< Psalm 114 >

1 Halleluja! Als Israel aus Ägypten auszog, Jakobs Haus aus dem Volk fremder Sprache,
Pamene Israeli anatuluka mu Igupto, nyumba ya Yakobo kuchoka ku mtundu wa anthu a chiyankhulo chachilendo,
2 da ward Juda sein Heiligtum, Israel sein Herrschaftsgebiet.
Yuda anasanduka malo opatulika a Mulungu, Israeli anasanduka ufumu wake.
3 Das Meer sah es und floh, der Jordan wandte sich rückwärts,
Nyanja inaona ndi kuthawa, mtsinje wa Yorodani unabwerera mʼmbuyo;
4 die Berge hüpften wie Widder, die Hügel gleichwie Lämmer.
mapiri analumphalumpha ngati nkhosa zazimuna, timapiri ngati ana ankhosa.
5 Was war dir, o Meer, daß du flohest, dir, Jordan, daß du dich rückwärts wandtest?
Nʼchifukwa chiyani iwe unathawa? iwe mtsinje wa Yorodani unabwereranji mʼmbuyo?
6 (Was war euch) ihr Berge, daß ihr hüpftet wie Widder, ihr Hügel gleichwie Lämmer?
inu mapiri, munalumphalumphiranji ngati nkhosa zazimuna, inu timapiri, ngati ana ankhosa?
7 Vor dem Anblick des Herrn erbebe, du Erde, vor dem Anblick des Gottes Jakobs,
Njenjemera pamaso pa Ambuye iwe dziko lapansi, pamaso pa Mulungu wa Yakobo,
8 der Felsen wandelt zum Wasserteich, Kieselgestein zum sprudelnden Quell!
amene anasandutsa thanthwe kukhala chitsime, thanthwe lolimba kukhala akasupe a madzi.

< Psalm 114 >