jedajas, vom Hause Jesuas, waren 973;
Ansembe anali awa: A banja la Yedaya (ndiye kuti zidzukulu za Yesuwa) 973
40 der Kinder Immers: 1052;
Zidzukulu za Imeri 1,052
41 der Kinder Pashurs: 1247;
Zidzukulu za Pasi-Huri 1,247
42 der Kinder Harims: 1017.
Zidzukulu za Harimu 1,017.
43 Von den Leviten: der Kinder Jesuas von Kadmiel unter den Kindern Hodevas waren 74;
Alevi anali awa: A banja la Yesuwa ndi Kadimieli, ndiye kuti zidzukulu za Hodaviya 74.
44 von den Sängern: der Kinder Asaphs waren 148.
Anthu oyimba: Zidzukulu za Asafu 148.
45 Von den Torhütern: der Kinder Sallums, der Kinder Athers, der Kinder Talmons, der Kinder Akkubs, der Kinder Hatitas, der Kinder Sobais waren 138.
Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Salumu, Ateri, Talimoni, Hatita ndi Sobai 138.
46 Von den Tempeldienern: der Kinder Zihas, der Kinder Hasuphas, der Kinder Tabbaots,
Anthu ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Ziha, zidzukulu za Hasufa, zidzukulu za Tabaoti,
47 der Kinder Keros, der Kinder Sias, der Kinder Padons,
Zidzukulu Kerosi, zidzukulu za Siya, zidzukulu za Padoni
48 der Kinder Lebanas, der Kinder Hagabas, der Kinder Salmais,
Zidzukulu za Lebana za Hagaba, ndi za Salimayi,
49 der Kinder Hanans, der Kinder Giddels,
Zidzukulu za Hanani, zidzukulu za Gideli, zidzukulu za Gahari,
50 der Kinder Gahars, der Kinder Reajas, der Kinder Rezins, der Kinder Nekodas,
Zidzukulu za Reyaya, zidzukulu za Rezini, zidzukulu za Nehoda,
51 der Kinder Gasams, der Kinder der Ussas,
Zidzukulu za Gazamu, zidzukulu za Uza, zidzukulu za Paseya,
52 der Kinder Paseachs, der Kinder Besais, der Kinder Meunim, der Kinder Nephisesim,
Zidzukulu za Besai, zidzukulu za Meunimu, zidzukulu za Nefusimu,
53 der Kinder Bakbuks, der Kinder Hakuphas, der Kinder Harhurs,
Zidzukulu za Bakibuku, zidzukulu za Hakufa, zidzukulu za Harihuri,
54 der Kinder Bazlits, der Kinder Mehidas,
Zidzukulu za Baziliti, zidzukulu za Mehida, zidzukulu za Harisa,
55 der Kinder Harsas, der Kinder Barkos, der Kinder Siseras, der Kinder Temas,
Zidzukulu za Barikosi, zidzukulu za Sisera, zidzukulu za Tema
56 der Kinder Neziachs, der Kinder Hatiphas;
Zidzukulu za Neziya, ndi zidzukulu za Hatifa.
57 von den Kindern der Knechte Salomos: der Kinder Sotais, der Kinder Sopherets,
Zidzukulu za antchito a Solomoni: Zidzukulu za Sotai, zidzukulu za Sofereti, zidzukulu za Perida
58 der Kinder Peridas, der Kinder Jaalas, der Kinder Darkons, der Kinder Giddels,
zidzukulu za Yaala, zidzukulu za Darikoni, zidzukulu za Gideli,
59 der Kinder Sephatjas, der Kinder Hattils, der Kinder Pocherets, von Zebajim, der Kinder Ammon,
zidzukulu za Sefatiya, zidzukulu za Hatilu zidzukulu za Pokereti-Hazebaimu ndi zidzukulu Amoni.
60 aller Tempeldiener und Kinder der Knechte Salomos waren 392.
Anthu onse ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi zidzukulu za antchito a Solomoni analipo 392.
61 Und diese zogen auch mit herauf aus Tel-Melach, Tel-Harsa, Kerub, Addon und Ammer, konnten aber das Haus ihrer Väter und ihre Abstammung nicht nachweisen, ob sie aus Israel seien:
Ali munsiwa anachokera ku Teli-Mela, Teri-Harisa, Kerubi, Adoni, ndi Imeri, koma sanathe kunena mwa tchutchutchu kuti makolo awo kapena mafuko awo analidi Aisraeli kapena ayi.
62 Die Kinder Delajas, die Kinder Tobijas, die Kinder Nekodas; derer waren 642.
Zidzukulu za Delaya, zidzukulu za Tobiya ndi zidzukulu za Nekoda 642.
63 Und von den Priestern: die Kinder Hobajas, die Kinder Hakkoz`, die Kinder der Barsillais, der von den Töchtern Barsillais, des Gileaditers, ein Weib genommen hatte und nach deren Namen genannt ward.
Ndiponso ena pakati pa ansembe anali awa: zidzukulu za Hobiya, zidzukulu za Hakozi ndi zidzukulu za Barizilai (munthu amene anakwatira mwana wamkazi wa Barizilai wa ku Giliyadi ndipo amatchedwa dzina limenelo).
64 Diese suchten ihr Geburtsregister, und als sie es nicht fanden, wurden sie von dem Priestertum ausgestoßen.
Iwowa anafufuzafufuza mayina awo mʼbuku la mibado ya mabanja awo ndipo sanapeze mayina awo kotero anachotsedwa pa unsembe nawerengedwa ngati odetsedwa pa chipembedzo.
65 Und der Landpfleger sagte ihnen, daß sie nicht vom Allerheiligsten essen dürften, bis ein Priester mit dem Licht und Recht aufstände.
Choncho bwanamkubwa anawawuza anthuwo kuti asamadye nawo chakudya china chilichonse choperekedwa kwa Mulungu mpaka patapezeka wansembe wodziwa kugwiritsa bwino ntchito ya Urimu ndi Tumimu.
66 Die ganze Gemeinde zählte insgesamt 42360 Seelen,
Chiwerengero chonse cha anthuwa chinali 42,360.
67 ausgenommen ihre Knechte und Mägde; derer waren 7337;
Kuwonjezera pamenepa panali antchito awo aamuna ndi aakazi 7,337 ndiponso anthu aamuna ndi aakazi oyimba nyimbo okwanira 245.
68 und sie hatten 245 Sänger und Sängerinnen
Panali akavalo 736, abulu angʼonoangʼono 245.
69 und 736 Pferde und 245 Maultiere und 435 Kamele und 6720 Esel.
Ngamira zawo zinalipo 435 ndipo abulu analipo 6,720.
70 Und sämtliche Familienhäupter gaben Beiträge zum Werk. Der Landpfleger gab für den Schatz 1000 Dareiken, 50 Sprengschalen, 530 Priesterröcke,
Atsogoleri ena a mabanja anapereka mphatso zothandizira ntchito. Bwanamkubwa anapereka ku thumba losungira chuma, ndalama zagolide za makilogalamu asanu ndi atatu, mabeseni makumi asanu ndi zovala za ansembe 530.
71 und von den Familien ward beigesteuert an den Schatz für das Werk an Gold 20000 Dareiken, und an Silber 2000 Minen.
Atsogoleri ena amabanja anapereka ku thumba losungira chuma ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndiponso ndalama za siliva zokwana makilogalamu 1,250.
72 Und das übrige Volk gab an Gold 20000 Dareiken und an Silber 2000 Minen und 67 Priesterröcke.
Anthu ena onse otsala anapereka ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndalama za siliva zokwana makilogalamu 140, ndiponso zovala za ansembe 67.
73 Und die Priester und Leviten, die Torhüter, Sänger und ein Teil des Volkes und die Tempeldiener und alle Israeliten ließen sich in ihren Städten nieder. Und als der siebente Monat nahte, waren die Kinder Israel in ihren Städten.
Choncho ansembe, Alevi, alonda a Nyumba ya Mulungu, anthu oyimba nyimbo, ena mwa anthu wamba, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi Aisraeli ena onse ankakhala mʼmizinda yawo. Pofika mwezi wachisanu ndi chiwiri Aisraeli onse anali atakhazikika mʼmizinda yawo.