< Psalm 121 >
1 Ein Lied für Wallfahrten. Ich hebe meine Augen auf zu den Bergen:
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndikweza maso anga ku mapiri; kodi thandizo langa limachokera kuti?
2 Meine Hilfe kommt vom HERRN, der Himmel und Erde geschaffen.
Thandizo langa limachokera kwa Yehova, wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
3 Er wird deinen Fuß nicht wanken lassen; nicht schlummert dein Hüter.
Sadzalola kuti phazi lako literereke; Iye amene amakusunga sadzawodzera.
4 Nein, nicht schlummert und nicht schläft der Hüter Israels.
Taonani, Iye amene amasunga Israeli sadzawodzera kapena kugona.
5 Der HERR ist dein Hüter, der HERR dein Schatten über deiner rechten Hand,
Yehova ndiye amene amakusunga; Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.
6 daß dich bei Tage die Sonne nicht sticht, noch der Mond in der Nacht.
Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana, kapena mwezi nthawi ya usiku.
7 Der HERR behütet dich vor allem Übel, er behütet deine Seele;
Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse; adzasunga moyo wako.
8 der HERR behütet deinen Ausgang und Eingang von nun an bis in Ewigkeit.
Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako; kuyambira tsopano mpaka muyaya.