< Job 5 >

1 Rufe doch! Ist einer, der dir antwortet? Und an welchen von den Heiligen willst du dich wenden?
“Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe? Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?
2 Denn den Toren erwürgt der Zorn, und den Einfältigen tötet der Eifer.
Mkwiyo umapha chitsiru, ndipo njiru imawononga wopusa.
3 Ich selbst habe einen Toren gesehen, der Wurzel schlug; sobald ich aber sein Gehöft verfluchte,
Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu, koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.
4 waren seine Söhne vom Glück verlassen und wurden unterdrückt im Tore, und niemand rettete sie;
Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe; amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.
5 seine Ernte fraß der Hungrige und nahm sie ihm aus den Dornen heraus, und sein Vermögen schnappten die Habgierigen weg.
Anthu anjala amamudyera zokolola zake, amamutengera ndi za pa minga pomwe, ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.
6 Denn Unglück wächst nicht aus dem Staub hervor, und Unheil sproßt nicht aus der Erde;
Pakuti masautso satuluka mʼfumbi, ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.
7 sondern der Mensch ist zum Unglück geboren, wie die Funken aufwärts fliegen.
Komatu munthu amabadwira kuti azunzike monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.
8 Aber doch würde ich Gott suchen und meine Rede an ihn richten,
“Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu; ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.
9 der große, unerforschliche Dinge tut, Wunder ohne Zahl:
Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.
10 Er gießt Regen auf die Erde und sendet Wasser über die Fluren;
Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi, ndipo amathirira minda ya anthu.
11 er erhöht die Niedrigen und die Leidtragenden erlangen das Heil;
Iye amakweza anthu wamba, ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
12 er vereitelt die Anschläge der Listigen, daß ihre Hand nicht helfen kann;
Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera, kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.
13 er fängt die Weisen in ihrer Klugheit, und der Verschmitzten Rat überstürzt sich selbst;
Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo, ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.
14 bei Tage stoßen sie an wie im Dunkel und tappen zu Mittag wie in der Nacht.
Mdima umawagwera nthawi yamasana; nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.
15 Aber den Armen errettet er vom Schwert und aus ihrem Maul und den Bedürftigen aus der Hand des Starken,
Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo; amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.
16 daß der Geringe Hoffnung faßt und die Frechheit ihr Maul verschließt.
Choncho osauka ali ndi chiyembekezo, ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.
17 Siehe, wohl dem Menschen, den Gott straft! Darum verwirf die Züchtigung des Allmächtigen nicht!
“Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula; nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.
18 Denn er verwundet und verbindet, er zerschlägt und seine Hand heilt.
Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo; Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.
19 In sechs Trübsalen wird er dich erretten, und in sieben wird dich kein Leid berühren:
Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi, mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.
20 In Hungersnot wird er dich vom Tode erlösen und im Kriege von dem Schwert;
Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa, ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.
21 vor der Geißel der Zunge wirst du geborgen sein und wirst Gewalttätigkeit nicht fürchten, wenn sie kommt;
Adzakuteteza kwa anthu osinjirira, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.
22 der Verwüstung und Dürre wirst du lachen und vor den wilden Tieren nicht erschrecken;
Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.
23 denn mit den Steinen des Feldes stehst du im Bunde, und die Tiere des Feldes halten Frieden mit dir.
Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako, ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.
24 Du wirst erfahren, daß dein Zelt sicher ist, und untersuchst du deine Wohnung, so fehlt dir nichts.
Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa; udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.
25 Du wirst erfahren, daß dein Same zahlreich wird und deine Sprößlinge wie das Gras auf Erden.
Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri, ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.
26 Du wirst in gutem Alter begraben werden, wie man Garben einbringt zu ihrer Zeit.
Udzafika ku manda utakalamba, monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.
27 Siehe, das haben wir erforscht, so ist es; vernimm es und merke es dir wohl!
“Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona, choncho uzimvere ndi kuzitsata.”

< Job 5 >