< Psalm 116 >
1 Ich liebe den HERRN, denn er hat erhört mein flehentlich Rufen;
Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
2 ja, er hat sein Ohr mir zugeneigt: ich will zu ihm rufen mein Leben lang!
Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
3 Umschlungen hatten mich des Todes Netze und die Ängste der Unterwelt mich befallen, in Drangsal und Kummer war ich geraten. (Sheol )
Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol )
4 Da rief ich den Namen des HERRN an: »Ach, HERR, errette meine Seele!«
Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
5 Gnädig ist der HERR und gerecht, und unser Gott ist voll Erbarmens;
Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
6 der HERR schützt den, der unbeirrt ihm traut: ich war schwach geworden, aber er half mir.
Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
7 Kehre zurück, meine Seele, zu deiner Ruhe, denn der HERR hat Gutes an dir getan!
Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
8 Ja, du hast mein Leben vom Tode errettet, meine Augen vom Weinen, meinen Fuß vom Anstoß;
Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
9 ich werde noch wandeln vor dem HERRN in den Landen des Lebens.
kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
10 Ich habe Glauben gehalten, wenn ich auch sagte: »Ich bin gar tief gebeugt«;
Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
11 in meiner Verzagtheit hab’ ich gesagt: »Die Menschen sind Lügner allesamt.«
Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
12 Wie soll ich dem HERRN vergelten alles, was er mir Gutes getan?
Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
13 Den Becher des Heils will ich erheben und den Namen des HERRN anrufen;
Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
14 meine Gelübde will ich bezahlen dem HERRN, ja angesichts seines ganzen Volkes.
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
15 Kostbar ist in den Augen des HERRN der Tod seiner Frommen.
Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
16 Ach, HERR, ich bin ja dein Knecht, ich bin dein Knecht, der Sohn deiner Magd; meine Bande hast du gelöst:
Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
17 dir will ich Dankopfer bringen und den Namen des HERRN anrufen;
Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
18 meine Gelübde will ich bezahlen dem HERRN, ja angesichts seines ganzen Volkes,
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
19 in den Vorhöfen am Hause des HERRN, in deiner Mitte, Jerusalem! Halleluja!
mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.