< Psalm 105 >

1 Preiset den HERRN, ruft seinen Namen an, macht seine Taten unter den Völkern bekannt!
Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
2 Singt ihm, spielet ihm, redet von all seinen Wundern!
Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
3 Rühmt euch seines heiligen Namens! Es mögen herzlich sich freun, die da suchen den HERRN!
Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
4 Fragt nach dem HERRN und seiner Stärke, suchet sein Angesicht allezeit!
Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
5 Gedenkt seiner Wunder, die er getan, seiner Zeichen und der Urteilssprüche seines Mundes,
Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
6 ihr Kinder Abrahams, seines Knechtes, ihr Söhne Jakobs, seine Erwählten!
inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
7 Er, der HERR, ist unser Gott, über die ganze Erde ergehen seine Gerichte.
Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
8 Er gedenkt seines Bundes auf ewig, des Wortes, das er geboten auf tausend Geschlechter,
Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
9 (des Bundes) den er mit Abraham geschlossen, und des Eides, den er Isaak geschworen,
pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
10 den für Jakob er als Satzung bestätigt und für Israel als ewigen Bund,
Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
11 da er sprach: »Dir will ich Kanaan geben, das Land, das ich euch als Erbbesitztum zugeteilt!«
“Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
12 Damals waren sie noch ein kleines Häuflein, gar wenige und nur Gäste im Lande;
Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
13 sie mußten wandern von Volk zu Volk, von einem Reich zur andern Völkerschaft;
ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
14 doch keinem gestattete er, sie zu bedrücken, ja Könige strafte er ihretwillen:
Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
15 »Tastet meine Gesalbten nicht an und tut meinen Propheten nichts zuleide!«
“Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
16 Dann, als er Hunger ins Land ließ kommen und jegliche Stütze des Brotes zerbrach,
Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
17 da hatte er schon einen Mann vor ihnen her gesandt: Joseph, der als Sklave verkauft war.
Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
18 Man hatte seine Füße gezwängt in den Stock, in Eisen(-fesseln) war er gelegt,
Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
19 bis zu der Zeit, wo seine Weissagung eintraf und der Ausspruch des HERRN ihn als echt erwies.
mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
20 Da sandte der König und ließ ihn entfesseln, der Völkergebieter, und machte ihn frei;
Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
21 er bestellte ihn über sein Haus zum Herrn, zum Gebieter über sein ganzes Besitztum;
Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
22 er sollte über seine Fürsten schalten nach Belieben und seine höchsten Beamten Weisheit lehren.
kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
23 So kam denn Israel nach Ägypten, und Jakob weilte als Gast im Lande Hams.
Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
24 Da machte Gott sein Volk gar fruchtbar und ließ es stärker werden als seine Bedränger;
Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
25 er wandelte ihren Sinn, sein Volk zu hassen und Arglist an seinen Knechten zu üben.
amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
26 Dann sandte er Mose, seinen Knecht, und Aaron, den er erkoren;
Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
27 die richteten seine Zeichen unter ihnen aus und die Wunder im Lande Hams:
Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
28 Er sandte Finsternis und ließ es dunkel werden; doch sie achteten nicht auf seine Worte;
Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
29 er verwandelte ihre Gewässer in Blut und ließ ihre Fische sterben;
Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
30 es wimmelte ihr Land von Fröschen bis hinein in ihre Königsgemächer;
Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
31 er gebot, da kamen Bremsenschwärme, Stechfliegen über ihr ganzes Gebiet;
Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
32 er gab ihnen Hagelschauer als Regen, sandte flammendes Feuer in ihr Land;
Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
33 er schlug ihre Reben und Feigenbäume und zerbrach die Bäume in ihrem Gebiet;
Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
34 er gebot, da kamen die Heuschrecken und die Grillen in zahlloser Menge,
Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
35 die verzehrten alle Gewächse im Land und fraßen die Früchte ihrer Felder.
zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
36 Dann schlug er alle Erstgeburt im Lande, die Erstlinge all ihrer Manneskraft.
Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
37 Nun ließ er sie ausziehn mit Silber und Gold, und kein Strauchelnder war in seinen Stämmen;
Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
38 Ägypten war ihres Auszugs froh, denn Angst vor ihnen hatte sie befallen.
Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
39 Er breitete Gewölk aus als Decke und Feuer, um ihnen die Nacht zu erhellen;
Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
40 auf Moses Bitte ließ er Wachteln kommen und sättigte sie mit Himmelsbrot;
Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
41 er spaltete einen Felsen: da rannen Wasser und flossen durch die Steppen als Strom;
Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
42 denn er gedachte seines heiligen Wortes, dachte an Abraham, seinen Knecht.
Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
43 So ließ er sein Volk in Freuden ausziehn, unter Jubel seine Erwählten;
Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
44 dann gab er ihnen die Länder der Heiden, und was die Völker erworben, das nahmen sie in Besitz,
Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
45 auf daß sie seine Gebote halten möchten und seine Gesetze bewahrten. Halleluja!
kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.

< Psalm 105 >