< 1 Mose 10 >

1 Dies ist das Geschlechtsregister der Söhne Noahs: Sem, Ham und Japhet; und nach der Sündflut wurden ihnen Kinder geboren.
Nayi mbiri ya ana a Nowa, Semu, Hamu ndi Yafeti. Ana atatuwa anabereka ana awo chitatha chigumula.
2 Die Söhne Japhets waren: Gomer, Magog, Madai, Javan, Tubal, Mesech und Tiras.
Ana aamuna a Yafeti anali: Gomeri, Magogi, Madai, Yavani, Tubala, Mesaki ndi Tirasi.
3 Die Söhne Gomers aber: Aschkenas, Riphat und Togarma.
Ana aamuna a Gomeri anali: Asikenazi, Rifati ndi Togarima.
4 Und die Söhne Javans: Elischa, Tarsis, Kittim und Rodanim.
Ana aamuna a Yavani anali: Elisa, Tarisisi, Kitimu ndi Rodanimu.
5 Sie haben sich auf die Inseln der Heiden verteilt, in ihre Länder, ein jedes nach seiner Sprache; in ihre Völkerschaften, ein jedes nach seiner Abstammung.
(Amenewa ndiwo makolo a anthu okhala mʼmphepete mwa nyanja. Awa ndi ana a Yafeti monga mwa mafuko a mu mitundu yawo, uliwonse ndi chiyankhulo chake).
6 Und dies sind die Söhne Hams: Kusch, Mizraim, Put und Kanaan.
Ana aamuna a Hamu anali: Kusi, Miziraimu, Puti ndi Kanaani.
7 Und die Söhne Kuschs: Seba, Chavila, Sabta, Raema, Sabteka und Dedan.
Ana aamuna a Kusi anali: Seba, Havila, Sabita, Raama ndi Sabiteka. Ana aamuna a Raama anali: Seba ndi Dedani.
8 Auch zeugte Kusch den Nimrod; der fing an ein Gewaltiger zu sein auf Erden.
Kusi anabereka Nimurodi amene anali wankhondo wamphamvu kwambiri pa dziko lapansi.
9 Er war ein gewaltiger Jäger vor dem HERRN; daher sagt man: Ein gewaltiger Jäger vor dem HERRN wie Nimrod.
Iye anali mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova; nʼchifukwa chake anthu ali ndi chisudzo, chakuti, “Ndiwe mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova monga Nimurodi.”
10 Und der Anfang seines Königreiches war Babel, Erek, Akkad und Kalne im Lande Sinear.
Malo oyambirira a ufumu wake anali Babeli, Ereki, Akadi ndi Kaline. Malo onsewa anali mʼdziko la Sinara.
11 Von diesem Land zog er nach Assur aus und baute Ninive, Rechobot-Ir und Kelach,
Atachoka mʼdziko limeneli anapita ku Asiriya kumene anakamanga Ninive, Rehoboti-Iri, Kala,
12 dazu Resen, zwischen Ninive und Kelach; das ist die große Stadt.
ndi Reseni, mzinda waukulu umene uli pakati pa Ninive ndi Kala.
13 Mizraim aber zeugte die Luditer, Anamiter, Lehabiter und Naphtuchiter;
Igupto ndiye kholo la Aludi, Aanami, Alehabu, Anafutu,
14 auch die Patrusiter und die Kasluchiter, von welchen die Philister und die Kaphtoriter ausgegangen sind.
Apaturusi, Akasilu ndi Akafitori (kumene kunachokera Afilisti).
15 Kanaan aber zeugte Zidon, seinen Erstgebornen und Het;
Kanaani anabereka mwana wake wachisamba, Sidoni, ndipo anaberekanso Ahiti;
16 auch die Jebusiter, Amoriter und Girgasiter;
Ayebusi, Aamori, Agirigasi;
17 die Heviter, Arkiter und Siniter;
Ahivi, Aariki, Asini,
18 die Arvaditer, Zemariter und die Chamatiter; und darnach breiteten sich die Geschlechter der Kanaaniter aus.
Aaravadi, Azemari ndi Ahamati. Pambuyo pake, mafuko a Akanaani anafalikira ponseponse,
19 Und der Kanaaniter Gebiet erstreckte sich von Zidon an bis dahin, wo man von Gerar nach Gaza kommt; desgleichen bis dahin, wo man von Sodom und Gomorra, Adama und Zeboim nach Lascha kommt.
mpaka ku malire a Kanaani. Malirewo anachokera ku Sidoni kulowa cha ku Gerari mpaka ku Gaza, ndi kulowa ku Sodomu, Gomora, Adima ndi Zeboimu mpaka ku Lasa.
20 Das sind die Söhne Hams nach ihren Geschlechtern und Sprachen, in ihren Ländern und Völkerschaften.
Amenewa ndiwo ana aamuna a Hamu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe amakhala ndi mitundu yawo.
21 Auch Sem wurden Kinder geboren, ihm, dem Vater aller Söhne Ebers, Japhets älterem Bruder.
Semu amene anali mkulu wake wa Yafeti nayenso anabereka nakhala kholo la Eberi.
22 Sems Söhne waren Elam, Assur, Arpakschad, Lud und Aram.
Ana aamuna a Semu anali: Elamu, Asuri, Aripakisadi, Ludi ndi Aramu.
23 Und Arams Söhne: Uz, Chul, Geter und Masch.
Ana aamuna a Aramu anali: Uzi, Huri, Geteri ndi Mesaki.
24 Arpakschad aber zeugte den Schelach, und Schelach zeugte den Eber.
Aripakisadi anabereka Sela, ndipo Selayo anabereka Eberi.
25 Und dem Eber wurden zwei Söhne geboren; der eine hieß Peleg, weil in seinen Tagen das Land verteilt ward; sein Bruder aber hieß Joktan.
A Eberi anabereka ana aamuna awiri: Wina anamutcha Pelegi chifukwa pa nthawiyo anthu a pa dziko lapansi anagawikana. Dzina la mʼbale wake linali Yokitani.
26 Und Joktan zeugte Almodad, Schaleph, Chazarmavet, Jarach,
Yokitani anabereka Alimodadi, Selefi, Hazari-Maveti, Yera,
27 Hadoram, Usal, Dikla,
Hadoramu, Uzali, Dikila,
28 Obal, Abimael, Scheba,
Obali, Abimaeli, Seba,
29 Ophir, Chavila und Jobad; diese alle sind Söhne Joktans.
Ofiri, Havila ndi Yobabu. Onsewa anali ana aamuna a Yokitani.
30 Und ihre Wohnsitze erstreckten sich von Mesa an, bis man gen Sephar kommt, zum östlichen Gebirge.
Chigawo chimene ankakhala chinayambira ku Mesa mpaka ku Seferi, ku dera la mapiri chakummawa.
31 Das sind die Söhne Sems nach ihren Geschlechtern und Sprachen, in ihren Ländern und Völkerschaften.
Amenewa ndiwo ana a Semu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe ankakhala ndi mitundu yawo.
32 Das sind die Geschlechter der Söhne Noahs nach ihrer Abstammung in ihren Völkern; und von ihnen haben sich nach der Sündflut die Völker auf der Erde verteilt.
Amenewa ndiwo mafuko a ana aamuna a Nowa monga mwa mibado ya mitundu yawo. Mitundu yonse ya anthu inatuluka mwa iwowa ndi kufalikira pa dziko lonse lapansi chitatha chigumula chija.

< 1 Mose 10 >