< Jeremia 6 >

1 Fliehet, ihr Kinder Benjamin, aus Jerusalems Mitte, und in Thekoa blaset die Posaune, und über Beth-Kerem richtet ein Zeichen auf; denn ein Unglück droht von Norden her und ein großes Verderben.
“Thawani, inu anthu a ku Benjamini! Tulukani mu Yerusalemu! Lizani lipenga ku Tekowa! Kwezani mbendera ku Beti-Hakeremu! Pakuti tsoka lalikulu likubwera kuchokera kumpoto, ndipo chiwonongekocho nʼchachikulu.
2 Die Liebliche und Verzärtelte, die Tochter Zion will ich zerstören.
Kodi mzinda wa Ziyoni suli ngati msipu wokongola kwambiri, kumene abusa amafikako ndi ziweto zawo?
3 Hirten mit ihren Herden werden zu ihr kommen; ihre Zelte werden sie aufschlagen rings um sie her, und ein jeder wird sein Teil abweiden.
Abusa ndi nkhosa zawo adzabwera kudzalimbana nawo; adzamanga matenti awo mowuzinga, ndipo aliyense adzakhazika anthu ake pamalo pake.”
4 «Heiliget einen Krieg gegen sie! Auf, laßt uns am Mittag hinaufziehen! Wehe uns, der Tag neigt sich, und die Abendschatten dehnen sich!
Adzanena kuti, “Konzekani kuwuthira nkhondo mzindawo! Nyamukani, kuti tiwuthire nkhondo mzindawu masana ano. Koma tili ndi tsoka, dzuwa lapendeka, ndipo zithunzithunzi za kumadzulo zikunka zitalika.
5 Auf, laßt uns bei Nacht hinaufziehen und ihre Paläste zerstören!»
Tsono nyamukani kuti tiwuthire nkhondo mzindawu usiku uno ndi kuwononga malinga ake!”
6 Denn also hat der HERR der Heerscharen befohlen: Fället Bäume und schüttet einen Wall auf gegen Jerusalem! Das ist die Stadt, welche gestraft werden soll; denn lauter Gewalttat ist in ihrer Mitte.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Dulani mitengo ndipo mumange mitumbira yankhondo kulimbana ndi Yerusalemu. Mzinda umenewu uyenera kulangidwa; wadzaza ndi kuponderezana.
7 Wie ein Brunnen sein Wasser quellen läßt, also läßt sie ihre Bosheit quellen; von Gewalttat und Bedrückung hört man in ihr; Leid und Mißhandlung muß ich beständig mitansehen.
Monga momwe chitsime chimatulutsira madzi ndi mmenenso Yerusalemu amatulutsira zoyipa zake. Chiwawa ndi chiwonongeko ndi zomwe zimamveka mu mzindamo; nthenda yake ndi mabala ake ndimaziona nthawi zonse.
8 Laß dich warnen, Jerusalem, damit sich meine Seele nicht ganz von dir entfremde, daß ich dich nicht zur Wüste mache, zu einem unbewohnten Lande!
Iwe Yerusalemu, tengapo phunziro, kuopa kuti chikondi changa pa iwe chingakuchokere ndi kusandutsa dziko lako kukhala bwinja mopanda munthu wokhalamo.”
9 Also spricht der HERR der Heerscharen: Am Überrest Israels wird man Nachlese halten wie am Weinstock. Strecke nochmals wie ein Weinleser deine Hand aus über die Ranken!
Yehova Wamphamvuzonse anandiwuza kuti, “Adani adzawakunkha ndithu anthu otsala a Israeli, monga momwe amachitira populula mphesa. Tsono iwe yesetsa kupulumutsa amene ungathe monga mmene amachitira munthu wokolola mphesa.”
10 Zu wem soll ich reden, wem Zeugnis ablegen, daß sie es hören? Siehe, ihre Ohren sind unbeschnitten, sie können nicht aufmerken. Siehe, das Wort des HERRN ist ihnen zum Hohn geworden; sie haben keine Lust daran.
Kodi ndiyankhule ndi yani ndi kumuchenjeza? Ndinene mawu ochenjeza kwa yani kuti amve? Makutu awo ndi otsekeka kotero kuti sangathe kumva. Mawu a Yehova ndi onyansa kwa iwo; sasangalatsidwa nawo.
11 Und ich bin des Grimmes des HERRN so voll, daß ich ihn kaum zurückhalten kann. Gieße ihn aus über die Kinder auf der Gasse und über den Kreis der Jünglinge allzumal! Ja, Mann und Weib sollen gefangen werden, Alte und Wohlbetagte.
Koma ine ndadzazidwa ndi mkwiyo wa Yehova, ndipo ndatopa ndi kusunga mkwiyo wa Yehova. Yehova anandiwuza kuti, “Tsono ndidzawutulutsira mkwiyo umenewu pa ana oyenda mʼmisewu ndi pa achinyamata amene asonkhana pamodzi; pakutinso mwamuna ndi mkazi wake adzatengedwa, pamodzi ndi okalamba amene ali ndi zaka zochuluka.
12 Ihre Häuser sollen andern zugewandt werden, Äcker und Weiber allzumal; denn ich will meine Hand ausstrecken wider die Bewohner dieses Landes, spricht der HERR.
Nyumba zawo adzazipereka kwa ena, pamodzi ndi minda yawo ndi akazi awo. Ndidzatambasula dzanja langa kukantha anthu okhala mʼdzikomo,” akutero Yehova.
13 Denn vom Kleinsten bis zum Größten trachten sie alle nach Gewinn, und vom Propheten bis zum Priester gehen sie alle mit Lügen um.
“Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, onse ali ndi dyera lofuna kupeza phindu mwa kuba; aneneri pamodzi ndi ansembe omwe, onse amachita zachinyengo.
14 Und sie heilen den Schaden der Tochter meines Volkes leichthin, indem sie sprechen: «Friede, Friede!» wo doch kein Friede ist.
Amapoletsa zilonda za anthu anga pamwamba pokha. Iwo amanena kuti, ‘Mtendere, mtendere,’ pamene palibe mtendere.
15 Schämen sollten sie sich, weil sie Greuel verübt haben; aber sie wissen nicht mehr, was sich schämen heißt, und empfinden keine Scham. Darum werden sie fallen unter den Fallenden; zur Zeit, da ich sie heimsuche, werden sie stürzen, spricht der HERR.
Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazo? Ayi, sachita manyazi ndi pangʼono pomwe; sadziwa ndi kugwetsa nkhope komwe. Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale; adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalange,” akutero Yehova.
16 Also spricht der HERR: Tretet hin an die Wege und schauet und fraget nach den Pfaden der Vorzeit, welches der gute Weg sei, und wandelt darauf, so werdet ihr Ruhe finden für eure Seelen! Sie aber sprechen: «Wir wollen ihn nicht gehen!»
Yehova akuti, “Imani pa mphambano ndipo mupenye; kumeneko ndiye kuli njira zakale, funsani kumene kuli njira yabwino. Yendani mʼmenemo, ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu. Koma inu munati, ‘Ife sitidzayenda njira imeneyo.’
17 Und ich habe Wächter über euch bestellt: Merkt doch auf den Schall der Posaune! Sie aber sprechen: «Wir wollen nicht aufmerken!»
Ine ndinakupatsani alonda oti akuyangʼanireni ndipo ndinati, ‘Imvani kulira kwa lipenga!’ koma inu munati, ‘Sitidzamvera.’
18 So höret nun, ihr Völker, und du, Gemeinde, erkenne, was unter ihnen geschieht! Höre es, Erde!
Nʼchifukwa chake imvani, inu anthu a mitundu ina; yangʼanitsitsani, inu amene mwasonkhana pano, chimene chidzawachitikire anthuwo.
19 Siehe, ich will Unheil über dieses Volk kommen lassen, die Frucht ihrer Anschläge; denn auf meine Worte achteten sie nicht, und mein Gesetz verwarfen sie.
Imvani, inu anthu okhala pa dziko lapansi, ndikubweretsa masautso pa anthu awa. Zimenezi ndi mphotho ya ntchito zawo. Iwowa sanamvere mawu anga ndipo anakana lamulo langa.
20 Was soll mir der Weihrauch von Saba und das köstliche Gewürzrohr aus fernem Lande? Eure Brandopfer mißfallen mir, und eure Schlachtopfer sind mir nicht angenehm.
Kodi pali phindu lanji ngakhale mubwere ndi lubani kuchokera ku Seba, kapena zonunkhira zina kuchokera ku dziko lakutali? Nsembe zanu zopsereza Ine sindidzalandira; nsembe zanu sizindikondweretsa.”
21 Darum spricht der HERR also: Siehe, ich will diesem Volke Steine des Anstoßes in den Weg legen, damit Väter und Kinder zugleich daran zu Fall kommen; ein Nachbar mit dem andern wird umkommen.
Choncho Yehova akuti, “Ndidzayika zokhumudwitsa pamaso pa anthu awa. Abambo ndi ana awo aamuna onse adzapunthwa ndi kugwa; anansi awo ndi abwenzi awo adzawonongeka.”
22 So spricht der HERR: Siehe, es kommt ein Volk von Norden her, und eine große Nation erhebt sich von den äußersten Enden der Erde.
Yehova akunena kuti, “Taonani, gulu lankhondo likubwera kuchokera kumpoto; mtundu wa anthu amphamvu wanyamuka kuchokera kumathero a dziko lapansi.
23 Mit Bogen und Wurfspieß sind sie bewaffnet; grausam sind sie und ohne Erbarmen. Ihr Lärmen ist wie das Brausen des Meeres, und auf Pferden reiten sie, gerüstet wie ein Mann zum Kampf wider dich, o Tochter Zion!
Atenga mauta ndi mikondo; ndi anthu ankhanza ndi opanda chifundo. Phokoso lawo lili ngati mkokomo wa nyanja. Akwera pa akavalo awo ndipo akonzekera ngati anthu ankhondo, kudzakuthirani nkhondo anthu a ku Ziyoni.”
24 Als wir von ihnen hörten, wurden unsere Hände schlaff, Angst ergriff uns, Wehen wie eine Gebärende.
A ku Ziyoni akuti “Ife tamva mbiri yawo, ndipo manja anthu alefukiratu. Nkhawa yatigwira, ndipo tikumva ululu ngati mayi pa nthawi yake yochira.
25 Gehe ja nicht aufs Feld hinaus und betritt die Straße nicht! Denn des Feindes Schwert verbreitet Schrecken ringsum.
Musapite ku minda kapena kuyenda mʼmisewu, pakuti mdani ali ndi lupanga, ndipo ponseponse anthu akuchita mantha.
26 Gürte einen Sack um dich, o Tochter meines Volkes, und wälze dich in der Asche; traure wie um einen einzigen Sohn, halte bittere Klage! Denn plötzlich wird der Verwüster über uns kommen.
Inu anthu anga, valani ziguduli ndipo gubudukani pa phulusa; lirani mwamphamvu ngati munthu wolirira mwana wake mmodzi yekha, pakuti mwadzidzidzi wowonongayo adzabwera kudzatipha.
27 Ich habe dich zum Prüfer über mein Volk bestellt, zum Goldprüfer, daß du erkennest und prüfest ihren Weg.
“Iwe Yeremiya, ndakuyika kuti ukhale choyesera zitsulo. Uwayese anthu anga monga ungayesere chitsulo kuti uwone makhalidwe awo.
28 Sie sind alle widerspenstige Empörer, gehen mit Verleumdungen um; Erz und Eisen sind sie, allesamt Verderber.
Onsewo ali ndi khalidwe lokanika ndi lowukira ndipo akunka nanena zamiseche. Iwo ndi olimba ngati mkuwa ndi chitsulo. Onse amangochita zoyipa zokhazokha.
29 Der Blasebalg schnaubt; aber aus dem Feuer kommt nur Blei, die Bösen werden doch nicht ausgeschieden!
Moto mu mvukuto ukuyaka kwambiri; mtovu watha kusungunuka ndi moto. Koma ntchito yosungunulayo sikupindula chifukwa zoyipa sizikuchokapo.
30 Darum wird man sie «verworfenes Silber» nennen, weil der HERR sie verworfen hat.
Iwo ali ngati siliva wotayidwa, chifukwa Yehova wawakana.”

< Jeremia 6 >